< Habakuku 3 >

1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
Молитва пророка Авакума; за певање.
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
Господе, чух реч Твоју, и уплаших се; Господе, дело своје усред година сачувај у животу, усред година објави га, у гневу сети се милости.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
Бог дође од Темана и Светац с горе Фарана; слава Његова покри небеса и земља се напуни хвале Његове.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
Светлост Му беше као сунце, зраци излажаху Му из руку, и онде беше сакривена сила Његова.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Пред Њим иђаше помор, и живо угљевље иђаше испод ногу Његових.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
Стаде, и измери земљу, погледа и разметну народе, распадоше се вечне горе, слегоше се хумови вечни; путеви су Му вечни.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
Видех шаторе етиопске у муци, устрепташе завеси земљи мадијанској.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Еда ли се на реке разгневи Господ? Еда ли се на реке распали гнев Твој? На море јарост Твоја, кад си појездио на коњима својим и на колима својим за спасење?
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
Помоли се лук Твој као што си се заклео племенима; раздро си земљу за реке.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
Видеше Те горе и уздрхташе, поводањ навали; бездана пусти глас свој, увис подиже руке своје.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
Сунце и месец стадоше у стану свом, идоше према светлости Твоје стреле, према севању сјајног копља Твог.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
Срдито си ишао по земљи, гневно си газио народе.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
Изашао си на спасење народу свом, на спасење с помазаником својим; размрскао си главу кући безбожничкој до врата откривши темељ.
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
Његовим копљима пробио си главу селима његовим кад наваљиваху као вихор да ме разаспу, радоваху се као да ће прождрети сиромаха у потаји.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
Ишао си по мору на коњима својим, по гомили многе воде.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
Чух, и утроба се моја усколеба, усне ми уздрхташе на глас, у кости ми уђе трулеж, и устресох се на месту свом; како ћу почивати у дан невоље, кад дође на народ који ће га опустошити.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
Јер смоква неће цвасти, нити ће бити рода на лози виновој; род ће маслинов преварити, и њиве неће дати хране, оваца ће нестати из тора, и говеда неће бити у обору.
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
Али ћу се ја радовати у Господу, веселићу се у Богу спасења свог.
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
Господ је Господ сила моја, и даће ми ноге као у кошуте, и водиће ме по висинама мојим. Начелнику певачком уз жице моје.

< Habakuku 3 >