< Genesis 9 >

1 Ndipo Mulungu anadalitsa Nowa ndi ana ake aamuna nati kwa iwo, “Berekanani ndipo muchulukane ndi kudzaza dziko lapansi.
And God blessed Noah and his sons, and said unto them: 'Be fruitful and multiply, and replenish the earth.
2 Nyama zonse za dziko lapansi, ndi mbalame zonse za mlengalenga, ndi chamoyo chilichonse chokwawa, ndiponso nsomba zonse za ku nyanja; zidzakuopani ndipo ndazipereka kuti muzilamulire.
And the fear of you and the dread of you shall be upon every beast of the earth, and upon every fowl of the air, and upon all wherewith the ground teemeth, and upon all the fishes of the sea: into your hand are they delivered.
3 Tsopano chamoyo chilichonse chidzakhala chakudya chanu. Monga momwe ndinakupatsirani ndiwo zamasamba, tsopano ndikupatsaninso nyama iliyonse.
Every moving thing that liveth shall be for food for you; as the green herb have I given you all.
4 “Koma musamadye nyama imene ikanali ndi magazi oyenda.
Only flesh with the life thereof, which is the blood thereof, shall ye not eat.
5 Aliyense wopha munthu adzaphedwa, nyama iliyonse yopha munthu idzaphedwa, munthu aliyense wopha munthu mnzake, adzaphedwa.
And surely your blood of your lives will I require; at the hand of every beast will I require it; and at the hand of man, even at the hand of every man's brother, will I require the life of man.
6 “Aliyense wopha munthu, adzaphedwanso ndi munthu; pakuti Mulungu analenga munthu mʼchifanizo chake.
Whoso sheddeth man's blood, by man shall his blood be shed; for in the image of God made He man.
7 Inu muberekane ndi kuchulukana kuti mudzaze dziko lonse lapansi ndi kuligonjetsa.”
And you, be ye fruitful, and multiply; swarm in the earth, and multiply therein.'
8 Mulungu anawuza Nowa ndi ana ake kuti,
And God spoke unto Noah, and to his sons with him, saying:
9 “Tsopano Ine ndapangana ndi iwe ndi zidzukulu zako zamʼtsogolomo,
'As for Me, behold, I establish My covenant with you, and with your seed after you;
10 pamodzi ndi zamoyo zonse, mbalame, ziweto ndi nyama zonse za kuthengo, ndi zonse zimene zinatuluka mʼchombo pamodzi ndi iwe.
and with every living creature that is with you, the fowl, the cattle, and every beast of the earth with you; of all that go out of the ark, even every beast of the earth.
11 Pangano langa ndi ili: Ine ndilonjeza kuti sindidzawononganso zamoyo ndi madzi a chigumula. Chigumula sichidzawononganso dziko lapansi.”
And I will establish My covenant with you; neither shall all flesh be cut off any more by the waters of the flood; neither shall there any more be a flood to destroy the earth.'
12 Ndipo Mulungu anati, “Ine ndikupereka chizindikiro ichi cha pangano langa la pakati pa Ine ndi iwe, ana ako, zamoyo zonse, pamodzi ndi mibado ya mʼtsogolo.
And God said: 'This is the token of the covenant which I make between Me and you and every living creature that is with you, for perpetual generations:
13 Ndayika utawaleza wanga mʼmitambo, ndipo chidzakhala chizindikiro cha pangano langa ndi dziko lapansi.
I have set My bow in the cloud, and it shall be for a token of a covenant between Me and the earth.
14 Nthawi zonse pakakhala mitambo mu mlengalenga ndipo utawaleza uwoneka,
And it shall come to pass, when I bring clouds over the earth, and the bow is seen in the cloud,
15 ndizikumbukira pangano langa pakati pa Ine ndi inu ndi zolengedwa zonse. Madzi sadzakhalanso chigumula chowononga dziko lapansi.
that I will remember My covenant, which is between Me and you and every living creature of all flesh; and the waters shall no more become a flood to destroy all flesh.
16 Utawaleza ukamadzaoneka mʼmitambo, ndidzawuona ndi kukumbukira pangano losatha pakati pa Mulungu ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And the bow shall be in the cloud; and I will look upon it, that I may remember the everlasting covenant between God and every living creature of all flesh that is upon the earth.'
17 Choncho Mulungu anati kwa Nowa, “Ichi ndiye chizindikiro cha pangano limene ndalichita pakati pa Ine ndi zamoyo zonse pa dziko lapansi.”
And God said unto Noah: 'This is the token of the covenant which I have established between Me and all flesh that is upon the earth.'
18 Ana aamuna a Nowa amene anatuluka mʼchombo muja anali Semu, Hamu ndi Yafeti. Hamu anali abambo ake a Kanaani.
And the sons of Noah, that went forth from the ark, were Shem, and Ham, and Japheth; and Ham is the father of Canaan.
19 Ana aamuna a Nowa amenewa ndiwo anali makolo a anthu onse pa dziko lapansi.
These three were the sons of Noah, and of these was the whole earth overspread.
20 Nowa anali munthu woyamba kulima munda wamphesa.
And Noah the husbandman began, and planted a vineyard.
21 Tsiku lina pamene Nowa anamwako vinyo wa zipatso za mʼmundawo analedzera ndipo anavula zovala zake zonse ndi kugona mu tenti yake ali maliseche.
And he drank of the wine, and was drunken; and he was uncovered within his tent.
22 Hamu, abambo ake a Kanaani ataona kuti abambo ake ali maliseche anakawuza abale ake awiri aja omwe anali panja.
And Ham, the father of Canaan, saw the nakedness of his father, and told his two brethren without.
23 Koma Semu ndi Yafeti anatenga chofunda nachiyika pa mapewa awo; ndipo anayenda chamʼmbuyo naphimba umaliseche wa abambo awo. Anafulatira kuti asaone umaliseche wa abambo awo.
And Shem and Japheth took a garment, and laid it upon both their shoulders, and went backward, and covered the nakedness of their father; and their faces were backward, and they saw not their father's nakedness.
24 Nowa atadzuka, kuledzera kutatha, ndikudziwa zimene mwana wake wamngʼono wamwamuna uja anamuchitira,
And Noah awoke from his wine, and knew what his youngest son had done unto him.
25 anati, “Atembereredwe Kanaani! Adzakhala kapolo wa pansi kwenikweni kwa abale ake.”
And he said: Cursed be Canaan; a servant of servants shall he be unto his brethren.
26 Anatinso, “Atamandike Yehova, Mulungu wa Semu! Kanaani akhale kapolo wa Semu.
And he said: Blessed be the LORD, the God of Shem; and let Canaan be their servant.
27 Mulungu akulitse dziko la Yafeti; Yafeti alandire madalitso pamodzi ndi Semu, ndipo Kanaani akhale kapolo wawo.”
God enlarge Japheth, and he shall dwell in the tents of Shem; and let Canaan be their servant.
28 Chitatha chigumula, Nowa anakhala ndi moyo zaka 350.
And Noah lived after the flood three hundred and fifty years.
29 Anamwalira ali ndi zaka 950.
And all the days of Noah were nine hundred and fifty years; and he died.

< Genesis 9 >