+ Genesis 1 >

1 Pachiyambi Mulungu analenga kumwamba ndi dziko lapansi.
Ekuqaleni uNkulunkulu wadala amazulu lomhlaba.
2 Dziko lapansi linali losakonzedwa ndi lopanda kanthu. Mdima wandiweyani unakuta nyanja ndipo Mzimu wa Mulungu unkayendayenda pamwamba pa madziwo.
Njalo umhlaba wawungelasimo ungelalutho, lobumnyama babuphezu kokujula; loMoya kaNkulunkulu wayendiza phezu kwamanzi.
3 Pamenepo Mulungu anati, “Kuwale” ndipo kunawaladi.
UNkulunkulu wasesithi: Kakube khona ukukhanya; kwasekusiba khona ukukhanya.
4 Mulungu anaona kuti kuwalako kunali bwino ndipo Iye analekanitsa kuwala ndi mdima.
UNkulunkulu wasebona ukukhanya ukuthi kuhle; uNkulunkulu wasesehlukanisa phakathi kokukhanya lobumnyama.
5 Mulungu anatcha kuwalako “usana” ndipo mdima anawutcha “usiku.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku loyamba.
UNkulunkulu wasebiza ukukhanya ngokuthi yimini, lobumnyama wabubiza ngokuthi yibusuku. Kwasekusiba yikuhlwa, njalo kwaba yikusa, usuku lokuqala.
6 Kenaka Mulungu anati, “Pakhale thambo pakati pa madzi kuti lilekanitse madzi a mʼmwamba ndi madzi a pansi.”
UNkulunkulu wasesithi: Kakube khona umkhathi phakathi kwamanzi; kawehlukanise phakathi kwamanzi lamanzi.
7 Ndipo Mulungu anapanga thambo nalekanitsa madzi amene anali pansi ndi pamwamba pa thambo lija, ndipo zinachitikadi.
UNkulunkulu wasesenza umkhathi, wasesehlukanisa phakathi kwamanzi angaphansi komkhathi lamanzi aphezu komkhathi; kwasekusiba njalo.
8 Mulungu anatcha thambo lija “kumwamba.” Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachiwiri.
UNkulunkulu wasebiza umkhathi ngokuthi ngamazulu. Kwasekusiba yikuhlwa, njalo kwaba yikusa, usuku lwesibili.
9 Mulungu anati, “Madzi a pansi pa thambo asonkhane pa malo amodzi kuti mtunda uwoneke,” ndipo zinachitikadi.
UNkulunkulu wasesithi: Kakuqoqelwe amanzi avela ngaphansi kwamazulu ndawonye, njalo kakubonakale umhlabathi owomileyo; kwasekusiba njalo.
10 Mulungu anawutcha mtundawo “dziko,” madzi osonkhana pamodziwo anawatcha “nyanja.” Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
UNkulunkulu wasebiza umhlabathi owomileyo ngokuthi ngumhlaba, lenhlangano yamanzi wayibiza ngokuthi zinlwandle. UNkulunkulu wasebona ukuthi kuhle.
11 Kenaka Mulungu anati, “Dziko libereke zomera zobala mbewu, mitengo yobala zipatso za mbewu, molingana ndi mitundu yake.” Ndipo zinachitikadi.
UNkulunkulu wasesithi: Umhlaba kawumilise utshani, imibhida ethela inhlanyelo, isihlahla sesithelo sisenza isithelo ngohlobo lwaso, onhlanyelo yaso ikuso phezu komhlaba. Kwasekusiba njalo.
12 Dziko linabereka zomera zokhala ndi mbewu monga mwa mitundu yake ndi mitengo yokhala ndi zipatso za mbewu mʼkati mwake monga mwa mitundu yake. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
Umhlaba wasuveza utshani, imibhida ethela inhlanyelo ngohlobo lwayo, lesihlahla sisenza isithelo, esinhlanyelo yaso ikuso ngohlobo lwaso. UNkulunkulu wasebona ukuthi kuhle.
13 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachitatu.
Kwasekusiba yikuhlwa, njalo kwaba yikusa, usuku lwesithathu.
14 Mulungu anati, “Pakhale zowunikira kuthambo kuti zilekanitse usana ndi usiku. Ndipo zimenezi zikhale zizindikiro zoonetsa nyengo, masiku ndi zaka;
UNkulunkulu wasesithi: Kakube khona izikhanyiso emkhathini wamazulu, ukuze zehlukanise phakathi kwemini lobusuku; njalo zibe yizibonakaliso lezikhathi ezimisiweyo, lensuku leminyaka.
15 zikhale kuthambo kuti ziwunikire pa dziko lapansi. Ndipo zinachitikadi.”
Njalo zibe yizikhanyiso emkhathini wamazulu, ukuze zikhanyise emhlabeni. Kwasekusiba njalo.
16 Mulungu anapanga zowunikira zazikulu ziwiri; chachikulu chilamulire usana ndi chachingʼono chilamulire usiku. Iye anapanganso nyenyezi.
UNkulunkulu wasesenza izikhanyiso ezimbili ezinkulu: Isikhanyiso esikhulu ukuze sibuse imini, lesikhanyiso esincinyane ukuze sibuse ubusuku, kanye lezinkanyezi.
17 Mulungu anaziyika mlengalenga kuti ziziwunikira pa dziko lapansi,
UNkulunkulu wasezimisa emkhathini wamazulu, ukuthi zikhanyise emhlabeni,
18 kuti zilamulire usana ndi usiku, ndi kuti zilekanitse kuwala ndi mdima. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
lokuthi zibuse emini lebusuku, lokwehlukanisa phakathi kokukhanya lobumnyama. UNkulunkulu wasebona ukuthi kuhle.
19 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachinayi.
Kwasekusiba yikuhlwa, njalo kwaba yikusa, usuku lwesine.
20 Mulungu anati, “Mʼmadzi mukhale zamoyo zochuluka ndipo mbalame ziwuluke mlengalenga pamwamba pa dziko lapansi.”
UNkulunkulu wasesithi: Amanzi kawagcwale ukunyakazela kwemiphefumulo ephilayo, njalo kakuphaphe inyoni phezu komhlaba emkhathini wamazulu.
21 Choncho Mulungu analenga zamoyo zikuluzikulu za mʼnyanja ndi chamoyo chamtundu uliwonse chokhala mʼmadzi ndi mbalame iliyonse ya mapiko monga mwa mtundu wake. Mulungu anaona kuti zinali bwino.
UNkulunkulu wasedala oququmadevu bolwandle abakhulu, laso sonke isidalwa esiphilayo esibhinqikayo, amanzi agcwele sona, ngohlobo lwaso, layo yonke inyoni elempiko, ngohlobo lwayo. UNkulunkulu wasebona ukuthi kuhle.
22 Mulungu anazidalitsa nati, “Muswane, ndi kudzaza mʼmadzi a mʼnyanja, ndipo mbalame zichuluke pa dziko lapansi.”
UNkulunkulu wasekubusisa, esithi: Zalani, lande, njalo ligcwalise amanzi enlwandle, lezinyoni kazande emhlabeni.
23 Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa pa tsiku lachisanu.
Kwasekusiba yikuhlwa, njalo kwaba yikusa, usuku lwesihlanu.
24 Kenaka Mulungu anati, “Dziko lapansi litulutse zolengedwa zamoyo monga mwa mitundu yawo: ziweto, zolengedwa zokwawa ndi nyama zakuthengo, iliyonse monga mwa mtundu wake.” Ndipo zinaterodi.
UNkulunkulu wasesithi: Umhlaba kawuveze izidalwa eziphilayo ngohlobo lwazo, izifuyo lokuhuquzelayo lenyamazana zomhlaba ngenhlobo zazo. Kwasekusiba njalo.
25 Mulungu anapanga nyama zakuthengo monga mwa mitundu yawo, nyama zoweta monga mwa mitundu yawo ndi nyama zokwawa monga mwa mitundu yawo. Ndipo Mulungu anaona kuti zinali bwino.
UNkulunkulu wasesenza izinyamazana zomhlaba ngenhlobo zazo, lezifuyo ngenhlobo zazo, lakho konke okuhuquzelayo komhlaba ngenhlobo zakho. UNkulunkulu wasebona ukuthi kuhle.
26 Zitatha izi Mulungu anati, “Tipange munthu mʼchifanizo chathu, mofanana ndi ife kuti alamulire nsomba za mʼnyanja, mbalame zamlengalenga, nyama zonse zoweta ndi zonse zokwawa za pa dziko lapansi ndi zamoyo zonse zakutchire.”
UNkulunkulu wasesithi: Asenze abantu ngomfanekiso wethu, ngesimo sethu, njalo babuse phezu kwenhlanzi zolwandle, laphezu kwenyoni zamazulu, laphezu kwezifuyo, laphezu komhlaba wonke, laphezu kwakho konke okuhuquzelayo lokho okuhuquzela emhlabeni.
27 Ndipo Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake. Anawalengadi mʼchifanizo cha Mulungu; analenga iwo, mwamuna ndi mkazi.
UNkulunkulu wasemdala umuntu ngomfanekiso wakhe; wamdala ngomfanekiso kaNkulunkulu; owesilisa lowesifazana wabadala.
28 Mulungu anawadalitsa nati kwa iwo, “Muberekane, muchulukane, mudzaze dziko lapansi ndipo muligonjetse. Mulamulire nsomba zamʼnyanja, mbalame zamlengalenga ndi cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimayenda mokwawa pa dziko lapansi.”
UNkulunkulu wasebabusisa, uNkulunkulu wasesithi kibo: Zalani lande, ligcwalise umhlaba njalo liwehlisele phansi; libuse phezu kwenhlanzi zolwandle, laphezu kwenyoni zamazulu, laphezu kwakho konke okuphilayo okuhuquzela emhlabeni.
29 Kenaka Mulungu anati, “Ine ndakupatsani chomera chilichonse cha pa dziko lapansi chimene chili ndi mbewu komanso mtengo uliwonse wobala zipatso zokhala ndi mbewu mʼkati mwake kuti zikhale chakudya chanu.
UNkulunkulu wasesithi: Khangelani, ngilinike yonke imibhida ethela inhlanyelo, esebusweni bomhlaba wonke, laso sonke isihlahla, okukuso isithelo sesihlahla esithela inhlanyelo; kini singesokudla.
30 Ndaperekanso msipu kwa nyama zonse za pa dziko lapansi ndi kwa mbalame zamlengalenga ndi kwa cholengedwa chamoyo chilichonse chimene chimakwawa, chilichonse chimene chili ndi moyo.” Ndipo zinachitikadi.
Njalo kuyo yonke inyamazana yomhlaba, lakuyo yonke inyoni yamazulu, lakukho konke okuhuquzela emhlabeni, okukukho umoya ophilayo, lonke uhlaza ngolokudla. Kwasekusiba njalo.
31 Mulungu anaona zonse zimene anazilenga kuti zinali zabwino kwambiri. Ndipo panali madzulo ndiponso mmawa, tsiku lachisanu ndi chimodzi.
UNkulunkulu wasebona konke akwenzileyo; khangela-ke kwakukuhle kakhulu. Kwasekusiba yikuhlwa, njalo kwaba yikusa, usuku lwesithupha.

+ Genesis 1 >