< Habakuku 2 >
1 Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
Je veux me tenir dans mon donjon et me placer sur la tour et observer pour voir ce qu'il me dira et ce que je répliquerai en sus de mon grief.
2 Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
Et l'Éternel me répondit et dit: Écris la vision et la grave sur des tables, afin que couramment on la lise.
3 Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
Car la vision a trait à un temps à venir, mais elle aspire au but, et ne mentira pas; si elle tarde, attends-la, car elle arrivera, elle n'y manquera pas.
4 “Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
Voici, son âme s'est enflée, elle n'est pas droite en lui, mais le juste par sa foi vivra.
5 Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol )
Oui, le vin est insolent, l'homme qu'il enorgueillit n'a point de repos; pareil à l'Enfer, il ouvre une large bouche, et il est comme la mort, et insatiable, et il s'empare de tous les peuples et accapare toutes les nations. (Sheol )
6 “Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Toutes ne diront-elles pas sur lui une chanson et des railleries et des sarcasmes, parlant ainsi: Malheur à qui accumulait ce qui n'était pas à lui! jusques à quand?… et à qui se chargeait d'emprunts à gages!
7 Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
Ne se lèveront-ils pas soudain, tes créanciers, et ne s'éveilleront-ils pas, tes oppresseurs? Et tu seras leur proie.
8 Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Parce que tu pillas des peuples nombreux, tous les autres peuples te pilleront, à cause du meurtre des hommes et de l'outrage fait au pays, aux villes et à tous leurs habitants.
9 “Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
Malheur à qui fait un gain inique pour sa maison, afin de placer son nid sur la hauteur pour se dérober au bras du malheur!
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
Tu décidas l'opprobre de ta maison, la destruction des peuples nombreux, et tu as péché contre toi-même.
11 Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
Car de la muraille la pierre crie, et de la charpente la poutre lui répond.
12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
Malheur à qui bâtit une ville avec le sang, et fonde une ville avec l'iniquité!
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
Voici, n'est-ce pas de par l'Éternel des armées que les peuples se fatiguent pour un feu, et les nations se peinent pour le néant?
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
Car la terre se remplira de la connaissance de la gloire de l'Éternel, de même que les eaux recouvrent la mer.
15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
Malheur à qui fait boire son prochain! à toi qui lui verses le feu de ton vin et l'enivres pour voir sa nudité!
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
Tu seras rassasié d'opprobre au lieu de gloire; bois aussi toi-même et découvre ton prépuce! qu'elle arrive à toi la coupe de la droite de l'Éternel, et que l'ignominie couvre ta gloire!
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Car la violence faite au Liban retombera sur toi, ainsi que la ruine des bêtes qu'elle épouvanta, à cause du meurtre des hommes et de la violence faite au pays, à la ville et a tous ses habitants.
18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
A quoi sert l'idole, pour que le sculpteur la taille? la statue et le docteur de mensonges, pour que le sculpteur se confie en sa sculpture en faisant des idoles muettes?
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
Malheur à qui dit au bois: « Éveille-toi! » « Lève-toi! » à la pierre muette, « qu'elle enseigne! » Voici, elle est plaquée d'or et d'argent, et il n'y a point d'esprit au dedans d'elle.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”
Mais l'Éternel est dans son temple saint! Que toute la terre se taise devant lui!