< Habakuku 2 >

1 Ndidzakhala pa malo anga aulonda, ndi kuyima pa mitumbira ya nkhondo; ndidzadikira kuti ndimve zimene Iye adzandiwuze, ndi yankho limene ndidzapatsidwe pa madandawulo anga.
Je me tiendrai à ma garde et je me placerai sur les remparts, et je regarderai pour voir ce qu'il me dira, et ce que je répondrai au sujet de ma plainte.
2 Tsono Yehova anandiyankha, nati: “Lemba masomphenyawa ndipo uwalembe mooneka bwino pa mapale kuti wowerenga awawerenge mosavuta.
Yahvé me répondit: « Écris la vision, et mets-la en évidence sur des tablettes, afin que celui qui court puisse la lire.
3 Pakuti masomphenyawa akudikira nthawi yake; masomphenyawa akunena zamʼtsogolo ndipo sizidzalephera kuchitika. Ngakhale achedwe kukwaniritsidwa, uwayembekezere; zidzachitika ndithu ndipo sadzachedwa.
Car la vision est encore pour le temps fixé, et elle se hâte vers la fin, et ne se démentira pas. Même si elle prend du temps, attendez-la, car elle viendra sûrement. Elle ne tardera pas.
4 “Taona, mdani wadzitukumula; zokhumba zake sizowongoka, koma wolungama adzakhala ndi moyo mwachikhulupiriro.
Voici, son âme s'enfle d'orgueil. Il n'est pas droit en lui, mais le juste vivra par sa foi.
5 Ndithu, wasokonezeka ndi vinyo; ndi wodzitama ndiponso wosakhazikika. Pakuti ngodzikonda ngati manda, ngosakhutitsidwa ngati imfa, wadzisonkhanitsira mitundu yonse ya anthu ndipo wagwira ukapolo anthu a mitundu yonse. (Sheol h7585)
Oui, de plus, le vin est perfide: un homme arrogant qui ne reste pas chez lui, qui élargit son désir comme le séjour des morts; il est comme la mort et ne peut être satisfait, mais il rassemble à lui toutes les nations et entasse à lui tous les peuples. (Sheol h7585)
6 “Kodi onse ogwidwawo sadzamunyoza ndi kumunyogodola ponena kuti, “Tsoka kwa amene amadzikundikira katundu amene si wake ndipo amadzilemeretsa ndi chuma cholanda! Kodi izi zidzachitika mpaka liti?
Tous ne prendront-ils pas contre lui une parabole et un proverbe de raillerie, et ne diront-ils pas: « Malheur à celui qui augmente ce qui ne lui appartient pas, et qui s'enrichit par l'extorsion! ». Jusqu'à quand? »
7 Kodi angongole ako sadzakuwukira mwadzidzidzi? Kodi sadzadzuka ndi kukuchititsa mantha? Pamenepo iwe udzalandidwa kalikonse.
Tes débiteurs ne vont-ils pas se lever soudainement, réveiller ceux qui te font trembler, et tu seras leur victime?
8 Pakuti unafunkha mitundu yambiri ya anthu, mitundu ina imene inatsala idzakufunkha iweyo. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Parce que tu as pillé de nombreuses nations, tout le reste des peuples te pillera à cause du sang des hommes, des violences faites au pays, à la ville et à tous ceux qui l'habitent.
9 “Tsoka kwa amene amalemera ndi chuma chochipeza mwachinyengo, kukweza malo ake okhalapo, kuthawa mavuto!
Malheur à celui qui obtient un mauvais gain pour sa maison, afin de placer son nid en haut, afin d'être délivré de la main du malheur!
10 Wakonzekera kuwononga mitundu yambiri ya anthu, kuchititsa manyazi nyumba yako yomwe ndi kuwononga moyo wako.
Tu as conçu la honte de ta maison en exterminant de nombreux peuples, et tu as péché contre ton âme.
11 Mwala pa khoma udzafuwula, ndipo mitanda ya matabwa idzavomereza zimenezi.
Car la pierre criera de la muraille, et la poutre de la charpente y répondra.
12 “Tsoka kwa amene amanga mzinda pokhetsa magazi ndi kukhazikitsa mzinda pochita zoyipa!
Malheur à celui qui bâtit une ville par le sang, et qui affermit une cité par l'iniquité!
13 Kodi Yehova Wamphamvuzonse sanatsimikize kuti ntchito za anthu zili ngati nkhuni pa moto, ndi kuti mitundu ya anthu imadzitopetsa popanda phindu?
Voici, n'est-ce pas de la part de l'Éternel des armées que les peuples travaillent pour le feu, et que les nations se fatiguent pour la vanité?
14 Pakuti dziko lapansi lidzadzaza ndi chidziwitso cha ulemerero wa Yehova, monga momwe madzi amadzazira nyanja.
Car la terre sera remplie de la connaissance de la gloire de l'Éternel, comme les eaux couvrent la mer.
15 “Tsoka kwa amene amamwetsa anzake zakumwa zoledzeretsa, kutsanula mʼbotolo mpaka ataledzera, kuti aone umaliseche wawo.
« Malheur à celui qui donne à boire à son prochain, en versant votre vin brûlant jusqu'à ce qu'ils soient ivres, afin que vous puissiez contempler leurs corps nus!
16 Udzachita manyazi mʼmalo mokhala ndi ulemerero. Tsopano ino ndi nthawi yako! Imwa mpaka umaliseche wako uwonekere! Chikho chochokera mʼdzanja lamanja la Yehova chikubwera kwa iwe, ndipo manyazi adzaphimba ulemerero wako.
Vous êtes remplis de honte, et non de gloire. Vous aussi, vous boirez et serez exposés! La coupe de la main droite de Yahvé se retournera contre vous, et l'opprobre couvrira votre gloire.
17 Udzathedwa nzeru ndi chiwawa chimene unachita ku Lebanoni, ndiponso udzachita mantha ndi nyama zimene unaziwononga. Pakuti wakhetsa magazi a anthu; wawononga mayiko ndi mizinda ndi aliyense wokhala mʼmenemo.
Car la violence faite au Liban vous accablera, et la destruction des animaux vous terrifiera, à cause du sang des hommes et de la violence faite au pays, à chaque ville et à ceux qui y habitent.
18 “Kodi fano lili ndi phindu lanji, poti analisema ndi munthu, kapena chifanizo chimene chimaphunzitsa mabodza? Pakuti munthu amene walipanga amakhulupirira ntchito ya manja ake; amapanga mafano amene samatha kuyankhula.
« Quelle valeur a l'image gravée, pour que son créateur l'ait gravée; l'image fondue, pour que celui qui en façonne la forme s'y fie, pour fabriquer des idoles muettes?
19 Tsoka kwa amene amawuza mtengo kuti, ‘Khala wamoyo!’ Kapena mwala wopanda moyo kuti, ‘Dzuka!’ Kodi zimenezi zingathe kulangiza? Ndi zokutidwa ndi golide ndi siliva; mʼkati mwake mulibe mpweya.
Malheur à celui qui dit au bois: « Réveille-toi! » ou à la pierre muette: « Lève-toi! ». Est-ce là un enseignement? Voici, elle est recouverte d'or et d'argent, et il n'y a en elle aucun souffle.
20 Koma Yehova ali mʼNyumba yake yopatulika; dziko lonse lapansi likhale chete pamaso pake.”
Mais Yahvé est dans son temple saint. Que toute la terre se taise devant lui! »

< Habakuku 2 >