< Genesis 8 >

1 Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
Then God remembered Noah, and all living things, and all the cattle, which were with him in the ark, and he brought a wind across the earth, and the waters were diminished.
2 Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
And the fountains of the abyss and the floodgates of heaven were closed. And the rain from heaven was restrained.
3 Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
And the waters were restored to their coming and going from the earth. And they began to diminish after one hundred and fifty days.
4 ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
And the ark rested in the seventh month, on the twenty-seventh day of the month, upon the mountains of Armenia.
5 Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
Yet in truth, the waters were departing and decreasing until the tenth month. For in the tenth month, on the first day of the month, the tips of the mountains appeared.
6 Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
And when forty days had passed, Noah, opening the window that he had made in the ark, sent forth a raven,
7 natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
which went forth and did not return, until the waters were dried up across the earth.
8 Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
Likewise, he sent forth a dove after him, in order to see if the waters had now ceased upon the face of the earth.
9 Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
But when she did not find a place where her foot might rest, she returned to him in the ark. For the waters were upon the whole earth. And he extended his hand and caught her, and he brought her into the ark.
10 Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
And then, having waited a further seven days, he again sent forth the dove out of the ark.
11 Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
And she came to him in the evening, carrying in her mouth an olive branch with green leaves. Noah then understood that the waters had ceased upon the earth.
12 Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
And nevertheless, he waited another seven days. And he sent forth the dove, which no longer returned to him.
13 Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
Therefore, in the six hundred and first year, in the first month, on the first day of the month, the waters were diminished upon the earth. And Noah, opening the cover of the ark, gazed out and saw that the surface of the earth had become dry.
14 Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
In the second month, on the twenty-seventh day of the month, the earth was made dry.
15 Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
Then God spoke to Noah, saying:
16 “Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
“Go out of the ark, you and your wife, your sons and the wives of your sons with you.
17 Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
Bring out with you all the living things that are with you, all that is flesh: as with the birds, so also with the wild beasts and all the animals that move upon the earth. And enter upon the land: increase and multiply upon it.”
18 Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
And so Noah and his sons went out, and his wife and the wives of his sons with him.
19 Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
Then also all living things, and the cattle, and the animals that move upon the earth, according to their kinds, departed from the ark.
20 Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
Then Noah built an altar to the Lord. And, taking from each of the cattle and birds that were clean, he offered holocausts upon the altar.
21 Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
And the Lord smelled the sweet odor and said: “I will no longer curse the earth because of man. For the feelings and thoughts of the heart of man are prone to evil from his youth. Therefore, I will no longer pierce every living soul as I have done.
22 “Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”
All the days of the earth, seedtime and harvest, cold and heat, summer and winter, night and day, will not cease.”

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark