< Habakuku 1 >

1 Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
Dette er det utsagn som profeten Habakuk skuet.
2 Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
Hvor lenge, Herre, skal jeg ennu rope uten at du hører! Jeg klager for dig over vold - og du frelser ikke.
3 Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
Hvorfor lar du mig skue urett, og hvorledes kan du selv se på slik elendighet? Ødeleggelse og vold har jeg for mine øine; det yppes kiv og opstår tretter.
4 Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
Derfor er loven maktesløs, og retten kommer aldri frem; for ugudelige omringer den rettferdige, derfor kommer retten frem forvendt.
5 “Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
Se eder omkring blandt folkene, se og bli forferdet, ja forferdet! For en gjerning gjør jeg i eders dager - I skulde ikke tro den når den blev fortalt.
6 Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
For se, jeg lar kaldeerne reise sig, det ville og voldsomme folk, som farer frem så vide som jorden når, for å ta i eie boliger som ikke hører det til.
7 Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
Fryktelig og forferdelig er det; fra sig selv henter det sin rett og sin høihet.
8 Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
Dets hester er raskere enn leoparder og skarpere til å springe enn ulver om aftenen; dets ryttere sprenger frem, dets ryttere kommer langt borte fra, de flyver som en ørn når den styrter sig over sitt rov.
9 onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
Alle kommer de for å gjøre voldsverk, de stirrer stridslystne fremad, og de samler fanger som sand.
10 Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
De spotter konger, og fyrster er til latter for dem; de ler av hver festning, de dynger jord op mot den og tar den.
11 Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
Så stryker de avsted som en vind og farer frem og drar skyld over sig; deres kraft er deres gud.
12 Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
Er du ikke fra fordums tid Herren min Gud, min Hellige? Vi skal ikke dø. Herre! Til å fullbyrde dom har du satt dem. Du vår klippe! Til å straffe har du gitt dem fullmakt.
13 Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
Du som er ren av øine, så du ikke kan se på ondt og ikke er i stand til å skue på elendighet! Hvorfor ser du på troløse, hvorfor tier du når den ugudelige tilintetgjør den som er rettferdigere enn han?
14 Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
Du har jo gjort med menneskene som med havets fisker, som med krypet, som ingen herre har!
15 Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
Dem alle drar de op med krok, samler dem i sin not og sanker dem i sitt garn; derfor gleder de sig og jubler.
16 Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
Derfor ofrer de til sin not og brenner røkelse for sitt garn; for de gir dem deres fete lodd og deres kraftige mat.
17 Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?
Men skal de derfor fremdeles få tømme sin not og uavlatelig slå folkeslag ihjel uten skånsel?

< Habakuku 1 >