< Genesis 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
And God said to Noah, "Come with all of your household into the ship, for I have seen your righteousness before me in this generation.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
You shall take seven pairs of every clean animal with you, the male and his female. Of the animals that are not clean, take two, the male and his female.
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
Also of the clean flying creatures of the sky, seven pairs, a male and a female, and of all the unclean flying creatures, one pair, a male and a female, to preserve their offspring on the surface of all the earth.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
In seven days, I will cause it to rain on the earth for forty days and forty nights. Every living thing that I have made, I will destroy from the surface of the ground."
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
Noah did everything that God commanded him.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
Noah was six hundred years old when the flood of waters came on the earth.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
Noah went into the ship with his sons, his wife, and his sons' wives, because of the waters of the flood.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
Clean animals, animals that are not clean, flying creatures, and everything that crawls on the ground
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
went by pairs to Noah into the ship, male and female, as God commanded Noah.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
It happened after the seven days, that the waters of the flood came on the earth.
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
In the six hundredth year of Noah's life, in the second month, on the seventeenth day of the month, on the same day all the fountains of the great deep were burst open, and the floodgates of the sky were opened.
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
The rain was on the earth forty days and forty nights.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
In the same day Noah, and Shem, Ham, and Japheth, the sons of Noah, and Noah's wife, and the three wives of his sons with them, entered into the ship;
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
they, and every wild animal after its kind, and every tame animal after their kind, every creature that crawls on the earth after its kind, and every flying creature after its kind, everything with wings.
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
They went to Noah into the ship, by pairs of all flesh with the breath of life in them.
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
Those who went in, went in male and female of all flesh, as God commanded him; and God shut him in.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
The flood was forty days on the earth. The waters increased, and lifted up the ship, and it was lifted up above the earth.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
The waters prevailed, and increased greatly on the earth; and the ship floated on the surface of the waters.
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
And the waters rose very high on the earth. And all the high mountains that were under the whole sky were covered.
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
The waters rose and covered the highest mountains to a depth of more than twenty-six feet.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
And all flesh died that moved on the earth, flying creatures, and tame animals, and wild animals, and every creature that crawls on the earth, and all humankind.
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
All in whose nostrils breathed the breath of life, of all that was on the dry land, died.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
Every living thing was destroyed that was on the surface of the ground, including people, animals, crawling creatures, and flying creatures of the sky. They were destroyed from the earth. Only Noah was left, and those who were with him in the ship.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
The waters prevailed on the earth one hundred fifty days.

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood