< Habakuku 1 >

1 Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
The prophecy which Habakkuk the prophet foresaw.
2 Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
How long, O Lord, have I entreated [thee], and thou wouldst not hear? [how long] shall I cry out unto thee [because of] violence, and thou wilt not save?
3 Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
Why wilt thou let me see wickedness, and wilt look on trouble, and the robbery and violence [that are] before me: while there is strife, and contention lifteth up [its head]?
4 Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
Therefore is the law powerless, and justice cometh not forth victorious; for the wicked encompasseth about the righteous; therefore doth justice come forth perverted.
5 “Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
Look ye about among the nations, and behold and be astonished and astounded; for [God] will fulfill a work in your days, ye would not believe it, if it were only told you.
6 Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
For, lo, I will raise up the Chaldeans, that bitter and impetuous nation, that march to the wide spaces of the earth to conquer dwelling-places that are not theirs.
7 Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
Terrible and dreadful are they: from themselves go forth their judicial laws and their dignity.
8 Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
And swifter than leopards are their horses, and fiercer than the evening wolves; and their horsemen spread themselves abroad: and their horsemen will come from afar; they will fly like the eagle hastening to eat.
9 onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
They all will come for violence: the front of their faces is like the east wind, and they gather captives as the sand.
10 Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
And they will make sport with kings, and princes will be a play unto them: at every strong-hold will they laugh, and they will cast up earth-mounds and capture it.
11 Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
Then doth their spirit become arrogant, and they are surpassingly proud, and offend, [imputing] this their power unto their god.
12 Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
Art thou not from everlasting, O Lord my God, my Holy One? we shall not die. O Lord, thou hast ordained them for judgment; and, O Protector, thou hast appointed them to correct [nations].
13 Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
Thou, who art too pure of eyes to behold evil, and canst not look on trouble, wherefore wilt thou look upon those that deal treacherously, be silent when the wicked swalloweth up him that is more righteous than he?
14 Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
And [why] makest thou men as the fishes of the sea, as the creeping things, that have no ruler over them?
15 Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
All of them he bringeth up with the angle, he draggeth them up in his net, and gathereth them in his drag: therefore he rejoiceth and is glad.
16 Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
Therefore he sacrificeth unto his net, and burneth incense unto his drag; because through them is his portion fat, and his food marrowy.
17 Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?
Shall he therefore [always] empty his net, and continually slay nations without sparing?

< Habakuku 1 >