< Habakuku 3 >

1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
Молитва пророка Авакума, для співу на струнному при́ладі:
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
„Господи, зві́стку Твою я почув та й злякався! Господи, оживи Своє ді́ло в сере́дині років, у сере́дині літ об'яви́, у гніві про милість згада́й!
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
Бог іде від Теману, і Святий від Парану гори. (Се́ла) Ве́лич Його́ вкрила небо, і слави Його́ стала повна земля!
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
А сяйво було́, наче со́няшне світло, промі́ння при боці у Нього, і там укриття́ Його поту́ги.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Перед обличчям Його́ морови́ця іде, а по сто́пах Його пнеться по́лум'я.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
Став, — і землю Він змі́ряв, поглянув — і наро́ди затряс, — і попа́дали го́ри дові́чні, вікові́ похили́лись узгі́р'я. Путі Його вічні.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
Я бачив наме́ти Куша́на під кривдою, тремтять покрива́ла мідія́нського кра́ю.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Чи на рі́ки, о Господи, Ти запала́в, чи на рі́ки Твій гнів? Чи Твоє пересе́рдя на море, що їздиш на ко́нях Своїх, на спасе́нних Своїх колесни́цях?
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
Лук твій голий, наги́й, напо́внений стріл сагайда́к. (Се́ла) Ти рі́чками землю розсі́к.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
Тебе вгледівши, го́ри дрижали, водяна́ течія́ потекла́, безо́дня свій голос дала́, зняла ви́соко руки свої.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
Сонце й місяць спини́лися в мешка́нні своє́му при світлі Твоїх стріл, що літають при ся́йві блискучого спи́са Твого́.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
У лю́ті ступав Ти землею, у гніві людей молоти́в.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
Ти вийшов спасти Свій наро́д, спасти Помазанця Свого́. Ти з дому безбожного го́лову збив, обнажи́в Ти основу по шию. (Се́ла)
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
Ти пробив його спи́сами го́лову кня́зя його́, як вони підняли́сь, щоб мене розпоро́шити; вони ті́шилися, немов мали поже́рти тає́мно убогого.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
Ти кі́ньми Своїми по мо́рю топта́в, по во́дній великій грома́ді.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
Я почув — і затремтіла утро́ба моя, задзвені́ли на голос цей гу́би мої, гнили́зна ввійшла́ в мої ко́сті, і тремчу́ я на місці своїм, бо маю чекати в споко́ї день у́тиску, коли при́йде наро́д, який має на вас наступа́ти.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
Коли б фі́ґове дерево не зацвіло́, і не було́ б урожа́ю в виноградниках, обмани́ло зайня́ття оливкою, а поле ї́жі не вродило б, позникала отара з коша́ри і не стало б в обо́рах худоби, —
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
то я Го́сподом ті́шитись буду й тоді́, раді́тиму Богом спасі́ння свого́!
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
Бог Госпо́дь — моя сила, і чи́нить Він но́ги мої, як у ла́ні, і во́дить мене по висо́тах!“Для дириґента хору на моїх стру́нних знаря́ддях.

< Habakuku 3 >