< Genesis 8 >

1 Tsono Mulungu anakumbukira Nowa ndi nyama zonse zakuthengo ndi ziweto zimene anali nazo mu chombo. Yehova anatumiza mphepo pa dziko lapansi ndipo madzi anaphwera.
Da ihukom Gud Noa og alle de vilde Dyr og Kvæget, som var hos ham i Arken; og Gud lod en Storm fare hen over Jorden, saa at Vandet begyndte at falde;
2 Tsono akasupe a madzi ambiri a pansi pa dziko ndi zitseko za madzi a kumwamba zinatsekedwa, ndipo mvula inaleka kugwa.
Verdensdybets Kilder og Himmelens Sluser lukkedes, Regnen fra Himmelen standsede,
3 Madzi amaphwabe pa dziko lapansi. Pakutha pa masiku 150, madzi anatsika,
og Vandet veg lidt efter lidt bort fra Jorden, og Vandet tog af efter de 150 Dages Forløb.
4 ndipo pa tsiku la 17 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, chombo chija chinakakhazikika pa mapiri a Ararati.
Paa den syttende Dag i den syvende Maaned sad Arken fast paa Ararats Bjerge,
5 Madzi anapitirira kuphwa mpaka mwezi wa khumi, ndipo pa tsiku loyamba la mwezi wa khumiwo msonga za mapiri zinayamba kuonekera.
og Vandet vedblev at synke indtil den tiende Maaned, og paa den første Dag i denne Maaned dukkede Bjergenes Toppe frem.
6 Patapita masiku makumi anayi, Nowa anatsekula zenera limene anapanga mʼchombomo
Da der var gaaet fyrretyve Dage: aabnede Noa den Luge, han havde lavet paa Arken,
7 natulutsa khwangwala, koma khwangwalayo ankangowuluka uku ndi uku mpaka madzi anawuma pa dziko lapansi.
og sendte en Ravn ud; den fløj frem og tilbage, indtil Vandet var tørret bort fra Jorden.
8 Kenaka anatulutsa nkhunda kuti aone ngati madzi aphwa pa dziko.
Da sendte han en Due ud for at se, om Vandet var sunket fra Jordens Overflade;
9 Koma nkhunda sinapeze poti nʼkutera chifukwa panali madzi ponseponse pa dziko lapansi. Choncho inabwerera kwa Nowa mʼchombo. Nowa anatulutsa dzanja lake kunja ndi kutenga nkhundayo kuyibwezera mʼchombo mmene iye anali.
men Duen fandt intet Sted at sætte sin Fod og vendte tilbage til ham i Arken, fordi der endnu var Vand over hele Jorden; og han rakte Haanden ud og tog den ind i Arken til sig.
10 Choncho anadikirabe masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatulutsanso nkhundayo mʼchombo muja.
Derpaa biede han yderligere syv Dage og sendte saa atter Duen ud fra Arken;
11 Pamene nkhunda inabwerera madzulo ake, inali itanyamula tsamba laliwisi la mtengo wa olivi. Motero Nowa anadziwa kuti madzi aphwadi pa dziko lapansi.
ved Aftenstid kom Duen tilbage til ham, og se, den havde et friskt Olieblad i Næbbet. Da skønnede Noa, at Vandet var svundet bort fra Jorden.
12 Iye anadikira masiku ena asanu ndi awiri ndipo anatumizanso nkhunda ija, koma nthawi imeneyi sinabwererenso kwa iye.
Derpaa biede han syv Dage til, og da han saa sendte Duen ud, kom den ikke mere tilbage til ham.
13 Pofika tsiku loyamba la mwezi woyamba wa chaka chimene Nowa anakwanitsa zaka 601, madzi anawuma pa dziko lapansi. Ndipo Nowa anachotsa denga la chombo ndipo anaona kuti kunja kwawuma.
I Noas 601ste Leveaar paa den første Dag i den første Maaned var Vandet tørret bort fra Jorden. Da tog Noa Dækket af Arken, og da han saa sig om, se, da var Jordens Overflade tør.
14 Pokwana tsiku la 27 la mwezi wachiwiri dziko lapansi linawumiratu.
Paa den syv og tyvende Dag i den anden Maaned var Jorden tør.
15 Tsono Mulungu anawuza Nowa kuti,
Da sagde Gud til Noa:
16 “Iwe, mkazi wako, ana ako pamodzi ndi akazi awo tulukani mʼchombomo.
»Gaa ud af Arken med din Hustru, dine Sønner og dine Sønnekoner
17 Tulutsa zamoyo zonse zili ndi iwe, mbalame, nyama ndi zokwawa zonse kuti ziswane ndi kuchulukana pa dziko lapansi.”
og for alle Dyr, der er hos dig, alt Kød, Fugle, Kvæg og alt Kryb, der kryber paa Jorden, ud med dig, at de kan vrimle paa Jorden og blive frugtbare og mangfoldige paa Jorden!«
18 Nowa anatuluka pamodzi ndi ana ake aamuna, mkazi wake ndi akazi a ana ake.
Da gik Noa ud med sine Sønner, sin Hustru og sine Sønnekoner;
19 Nyama zonse, zokwawa zonse, mbalame zonse, chilichonse choyenda pa dziko lapansi, zinatuluka mʼchombo motsogozana monga mwa mitundu yawo.
og alle de vildtlevende Dyr, alt Kvæget, alle Fuglene og alt Krybet, der kryber paa Jorden, efter deres Slægter, gik ud af Arken.
20 Pamenepo Nowa anamanga guwa lansembe la Yehova ndipo anatengako mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya ndi mbalame zoti nʼkudya naperekapo nsembe yopsereza.
Derpaa byggede Noa HERREN et Alter og tog nogle af alle de rene Dyr og Fugle og ofrede Brændofre paa Alteret.
21 Yehova atamva fungo labwino anati mu mtima mwake: “Sindidzatembereranso nthaka chifukwa cha munthu, ngakhale kuti maganizo a mu mtima mwake ndi oyipa kuyambira ubwana wake. Ndipo sindidzawononganso zolengedwa zonse zamoyo monga ndachitiramu.
Og da HERREN indaandede den liflige Duft, sagde han til sig selv: »Jeg vil aldrig mere forbande Jorden for Menneskenes Skyld, thi Menneskehjertets Higen er ond fra Ungdommen af, og jeg vil aldrig mere tilintetgøre alt, hvad der lever, saaledes som jeg nu har gjort!
22 “Nthawi zonse mmene dziko lapansi lidzakhalire, nthawi yodzala ndi nthawi yokolola yozizira ndi yotentha, dzinja ndi chilimwe, usana ndi usiku, sizidzatha.”
Herefter skal, saa længe Jorden staar, Sæd og Høst, Kulde og Hede, Sommer og Vinter, Dag og Nat ikke ophøre!«

< Genesis 8 >

A Dove is Sent Forth from the Ark
A Dove is Sent Forth from the Ark