< Genesis 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
And the Lord said to him: Go in thou and all thy house into the ark: for thee I have seen just before me in this generation.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
Of all clean beasts take seven and seven, the male and the female.
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
But of the beasts that are unclean two and two, the male and the female. Of the fowls also of the air seven and seven, the male and the female: that seed may be saved upon the face of the whole earth.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
For yet a while, and after seven days, I will rain upon the earth forty days and forty nights; and I will destroy every substance that I have made, from the face of the earth.
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
And Noe did all things which the Lord had commanded him.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
And he was six hundred years old, when the waters of the flood overflowed the earth.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
And Noe went in and his sons, his wife and the wives of his sons with him into the ark, because of the waters of the flood.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
And of beasts clean and unclean, and of fowls, and of every thing that moveth upon the earth,
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
Two and two went in to Noe into the ark, male and female, as the Lord had commanded Noe.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
And after the seven days were passed, the waters of the flood overflowed the earth.
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
In the six hundredth year of the life of Noe, in the second month, in the seventeenth day of the month, all the fountains of the great deep were broken up, and the flood gates of heaven were opened:
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
And the rain fell upon the earth forty days and forty nights.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
In the selfsame day Noe, and Sem, and Cham, and Japheth his sons: his wife, and the three wives of his sons with them, went into the ark:
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
They and every beast according to its kind, and all the cattle in their kind, and every thing that moveth upon the earth according to its kind, and every fowl according to its kind, all birds, and all that fly,
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
Went in to Noe into the ark, two and two of all flesh, wherein was the breath of life.
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
And they that went in, went in male and female of all flesh, as God had commanded him: and the Lord shut him in on the outside.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
And the flood was forty days upon the earth, and the waters increased, and lifted up the ark on high from the earth.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
For they overflowed exceedingly: and filled all on the face of the earth: and the ark was carried upon the waters.
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
And the waters prevailed beyond measure upon the earth: and all the high mountains under the whole heaven were covered.
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
The water was fifteen cubits higher than the mountains which it covered.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
And all flesh was destroyed that moved upon the earth, both of fowl, and of cattle, and of beasts, and of all creeping things that creep upon the earth: and all men.
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
And all things wherein there is the breath of life on the earth, died.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
And he destroyed all the substance that was upon the earth, from man even to beast, and the creeping things and fowls of the air: and they were destroyed from the earth: and Noe only remained, and they that were with him in the ark.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
And the waters prevailed upon the earth a hundred and fifty days.

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood