< Habakuku 1 >

1 Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
Révélation que vit Habacuc, le prophète.
2 Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
Yahvé, jusqu'à quand vais-je crier, et tu n'écouteras pas? Je crie vers toi « Violence! » et tu ne sauveras pas?
3 Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
Pourquoi me montres-tu l'iniquité, et regardes-tu la perversité? Car la destruction et la violence sont devant moi. Il y a des querelles, et la dispute s'élève.
4 Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
C'est pourquoi la loi est paralysée, et la justice ne prévaut jamais; car les méchants entourent les justes; c'est pourquoi la justice sort pervertie.
5 “Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
« Regardez parmi les nations, observez, et soyez étonnés; car je fais en vos jours une œuvre que vous ne croirez pas, même si on vous la raconte.
6 Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
Car voici, je fais surgir les Chaldéens, cette nation âpre et hâtive qui marche sur toute la largeur de la terre, pour posséder des demeures qui ne sont pas à elle.
7 Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
Ils sont craints et redoutés. Leur jugement et leur dignité viennent d'eux-mêmes.
8 Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
Leurs chevaux sont plus rapides que les léopards, Et plus féroces que les loups du soir. Leurs cavaliers avancent fièrement. Oui, leurs cavaliers viennent de loin. Ils volent comme l'aigle qui se précipite pour dévorer.
9 onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
Ils viennent tous pour la violence. Leurs hordes sont tournées vers l'avant. Ils rassemblent les prisonniers comme du sable.
10 Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
Ils se moquent des rois, Et les princes sont pour eux une dérision. Ils se moquent de toute forteresse, car ils construisent une rampe de terre et la prennent.
11 Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
Puis ils passent comme le vent et s'en vont. Ils sont vraiment coupables, eux dont la force est leur dieu. »
12 Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
N'es-tu pas de toute éternité, Yahvé mon Dieu, mon Saint? Nous ne mourrons pas. Yahvé, tu les as établis pour juger. Toi, Rocher, tu l'as établi pour punir.
13 Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
Toi qui as des yeux plus purs que ceux qui voient le mal, et qui ne peux regarder la perversité, pourquoi tolères-tu les perfides et te tais-tu quand le méchant engloutit celui qui est plus juste que lui,
14 Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
et rend les hommes semblables aux poissons de la mer, aux reptiles qui n'ont pas de maître sur eux?
15 Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
Il les prend tous avec l'hameçon. Il les attrape dans son filet et les recueille dans sa gibecière. C'est pourquoi il se réjouit et se réjouit.
16 Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
C'est pourquoi il sacrifie à son filet et brûle de l'encens à sa drague, parce que grâce à eux sa vie est luxueuse et sa nourriture est bonne.
17 Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?
Videra-t-il donc continuellement son filet, Et tuera-t-il les nations sans pitié?

< Habakuku 1 >