< Genesis 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
Derpaa sagde HERREN til Noa: »Gaa ind i Arken med hele dit Hus, thi dig har jeg fundet retfærdig for mine Øjne i denne Slægt.
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
Af alle rene Dyr skal du tage syv Par, Han og Hun, og af alle urene Dyr eet Par, Han og Hun,
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
ligeledes af Himmelens Fugle syv Par, Han og Hun, for at de kan forplante sig paa hele Jorden.
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
Thi om syv Dage vil jeg lade det regne paa Jorden i fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter og udslette alle Væsener, som jeg har gjort, fra Jordens Flade.«
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
Og Noa gjorde ganske som HERREN havde paalagt ham.
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
Noa var 600 Aar gammel, da Vandfloden kom over Jorden.
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
Noa gik med sine Sønner, sin Hustru og sine Sønnekoner ind i Arken for at undslippe Flodens Vande.
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
De rene og de urene Dyr, Fuglene og alt, hvad der kryber paa Jorden,
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
gik Par for Par ind i Arken til Noa, Han og Hundyr, som Gud havde paalagt Noa.
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
Da nu syv Dage var omme, kom Flodens Vande over Jorden;
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
i Noas 600de Leveaar paa den syttende Dag i den anden Maaned, den Dag brast det store Verdensdybs Kilder, og Himmelens Sluser aabnedes,
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
og Regnen faldt over Jorden i fyrretyve Dage og fyrretyve Nætter.
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
Selv samme Dag gik Noa ind i Arken og med ham hans Sønner Sem, Kam og Jafet, hans Hustru og hans tre Sønnekoner
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
og desuden alle vildtlevende Dyr efter deres Arter, alt Kvæg efter dets Arter, alt Kryb paa Jorden efter dets Arter og alle Fugle efter deres Arter, alle Fugle, alt, hvad der har Vinger;
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
af alt Kød, som har Livsaande, gik Par for Par ind i Arken til Noa;
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
Han og Hundyr af alt Kød gik ind, som Gud havde paabudt, og HERREN lukkede efter ham.
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
Da kom Vandfloden over Jorden i fyrretyve Dage, og Vandet steg og løftede Arken, saa den hævedes over Jorden.
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
Og Vandet steg og stod højt over Jorden, og Arken flød paa Vandet;
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
og Vandet steg og steg over Jorden, saa de højeste Bjerge under Himmelen stod under Vand;
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
femten Alen stod Vandet over dem, saa Bjergene stod helt under Vand.
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
Da omkom alt Kød, som rørte sig paa Jorden, Fugle, Kvæg, vildtlevende Dyr og alt Kryb paa Jorden og alle Mennesker;
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
alt, i hvis Næse det var Livets Aande, alt, hvad der var paa det faste Land, døde.
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
Saaledes udslettedes alle Væsener, der var paa Jordens Flade, Mennesker, Kvæg, Kryb og Himmelens Fugle; de udslettedes af Jorden, og tilbage blev kun Noa og de, der var hos ham i Arken.
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
Vandet steg over Jorden i 150 Dage.

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood