< Genesis 8 >

1 Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
UNkulunkulu wasemkhumbula uNowa, lakho konke okuphilayo, laso sonke isifuyo, esasilaye emkhunjini. UNkulunkulu wavunguzisa umoya phezu komhlaba, lamanzi etsha.
2 Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
Kwasekumiswa imithombo yokujula lamasango empophoma zamazulu, lezulu elivela emazulwini lanqandwa.
3 Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
Lamanzi etsha esuka emhlabeni, ehamba ebuyela; amanzi asencipha ekupheleni kwensuku ezilikhulu lamatshumi amahlanu.
4 ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
Umkhumbi wasuhlala ngenyanga yesikhombisa, ngosuku lwetshumi lesikhombisa lwenyanga, phezu kwezintaba zeArarathi.
5 Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
Lamanzi aya esetsha kwaze kwaba senyangeni yetshumi; ngeyetshumi ngosuku lokuqala lwenyanga kwabonakala ingqonga zezintaba.
6 Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
Kwasekusithi ekupheleni kwensuku ezingamatshumi amane, uNowa wasevula iwindi lomkhumbi ayelenzile,
7 natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
wasethuma iwabayi, lazulazula njalo, aze atsha amanzi emhlabeni.
8 Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
Wasethuma ijuba lisuka kuye, ukubona ukuthi amanzi asemalutshwana yini ebusweni bomhlaba;
9 Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
kodwa ijuba kalitholanga indawo yokuphumula kwengaphansi yonyawo lwalo, ngakho labuyela kuye emkhunjini, ngoba amanzi ayekhona ebusweni bomhlaba wonke. Waseselula isandla sakhe, walithatha, walingenisa kuye emkhunjini.
10 Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
Waselinda futhi ezinye izinsuku eziyisikhombisa; wasephinda elithuma ijuba lisuka emkhunjini.
11 Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
Ijuba laselibuya kuye ngesikhathi santambama, khangela-ke, ihlamvu lomhlwathi elisanda ukuquntwa lalisemlonyeni walo; ngakho uNowa wasesazi ukuthi amanzi asemalutshwana phezu komhlaba.
12 Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
Waselinda futhi ezinye insuku eziyisikhombisa; waselithuma ijuba; kalabe lisabuyela kuye futhi.
13 Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
Kwasekusithi ngomnyaka wamakhulu ayisithupha lanye, ngenyanga yokuqala, ngolokuqala lwenyanga, amanzi atsha emhlabeni. UNowa wasesusa isifulelo somkhumbi, wabona, khangela-ke, ubuso bomhlaba babomile.
14 Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
Njalo ngenyanga yesibili, ngosuku lwamatshumi amabili lesikhombisa lwenyanga, umhlaba wawusuwomile.
15 Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
UNkulunkulu wasekhuluma kuNowa, esithi:
16 “Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
Phuma emkhunjini, wena lomkakho lamadodana akho labafazi bamadodana akho kanye lawe.
17 Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
Konke okuphilayo okulawe, kuyo yonke inyama, eyenyoni leyesifuyo leyakho konke okuhuquzelayo kuhuquzela emhlabeni, phuma lakho; ukuze kuzale kwande emhlabeni, kuzale, kwande phezu komhlaba.
18 Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
UNowa wasephuma, lamadodana akhe, lomkakhe, labafazi bamadodana akhe kanye laye.
19 Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
Yonke inyamazana, konke okuhuquzelayo, layo yonke inyoni, konke okuhamba emhlabeni, ngenhlobo zakho, kwaphuma emkhunjini.
20 Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
UNowa waseyakhela iNkosi ilathi; wathatha kuso sonke isifuyo esihlambulukileyo, lakuyo yonke inyoni ehlambulukileyo, wanikela umnikelo wokutshiswa phezu kwelathi.
21 Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
INkosi yasisizwa uqhatshi olumnandi; iNkosi yasisithi enhliziyweni yayo: Kangisayikuphinda ngiqalekise umhlaba ngenxa yomuntu, ngoba ukuceba kwenhliziyo yomuntu kubi kusukela ebutsheni bakhe; futhi kangisayikuphinda ngitshaye konke okuphilayo njengalokhu ngenzile.
22 “Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”
Ngazo zonke izinsuku zomhlaba, ukuhlanyela lokuvuna, lamakhaza lokukhudumala, lehlobo lobusika, lemini lobusuku, kakuyikuphela.

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark