+ Genesis 1 >
1 Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
No início, Deus criou os céus e a terra.
2 Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
A terra estava sem forma e vazia. A escuridão estava na superfície das profundezas e o Espírito de Deus pairava sobre a superfície das águas.
3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
Deus disse: “Que haja luz”, e houve luz.
4 Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
Deus viu a luz, e viu que ela era boa. Deus dividiu a luz das trevas.
5 Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
Deus chamou a luz de “dia”, e a escuridão de “noite”. Havia a noite e havia a manhã, o primeiro dia.
6 Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
Deus disse: “Que haja uma extensão no meio das águas, e que ela divida as águas das águas”.
7 Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
Deus fez a extensão, e dividiu as águas que estavam sob a extensão das águas que estavam acima da extensão; e assim foi.
8 Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
Deus chamou a vastidão de “céu”. Havia a noite e havia a manhã, um segundo dia.
9 Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
Deus disse: “Que as águas sob o céu sejam reunidas num só lugar, e que a terra seca apareça;” e assim foi.
10 Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Deus chamou a terra seca de “terra”, e a reunião das águas ele chamou de “mares”. Deus viu que era bom.
11 Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
Deus disse: “Que a terra produza grama, ervas que produzam sementes, e árvores frutíferas que dêem frutos depois de sua espécie, com suas sementes dentro dela, na terra;” e assim foi.
12 Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
A terra produziu grama, ervas produzindo sementes depois de sua espécie, e árvores dando frutos, com suas sementes dentro dela, depois de sua espécie; e Deus viu que era boa.
13 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
Havia a noite e havia a manhã, um terceiro dia.
14 Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
Deus disse: “Que haja luzes na extensão do céu para dividir o dia da noite; e que sejam para que os sinais marquem as estações, os dias e os anos;
15 zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
e que sejam para que as luzes na extensão do céu dêem luz sobre a terra;” e assim foi.
16 Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
Deus fez as duas grandes luzes: a luz maior para governar o dia, e a luz menor para governar a noite. Ele também fez as estrelas.
17 Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
Deus as colocou na vastidão do céu para dar luz à terra,
18 kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
e para governar o dia e a noite, e para dividir a luz da escuridão. Deus viu que era bom.
19 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
Havia a noite e havia a manhã, um quarto dia.
20 Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
Deus disse: “Deixem as águas transbordar de seres vivos, e deixem as aves voar sobre a terra na extensão aberta do céu”.
21 Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Deus criou as grandes criaturas marinhas e todos os seres vivos que se movem, com os quais as águas transbordaram, depois de sua espécie, e cada ave alada depois de sua espécie. Deus viu que era bom.
22 Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
Deus os abençoou, dizendo: “Sede fecundos e multiplicai-vos, e enchei as águas dos mares, e deixai as aves multiplicarem-se na terra”.
23 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
Havia a noite e havia a manhã, um quinto dia.
24 Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
Deus disse: “Que a terra produza seres vivos segundo sua espécie, gado, coisas rastejantes e animais da terra segundo sua espécie”; e assim foi.
25 Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Deus fez os animais da terra depois de sua espécie, e o gado depois de sua espécie, e tudo o que rasteja no solo depois de sua espécie. Deus viu que era bom.
26 Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
Deus disse: “Vamos fazer o homem à nossa imagem, à nossa semelhança”. Que tenham domínio sobre os peixes do mar, e sobre as aves do céu, e sobre o gado, e sobre toda a terra, e sobre cada coisa rasteira que se arrepia sobre a terra”.
27 Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
Deus criou o homem à sua própria imagem. À imagem de Deus ele o criou; macho e fêmea ele os criou”.
28 Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
Deus os abençoou. Deus lhes disse: “Sede fecundos, multiplicai-vos, enchei a terra e sujeitai-a”. Tenham domínio sobre os peixes do mar, sobre as aves do céu e sobre todo ser vivo que se move sobre a terra”.
29 Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
Deus disse: “Eis que vos dei toda erva que dá semente, que está na superfície de toda a terra, e toda árvore que dá fruto que dá semente”. Será seu alimento”.
30 Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
A cada animal da terra, e a cada ave do céu, e a tudo que rasteja na terra, na qual há vida, eu dei toda erva verde para alimento”; e assim foi.
31 Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.
Deus viu tudo o que tinha feito e, eis que era muito bom. Havia a noite e havia a manhã, um sexto dia.