< Habakuku 1 >
1 Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.
The burden that Habacuc the prophet saw.
2 Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani, koma wosayankha? Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!” koma wosatipulumutsa?
How long, O Lord, shall I cry, and thou wilt not hear? shall I cry out to thee suffering violence, and thou wilt not save?
3 Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa? Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa? Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa; pali ndewu ndi kukangana kwambiri.
Why hast thou shewn me iniquity and grievance, to see rapine and injustice before me? and there is a judgment, but opposition is more powerful.
4 Kotero malamulo anu atha mphamvu, ndipo chilungamo sichikugwira ntchito. Anthu oyipa aposa olungama, kotero apotoza chilungamo.
Therefore the law is torn in pieces, and judgment cometh not to the end: because the wicked prevaileth against the just, therefore wrong judgment goeth forth.
5 “Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani, ndipo muthedwe nazo nzeru. Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu zimene inu simudzazikhulupirira, ngakhale wina atakufotokozerani.
Behold ye among the nations, and see: wonder, and be astonished: for a work is done in your days, which no man will believe when it shall be told.
6 Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni, anthu ankhanza ndiponso amphamvu, amene amapita pa dziko lonse lapansi kukalanda malo amene si awo.
For behold, I will raise up the Chaldeans, a bitter and swift nation, marching upon the breadth of the earth, to possess the dwelling places that are not their own.
7 Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa; amadzipangira okha malamulo ndi kudzipezera okha ulemu.
They are dreadful, and terrible: from themselves shall their judgment, and their burden proceed.
8 Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo. Okwerapo awo akuthamanga molunjika; a pa akavalo awo ndi ochokera kutali, akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;
Their horses are lighter than leopards, and swifter than evening wolves; and their horsemen shall be spread abroad: for their horsemen shall come from afar, they shall fly as an eagle that maketh haste to eat.
9 onse akubwera atakonzekera zachiwawa. Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.
They shall all come to the prey, their face is like a burning wind: and they shall gather together captives as the sand.
10 Akunyoza mafumu ndiponso kuchitira chipongwe olamulira. Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa; akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.
And their prince shall triumph over kings, and princes shall be his laughingstock: and he shall laugh at every strong hold, and shall cast up a mount, and shall take it.
11 Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe, anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”
Then shall his spirit be changed, and he shall pass, and fall: this is his strength of his god.
12 Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire? Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa. Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo; Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.
Wast thou not from the beginning, O Lord my God, my holy one, and we shall not die? Lord, thou hast appointed him for judgment: and made him strong for correction.
13 Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa; Inu simulekerera cholakwa. Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa? Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?
Thy eyes are too pure to behold evil, and thou canst not look on iniquity. Why lookest thou upon them that do unjust things, and holdest thy peace when the wicked devoureth the man that is more just than himself?
14 Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja, ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.
And thou wilt make men as the fishes of the sea, and as the creeping things that have no ruler.
15 Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza, amawakola mu ukonde wake, amawasonkhanitsa mu khoka lake; kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.
He lifted up all them with his hook, he drew them in his drag, and gathered them into his net: for this he will be glad and rejoice.
16 Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake ndiponso kufukizira lubani khoka lake, popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.
Therefore will he offer victims to his drag, and he will sacrifice to his net: because through them his portion is made fat, and his meat dainty.
17 Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo, kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?
For this cause therefore he spreadeth his net, and will not spare continually to slay the nations.