< Habakuku 3 >

1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
Une prière du prophète Habacuc, sur une musique victorieuse.
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
Yahvé, j'ai entendu parler de ta renommée. Je suis en admiration devant tes actes, Yahvé. Renouvelez votre travail au milieu des années. Au milieu des années, faites-le savoir. Dans la colère, tu te souviens de la miséricorde.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
Dieu est venu de Teman, le Saint du mont Paran. (Selah) Sa gloire a couvert les cieux, et sa louange a rempli la terre.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
Sa splendeur est comme le lever du soleil. Des rayons brillent de sa main, où son pouvoir est caché.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
La peste l'a précédé, et la peste suivaient ses pas.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
Il se tint debout, et il fit trembler la terre. Il a regardé, et a fait trembler les nations. Les anciennes montagnes se sont effondrées. Les collines séculaires se sont effondrées. Ses voies sont éternelles.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
J'ai vu les tentes de Cushan dans la détresse. Les habitations du pays de Madian ont tremblé.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Les fleuves ont-ils déplu à Yahvé? était votre colère contre les rivières, ou ta colère contre la mer, que vous avez monté sur vos chevaux, sur tes chars de salut?
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
Tu as découvert ton arc. Tu as appelé tes flèches assermentées. (Selah) Tu as fendu la terre avec des rivières.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
Les montagnes t'ont vu, et elles ont eu peur. La tempête des eaux est passée. L'abîme a rugi et a levé les mains en l'air.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
Le soleil et la lune étaient immobiles dans le ciel. à la lumière de tes flèches pendant qu'ils partaient, à l'éclat de votre lance étincelante.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
Tu as parcouru le pays avec fureur. Tu as battu les nations dans la colère.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
Tu es sorti pour le salut de ton peuple, pour le salut de tes oints. Tu as écrasé la tête du pays de la méchanceté. Vous les avez déshabillés de la tête aux pieds. (Selah)
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
Tu as percé la tête de ses guerriers avec leurs propres lances. Ils sont venus comme un tourbillon pour me disperser, jubilant comme pour dévorer les malheureux en secret.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
Tu as foulé la mer avec tes chevaux, le barattage des eaux puissantes.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
J'ai entendu, et mon corps a tremblé. Mes lèvres ont frémi à la voix. La pourriture entre dans mes os, et je tremble à ma place. car je dois attendre tranquillement le jour de la détresse, pour l'arrivée des gens qui nous envahissent.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
Car même si le figuier ne fleurit pas, ni de fruits dans les vignes, le travail de l'olive échoue, les champs ne produisent pas de nourriture, les troupeaux sont coupés du bercail, et il n'y a pas de troupeau dans les stalles,
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
Mais je me réjouirai en Yahvé. Je serai joyeux dans le Dieu de mon salut!
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
Yahvé, l'Éternel, est ma force. Il rend mes pieds comme des pieds de cerf, et me permet d'aller dans les hautes sphères. Pour le directeur musical, sur mes instruments à cordes.

< Habakuku 3 >