< Genesis 8 >
1 Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
Puis, Dieu se souvint de Noé, et de toutes les bêtes fauves, et de tous les bestiaux, et de tous les oiseaux, et de tous les reptiles qui étaient avec lui dans l'arche. Il fit souffler un vent sur la terre, et l'eau céda.
2 Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
Les sources de l'abîme furent fermées, ainsi que les cataractes du ciel, et la pluie du ciel cessa.
3 Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
L'eau qui fuyait sur la terre s'affaissa, et diminua après cent cinquante jours.
4 ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
Et, le vingt-septième jour de la septième lune, l'arche s'arrêta sur le mont Ararat.
5 Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
Or, l'eau diminua jusqu'à la dixième lune, et, le premier jour de la dixième lune, les cimes des montagnes apparurent.
6 Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
Après quarante jours, Noé ouvrit la porte de l'arche qu'il avait faite,
7 natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
Et fit partir un corbeau, qui, étant sorti, ne revint plus, même après que l'eau se fut desséchée sur la terre.
8 Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
Après lui, Noé envoya une colombe pour voir si l'eau s'était retirée de la terre.
9 Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
Mais la colombe, n'ayant point trouvé où poser ses pieds, revint auprès de lui dans l'arche, parce que l'eau était sur toute la surface de la terre. Et, ayant étendu la main, il la prit et l'introduisit auprès de lui dans l'arche.
10 Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
Puis, après avoir attendu sept jours encore, il fit de nouveau partir de l'arche la colombe.
11 Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
Et sur le soir la colombe revint près de lui, tenant en son bec un brin de branche et une feuille d'olivier. Noé reconnut alors que l'eau s'était retirée de la terre.
12 Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
Et après avoir attendu encore sept jours, il fit de nouveau partir la colombe, qui ne revint plus auprès de lui.
13 Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
Or, l'an six cent un de la vie de Noé, le premier jour de la première lune, l'eau disparut sur la terre. Et Noé ouvrit le toit de l'arche qu'il avait faite et vit que l'eau s'était retirée de la face de la terre
14 Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
Et, le vingt-septième jour de la seconde lune, la terre se trouva sèche.
15 Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
Et le Seigneur Dieu parla à Noé, disant:
16 “Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
Sors de l'arche avec ta femme, et tes fils, et les femmes de tes fils, et toutes les bêtes fauves qui sont auprès de toi,
17 Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
Et toute chair, depuis les oiseaux jusqu'aux bestiaux; fais aussi sortir tout reptile se traînant à terre; et croissez et multipliez.
18 Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
Noé sortit donc avec sa femme, et ses fils, et les femmes de ses fils;
19 Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
Et toutes les bêtes fauves, et tous les bestiaux, et tout oiseau, et tout reptile se traînant à terre, selon leurs espèces, sortirent avec lui.
20 Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
Et Noé éleva un autel au Seigneur; puis il prit de tous les bestiaux purs, et de tous les oiseaux purs, et il en offrit sur l'autel un holocauste au Seigneur.
21 Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
Et le Seigneur Dieu respira un parfum délicieux. Et le Seigneur Dieu, ayant réfléchi, dit: Je ne veux plus maudire la terre à cause des œuvres des hommes, parce que l'esprit de l'homme, dès sa jeunesse, se complaît dans le mal. Je ne veux donc plus frapper toute chair vivante, comme je l'ai fait.
22 “Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”
Tous les jours de la terre, les semailles et la moisson, le froid et l'ardente chaleur, l'automne et le printemps, ne se reposeront jamais plus, ni jour ni nuit.