< Habakuku 3 >
1 Pemphero la mneneri Habakuku potsata mayimbidwe a Sigionoti.
Profet Habakkuk e ratoumnae, Shigionoth la.
2 Inu Yehova, ndamva za kutchuka kwanu; Inu Yehova, ntchito zanu zandiopsa. Muzichitenso masiku athu ano, masiku athu ano zidziwike; mu ukali wanu mukumbukire kuchita chifundo.
Oe BAWIPA kai ni na lawk ka thai teh ka taki toe. Atu e kumnaw dawk na thaw tawk e a kamnue teh ka hmu toe. Na lungkhuek ei nakunghai, na lungmanae teh na pahnim hoeh.
3 Mulungu anabwera kuchokera ku Temani, Woyerayo kuchokera ku Phiri la Parani. (Sela) Ulemerero wake unaphimba mlengalenga ndipo dziko lapansi linadzaza ndi matamando ake.
Cathut teh Teiman kho hai thoseh, Tami Kathoung teh Paran koehoi thoseh, a tho. Bawilennae ni kalvan a ramuk teh, a bawilennae ni talai van akawi.
4 Kuwala kwa ulemerero wake kunali ngati kutuluka kwa dzuwa; kunyezimira kunkatuluka mʼdzanja lake, mʼmene anabisamo mphamvu zake.
A meilam teh kanî patetlah ao. A kut dawk kaawm e a bahu teh a raeng lah a tâco.
5 Patsogolo pake pankagwa mliri; nthenda yoopsa inkagwa kumbuyo kwake.
A hmalah runae ni a cei teh, a hnuklah patawnae ni a kâbang.
6 Iye anayimirira ndi kugwedeza dziko lapansi; anayangʼana ndipo mitundu ya anthu inanjenjemera. Mapiri okhazikika anagumuka ndipo zitunda zakalekale zinatitimira. Njira zake ndi zachikhalire.
A kangdue teh talaipui a bangnue. A khet nah miphunnaw a tâlueng awh. Ayan e monnaw ni a kâbawng awh teh, kacakpounge monruinaw a tip awh. Hatei, Bawipa teh a lamthung dawk poe a cei.
7 Ndinaona matenti a ku Kusani ali pa mavuto, mokhala a ku Midiyani muli ululu waukulu.
Kushan ram dawk e rimnaw ni roedengnae a kâhmo awh teh, Midian ram dawk e yaphninaw a kâhuet e hah ka hmu.
8 Inu Yehova, kodi munakwiyira mitsinje? Kodi munakalipira timitsinje? Kodi munapsera mtima nyanja pamene munakwera pa akavalo anu ndiponso magaleta anu achipulumutso?
Oe BAWIPA, Nang ni rungngangnae rangleng na kâcui nahanelah, tuipuinaw koe na lungkhuek na maw. Tuipui hoi na kâtaran maw.
9 Munasolola uta wanu mʼchimake, munayitanitsa mivi yambiri. (Sela) Munagawa dziko lapansi ndi mitsinje;
Nang ni catounnaw koe lawkkam na tâ e patetlah lilava coungkacoe na rasa sin toe, talai dawk tuinaw na phuek sak toe.
10 mapiri anakuonani ndipo anagwedezeka. Madzi amphamvu anasefukira; nyanja yozama inakokoma ndipo mafunde ake anakwera kwambiri.
Monnaw ni BAWIPA a hmu awh navah a kâhuet awh. Ka poum e tuinaw ni muen a ramuk. Tuipuinaw ni a hram awh teh a kut a dâw awh.
11 Dzuwa ndi mwezi zinayima chilili mlengalenga, pa kungʼanima kwa mivi yanu yowulukayo, pa kunyezimira kwa mkondo wanu.
Kanî hoi thapa ni amamae hmuen dawk ao awh. Ahnimae a angnae dawk pala ni a cei teh, a raeng dawk tahroe hai sumpa lah a palik.
12 Munayendayenda mʼdziko lapansi muli ndi ukali, ndipo munapondereza mitundu ya anthu muli ndi mkwiyo.
A lungkhuek laihoi ram pueng dawk a cei teh, a lungkhueknae ni miphunnaw hah koung a coungroe.
13 Munapita kukalanditsa anthu anu, kukapulumutsa wodzozedwa wanu. Munakantha mtsogoleri wa dziko la anthu oyipa, munawononga anthu ake onse. (Sela)
Bawipa e a taminaw rungngangnae hanelah na tho teh, satui na awi e naw rungngang hanlah na tho. Tami kalan hoeh e im teh imthungkhu koehoi rep na kanawi pouh teh a carawng koe totouh na raphoe pouh.
14 Ndi mkondo wake womwe munalasa mtsogoleri wake pamene ankhondo ake anabwera mwamphamvu kudzatibalalitsa, ankasangalala ngati kuti akudzawononga osauka amene akubisala.
Ransabawinaw e a lû hah palanaw hoi pawkkayawng lah a ka pouh. Ahnimouh teh kaimouh palek sak hanelah tûilî kathout patetlah a tho awh. Mathoenaw kei hanelah a lunghawi awh.
15 Munapondaponda pa nyanja ndi akavalo anu, kuvundula madzi amphamvu.
Bawipa nang ni marangnaw na kâcui teh athakaawme tuicapa lungui na cei.
16 Ndinamva ndipo mtima wanga unagunda kwambiri, milomo yanga inanjenjemera pakumva phokosolo; mafupa anga anaguluka, ndipo mawondo anga anawombana. Komabe ndikuyembekezera mofatsa, tsiku la masautso limene lidzafike pa mtundu wa anthu umene ukutithira nkhondo.
Na pâpho lawk ka thai navah ka lung a tâlueng, ka kam ka cakuep, ka hru a hmawn, ka takbuem a pâyaw. Bangkongtetpawiteh, runae hnin, kathetkung ni miphunnaw a tuknae tueng totouh ka o han rah.
17 Ngakhale mtengo wa mkuyu usachite maluwa, ndipo mipesa ikhale yopanda mphesa. Ngakhale mitengo ya olivi isabereke zipatso, ndipo mʼminda musatuluke kanthu. Ngakhale nkhosa ndi ngʼombe zithe mʼkhola,
Thaibunglung kung ni pei hoeh, Misurkung paw hoeh, olivekung hai ngaihawi hane awm hoeh. law dawk hai apawhik paw hoeh, tu takha dawk tu kathup niteh, maito im dawk maito kaawm hoeh nakunghai.
18 komabe ine ndidzakondwera mwa Yehova, ndidzasangalala mwa Mulungu Mpulumutsi wanga.
Cathut dawk ka lung ahawi teh na ka rungngangnae Cathut kâuep lahoi ka lung ahawi han.
19 Ambuye Yehova ndiye mphamvu yanga; amalimbitsa miyendo yanga ngati ya mbawala yayikazi, amandithandiza kukafika pamwamba pa phiri. Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Pa zoyimbira za nsambo.
Bawipa Jehovah teh kaie ka thaonae doeh, ka khok teh sayuk khok patetlah a coung sak teh, ka rasang e hmuen na poe han.