< Genesis 7 >
1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
Hagi Ra Anumzamo'a anage huno Noana asami'ne, Maka ama mopafima menima mani'naza vahepina kagrake fatgo nera mani'nanke'na negagoe. E'igu kagrane nagaka'anena ventefi mareriho.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
Kase avima hanagu avusese zagagafafintira 7ni'a aravere aravere zamavarentetere huo. Ana nehunka avusese osu zagagafafintira magoke arave zanavrentetere huo.
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
Ana nehunka kase avima hanagu nama 7ni'a aravere aravere zamavarentetere huo.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
Na'ankure 7ni'a zagegna manite'na Nagra ha'nenkeno kora rugahie. 40'a zagene hanine ko' nerinke'na, Nagrama mopafima trohu zamante'noa zana maka zamahe fanane hugahue.
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
Higeno Anumzamo'ma asmi'neaza huno Noa'a mika'zana hu'ne.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
Ana knafina Noa'a 600'a zagegafu mani'tegeno, timo'a mopa ahe refite'ne.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
Ko' runaku nehige'za, Noa'ene nenaro'ene, mofavre zaga'ane anoferahe'zane ventefi mareri'naze.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
Hagi agru osu zagaramimpinti'ene agruma hu'naza zagaramimpinti'ene namaramimpinti'ene, mika zagaramimpintira vene a'ene taretare hu'za Anumzamo'ma kema hu'neaza hu'za Noa'ene ventefi ufre'naze.
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
Hagi 7ni'a zagegna manitageno, kora erigafa huno rigeno, ti hageno refite'ne.
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
Noa'a 600'a zagegafu manitegeno 2 ikana 17tini zupa mopamo'a ruhagro higeno mopa agu'afinti tina hanatino tusi'a ti hage'ne. Tusi'a ko' ruvava huno havi avufgafinti hatihati huno tusi'a ti hage'ne.
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
Ana nehuno masane, hanine 40'a knafi ruose kora ruvava huno vu'ne.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
Noa'ma ventefi mareria zupa, mofavre naga'a Semiki, Hamuki, Jafeti'ma a'ne zamima nezmarerama hu'za mareri'naze.
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
Trampi zagagafane, kumate zagagafane, namane, rumofo rumofo mopafi ne'onse zagarmina, vene a'ene Noante etere hu'za ventefi ufre'naze.
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
Aravere aravere zamasimu nentaza zagagafamo'za ana maka Noante e'za ventefi ufre'naze.
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
Anante Anumzamo'ma kema hu'neaza huno aravere aravere mika ufre varetageno, Ra Anumzamo'a kafana erigi zamante'ne.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
Ranko'ma ru'neana zagene hanine 40'a knafi kora ruvava huno tusi'a ti hageno ana ventea mopafinti erisga huno mareri'ne.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
Ana nehuno timo'a reviteno marenerino mopa refitegeno, ventemo'a timofo agofetu me'ne.
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
Hagi timo'a mago'ene hageno marerino osi agonaramine, zaza agonaraminena mika erinakri vagare'ne.
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
Hagi timo'a mago'ene mareri aviteno, mika mopane mareri agatere'nea agonaraminena 7ni'a mita aru agatereno refite'ne.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
E'ina higeno mopafima mani'nea zagaramine, nontega zagagafane, trampi zagagafane, namaramine, ne'onse zagarmine, vahe'ene, mopafima vanoma nehaza zagarminena zamahe fri vagare'ne.
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
Hagi mopafima zamasimu eri'za mani'naza zagagafa, maka fri hana hu'naze.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
Anumzamo'a vahe'ene, ne'onse zagarmine, namaramine, zagagafanena zamahe fanane hige'za omanitfa hu'naze. Higeno Noa'ene ventefi mani'namo'za zamagrake kasefa hu'za mani'naze.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
Hagi 150'a zagegnafi timo'a mopa refite'ne.