< Genesis 7 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
Rəbbee Nühuk'le uvhuyn: – Xizanıka sacigee gameeqa ılqeç'e. Yizde ögee, vale qorkuna ine nasıle deşor.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
Dyunyeyne aq'vayle cins g'ıts'maq'vancenva məttıne həyvanaaşina yighıble q'öblena, xhalyne həyvanaaşina vughulyna, xhuvulyna alept'e. Harıne xəəne şit'enab yighıble q'öblena alept'e.
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
Yighne yiğıle ç'iyeyne aq'valqa yoqts'al yiğnayiy yoqts'al xəmna gyoğiy gyoğa'as. İtxhınin nafasnan gırgın kar ç'iyeyne aq'vayle hakkal ha'asın.
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
Rəbbee Nühulqa nəxübiy əmr hav'u, mang'vee gırgın kar həməxdıd hı'iyn.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
Ç'iyeyn aq'va q'ıfrımıka qadıyne xhinen alyat'uyng'a, Nühuka yixhıd vəş sen ıxha.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
Nüh, cuna xhunaşşe, dixbı, sossar sacigee xhyanıke g'attivxhanasdemee gameeqa ılqebaç'enbı.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
Allahee Nühulk'le uvhuyn xhinne, məttın, xhalin həyvanar, şit'yar, gırgın ç'iyeyl hadağvanbı q'öble-q'öblena, vughulynayiy xhuvulyna, Nühuka gameeqa ılqedaç'enbı.
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
Ç'iye yighne yiğıle q'ıfrımıka qadıyne xhinen alyat'an.
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
Nühune ı'mrene yixhıd vəş'esde sene, q'öb'esde vuzanee yits'ıyighıd'esde yiğıl məxdun q'ıfrımıkan gyoğiy gyooğa giyğal, ittehesu, xəən g'uleppı aaqı. Gırgıned k'oralybışençe xhyan ı'xı'yxə giyğal.
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
Yoqts'al yiğna, yoqts'al xəmna gyoğiy gyoğu.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
Mane yiğıl Nühuka sacigee cuna xhunaşşe, dixbı Sam, Ham, Yafəs, con yedar gameeqa ılqebaç'iynbı.
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
Manbışika sacigee gırgın həyvanar: çavra-vəq'ə, çolun həyvanar, şit'yar, gırgın ileedaxvanbı, ç'iyeyl hadağvanbı, gameeqa ılqedaç'enbı.
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
Gırgın nafas ileşşenbı q'öblena Nühuka gameeqa ılqeeç'u.
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
Allahee Nühuk'le uvhuyn xhinne, gırgıne həyvanaaşina vughulynayiy xhuvulyna qabı. Manbışiqad qihna Rəbbee gamıyn akka qa'an.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
Q'ıfrım gibğılıyn yoqts'al yiğ ıxhamee, xhyan geed qıxha gamı ç'iyeyle haly'etçuyn.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
Xhyan geed ooqa ılqeç'e, gamıd xhinene aq'val ı'ğiykar giyğal.
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
Geed qıxhayne xhyanın, nekke axtın suvabıd çik avud g'alya'a.
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
Xhyan yits'ı xholle xılekkumna suvabışile axtı qexhe.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
Ç'iyeyne aq'valin gırgın kar:
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
şit'yar, çavra-vəq'ə, çolun həyvanar, hadağvanbı, insanar, nafas ileşşen gırgın qeek'an.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
Rəbbee ç'iyeyne aq'valin nafas ileşşen gırgın kar hakkal ha'an: insanaaşile otçu, çavra-vəq'ə, hadağvanbı, xəəne şit'yaaşılqamee nafas ileşşen gırgın kar gek'an. Saccu Nühiy gameebınbı üç'übba axva.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
Xhyan ç'iyeyne aq'val vəşşe xhots'al yiğna geed qıxhayle qiyğa,