< Habakuku 3 >
1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
A prayer of Habakkuk the prophet, [set] on shigionoth:
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
O YHWH, I heard your report, I have been afraid, O YHWH, Your work! In midst of years revive it, In the midst of years You make known, In anger You remember mercy.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
God comes from Teman, The Holy One from Mount Paran. (Pause) His splendor has covered the heavens, And His praise has filled the earth.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
And the brightness is as the light, He has rays out of His hand, And there—the hiding of His strength.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
Before Him goes pestilence, And a burning flame goes forth at His feet.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
He has stood, and He measures earth, He has seen, and He shakes off nations, And mountains of antiquity scatter themselves, The hills of old have bowed, The ways of old [are] His.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
Under sorrow I have seen tents of Cushan, Curtains of the land of Midian tremble.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Has YHWH been angry against rivers? Against rivers [is] Your anger? [Is] Your wrath against the sea? For You ride on Your horses—Your chariots of salvation.
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
You make Your bow utterly naked, The tribes have sworn, saying, (Pause) You cleave the earth [with] rivers.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
Seen You—pained are mountains, An inundation of waters has passed over, The deep has given forth its voice, It has lifted up its hands high.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
Sun—moon—has stood—a habitation, Your arrows go on at the light, At the brightness, the glittering of Your spear.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
In indignation You tread earth, In anger You thresh nations.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
You have gone forth for the salvation of Your people, For salvation with Your Anointed, You have struck the head of the house of the wicked, Laying bare the foundation to the neck. (Pause)
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
You have pierced the head of his leaders with his own rods, They are tempestuous to scatter me, Their exultation [is] as to consume the poor in secret.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
You have proceeded through the sea with Your horses—the clay of many waters.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
I have heard, and my belly trembles, At the noise have my lips quivered, Rottenness comes into my bones, And in my place I tremble, That I rest for a day of distress, At the coming up of the people, he overcomes it.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
Though the fig tree does not flourish, And there is no produce among vines, The work of the olive has failed, And fields have not yielded food, The flock has been cut off from the fold, And there is no herd in the stalls,
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
Yet I, in YHWH I exult, I am joyful in the God of my salvation.
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
YHWH the Lord [is] my strength, And He makes my feet like does, And causes me to tread on my high-places. To the overseer with my stringed instruments!