< Genesis 8 >

1 Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
А Бог се опомену Ноја и свих звери и све стоке што беху с њим у ковчегу; и посла Бог ветар на земљу да узбије воду.
2 Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
И затворише се извори бездану и уставе небеске, и дажд с неба престаде.
3 Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
И стаде вода опадати на земљи, и једнако опадаше после сто педесет дана;
4 ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
Те се устави ковчег седмог месеца дана седамнаестог на планини Арарату.
5 Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
И вода опадаше све већма до десетог месеца; и првог дана десетог месеца показаше се врхови од брда.
6 Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
А после четрдесет дана отвори Ноје прозор на ковчегу, који беше начинио;
7 natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
И испусти гаврана, који једнако одлеташе и долеташе докле не пресахну вода на земљи.
8 Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
Па пусти и голубицу да би видео је ли опала вода са земље.
9 Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
А голубица не нашавши где би стала ногом својом врати се к њему у ковчег, јер још беше вода по свој земљи; и Ноје пруживши руку ухвати је и узе к себи у ковчег.
10 Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
И почека још седам дана, па опет испусти голубицу из ковчега.
11 Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
И пред вече врати се к њему голубица, и гле, у кљуну јој лист маслинов, који беше откинула; тако позна Ноје да је опала вода са земље.
12 Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
Али почека још седам дана, па опет испусти голубицу, а она му се више не врати.
13 Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
Шест стотина прве године века Нојевог први дан првог месеца усахну вода на земљи; и Ноје откри кров на ковчегу, и угледа земљу суву.
14 Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
А другог месеца двадесет седмог дана беше сва земља сува.
15 Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
Тада рече Бог Ноју говорећи:
16 “Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
Изађи из ковчега ти и жена твоја и синови твоји и жене синова твојих с тобом;
17 Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
Све звери што су са тобом од сваког тела, птице и стоку и шта год гамиже по земљи, изведи са собом, нека се разиђу по земљи, и нека се плоде и множе на земљи.
18 Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
И изиђе Ноје и синови његови и жена његова и жене синова његових с њим.
19 Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
Све звери, све ситне животиње, све птице и све што се миче по земљи по својим врстама изиђоше из ковчега.
20 Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
И начини Ноје жртвеник Господу, и узе од сваке чисте стоке и од свих птица чистих, и принесе на жртвенику жртве паљенице.
21 Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
И Господ омириса мирис угодни, и рече у срцу свом: Нећу више клети земље с људи, што је мисао срца човечијег зла од малена; нити ћу више убијати све што живи, као што учиних.
22 “Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”
Од сада докле буде земље, неће нестајати сетве ни жетве, студени ни врућине, лета ни зиме, дана ни ноћи.

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark