< Genesis 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
INkosi yasisithi kuNowa: Ngena wena lendlu yakho yonke emkhunjini, ngoba wena ngikubone ulungile phambi kwami kulesisizukulwana.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
Kuyo yonke inyamazana ehlambulukileyo uzazithathela ngasikhombisa ngasikhombisa, enduna lensikazi yayo; njalo kuyo inyamazana engahlambulukanga ezimbili, enduna lensikazi yayo.
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
Lakuzo inyoni zamazulu ngasikhombisa ngasikhombisa, enduna lensikazi, ukulondoloza inhlanyelo iphila ebusweni bomhlaba wonke.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
Ngoba kusele izinsuku eziyisikhombisa, besenginisa izulu emhlabeni, izinsuku ezingamatshumi amane lobusuku obungamatshumi amane, ngibhubhise konke okuphilayo, engakwenzayo, ebusweni bomhlaba.
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
UNowa wasesenza njengakho konke iNkosi eyamlaya khona.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
UNowa wayeleminyaka engamakhulu ayisithupha, lapho uzamcolo wamanzi ephezu komhlaba.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
UNowa wasengena emkhunjini lamadodana akhe lomkakhe labafazi bamadodana akhe kanye laye, ngenxa yamanzi kazamcolo.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
Kuzo inyamazana ezihlambulukileyo, lakuzo inyamazana ezingahlambulukanga, lakuzo inyoni, lakukho konke okuhuquzelayo phezu komhlaba,
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
ngambili ngambili kweza kuNowa emkhunjini, okuduna lokusikazi, njengoba uNkulunkulu emlayile uNowa.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
Kwasekusithi emva kwensuku eziyisikhombisa amanzi kazamcolo ayephezu komhlaba.
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
Ngomnyaka wamakhulu ayisithupha wempilo kaNowa, ngenyanga yesibili, ngosuku lwetshumi lesikhombisa lwenyanga, ngalolosuku yonke imithombo yokujula okukhulu yaqhekezwa, lamasango empophoma zamazulu avulwa.
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
Izulu laliphezu komhlaba insuku ezingamatshumi amane lobusuku obungamatshumi amane.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
Ngalolosuku olufananayo uNowa wangena loShemu loHamu loJafethi, amadodana kaNowa, lomkaNowa, labafazi abathathu bamadodana akhe kanye labo, emkhunjini,
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
bona, layo yonke inyamazana ngohlobo lwayo, laso sonke isifuyo ngohlobo lwaso, lakho konke okuhuquzelayo kuhuquzela phezu komhlaba ngohlobo lwakho, lakho konke okuphaphayo ngohlobo lwakho, yonke inyoni yalo lonke uphiko.
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
Zasezingena kuNowa emkhunjini, ngambili ngambili, kuyo yonke inyama, okukuyo umoya wempilo.
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
Lezangenayo, kwangena enduna lensikazi kuyo yonke inyama, njengalokho uNkulunkulu ayemlaye khona; iNkosi yasimvalela phakathi.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
Uzamcolo wasesiba semhlabeni insuku ezingamatshumi amane; amanzi asesanda asephakamisa umkhumbi, waze waphakama phezu komhlaba.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
Amanzi asephakama ngamandla, anda kakhulu phezu komhlaba; lomkhumbi wahamba phezu kobuso bamanzi.
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
Amanzi asephakama ngamandla kakhulukazi emhlabeni, zaze zasitshekelwa zonke intaba eziphakemeyo ezingaphansi kwamazulu wonke.
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
Izingalo ezilitshumi lanhlanu amanzi aqonga aphakama ngamandla, lezintaba zasitshekelwa.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
Yonke-ke inyama yaphela, eyayihamba phezu komhlaba, eyenyoni, leyesifuyo, leyenyamazana, leyakho konke okuhuquzelayo kuhuquzela phezu komhlaba, laye wonke umuntu;
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
konke okulokuphefumula komoya wempilo emakhaleni akho, kwakho konke okusemhlabeni owomileyo, kwafa.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
Kwachithwa konke okwakukhona, okwakusebusweni bomhlaba, kusukela emuntwini kusiya esifuyweni kusiya kokuhuquzelayo njalo kusiya enyonini yamazulu; kwasekuchithwa emhlabeni; kwasekutshiywa uNowa kuphela, lalokho ayelakho emkhunjini.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
Lamanzi ayephakama ngamandla phezu komhlaba, okwensuku ezilikhulu lamatshumi amahlanu.

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood