< Habakuku 2 >

1 Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
На стражи моей стану, и взыду на камень, и посмотрю еже видети, что возглаголет во мне и что отвещаю на обличение мое.
2 Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
И отвеща Господь ко мне и рече: впиши видение, и яве на дске, яко да постигнет читаяй я.
3 Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
Зане еще видение на время, и просияет в конец, а не вотще: аще умедлит, потерпи ему, яко идый приидет и не умедлит.
4 “Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
Аще усумнится, не благоволит душа моя в нем: праведник же (мой) от веры жив будет.
5 Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
Презорливый же и обидливый муж и величавый ничесоже скончает: иже разшири аки ад душу свою, и сей яко смерть ненасыщен: и соберет к себе вся языки и приимет к себе вся люди. (Sheol h7585)
6 “Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Не сия ли вся на него притчу приимут и гадание в повесть его? И рекут: горе умножающему себе не сущая его, доколе? И отягчающему узу свою тяжце.
7 Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
Яко внезапу востанут угрызающии его, и ободрятся наветницы твои, и будеши в разграбление им.
8 Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Понеже ты пленил еси страны многи, пленят тя вси оставшии людие крове ради человечи и нечестия земли и града и всех живущих на ней.
9 “Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
Горе лихоимствующым лихоимство злое дому своему, еже учинити на высоте гнездо свое, еже исторгнути от руки злых.
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
Умыслил еси стыдение дому своему, скончал еси люди многи, и согреши душа твоя.
11 Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
Зане камень из стены возопиет, и хрущь от древа возглаголет сия:
12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
у, люте созидающему град кровьми и уготовляющему град неправдами.
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
Не сия ли суть от Господа Вседержителя? И оскудеша людие мнози огнем, и языцы мнози изнемогоша:
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
яко наполнится вся земля ведения славы Господни, якоже вода многа в мори покрыет я.
15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
Горе напаяющему подруга своего развращением мутным, и упоявающему, яко да взирает к пещерам их.
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
Сытость безчестия от славы испий и ты: сердце, поколеблися и сотряснися: обыде о тебе чаша десницы Господни, и собрася безчестие на главу твою.
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Занеже нечестие Ливаново покрыет тя, и страсть зверей престрашит тя, крове ради человечи и нечестия земли и града и всех живущих на ней.
18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
Что пользует изваяное, яко изваяша е? Создаша слияние, мечтание ложное, яко упова создавый на создание свое, сотворити кумиры немыя.
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
У, люте глаголющему ко древу: ободрися, востани: и камению: возвысися: и то есть мечтание, и сие есть скование злата и сребра, и всякаго духа несть в нем.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”
Господь же во храме святем Своем: да убоится от лица Его вся земля.

< Habakuku 2 >