< Genesis 7 >

1 Ndipo Yehova anati kwa Nowa, “Lowa mu chombo iwe ndi banja lako lonse, chifukwa ndaona kuti ndiwe wolungama mu mʼbado uwu.
上主對諾厄說:「你和你全家進入方舟,因為在這一世代,我看只有你在我面前正義。
2 Pa mtundu uliwonse wa nyama zoti nʼkudya utengepo zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi zazikazi zisanu ndi ziwirinso. Koma pa mtundu wa nyama iliyonse yosati nʼkudya utengepo zazimuna ziwiri ndi zazikazi ziwirinso.
由一切潔淨牲畜中,各取公母七對;由那些不潔淨的牲畜中,各取公母一對;
3 Chimodzimodzinso mbalame, utenge zisanu ndi ziwiri zazimuna ndi zisanu ndi ziwiri zazikazi za mtundu uliwonse kuti mitundu yawo isungike ndi moyo pa dziko lonse lapansi.
由天空的飛鳥中,也各取公母七對;好在全地面上傳種。
4 Pakapita masiku asanu ndi awiri ndidzagwetsa mvula pa dziko lapansi kwa masiku makumi anayi usana ndi usiku ndipo ndidzawononga cha moyo chilichonse chimene ndinachipanga pa dziko lapansi.”
因為還有七天,我要在地上降雨四十天四十夜,消滅我在地面上所造的一切生物。」
5 Ndipo Nowa anachita zonse zimene Yehova anamulamulira.
諾厄全照上主吩咐他的做了。
6 Pamene chigumula chinabwera pa dziko lapansi Nowa anali ndi zaka 600.
當洪水在地上氾濫時,諾厄已六百歲。
7 Ndipo Nowa, ana ake aamuna, mkazi wake, pamodzi ndi ana ake aakazi analowa mu chombo chija kuthawa madzi a chigumula.
諾厄和他的兒子,他的妻子和他的兒媳,同他進了方舟,為躲避洪水。
8 Nyama zoti nʼkudya ndi nyama zosadyedwa, mbalame, pamodzi ndi nyama zokwawa zonse zinadza kwa Nowa ziwiriziwiri ndi kulowa mʼchombomo.
潔淨的牲畜和不潔淨的牲畜,飛鳥和各種在地上爬行的動物,
9 Ndipo Nowa anatenga ziwiriziwiri, yayimuna ndi yayikazi monga anamulamulira Mulungu.
一對一對地同諾厄進了方舟;都是一公一母,照天主對他所吩咐的。
10 Patapita masiku asanu ndi awiri chigumula chinabwera pa dziko lapansi.
七天一過,洪水就在地上氾濫。
11 Pa tsiku la 17 la mwezi wachiwiri, Nowa ali ndi zaka 600, akasupe onse akuya kwambiri anasefuka ndiponso zitseko za madzi akumwamba zinatsekuka.
諾厄六百歲那一年,二月十七日那天,所有深淵的泉水都冒出,天上的水閘都開放了;
12 Ndipo mvula inagwa pa dziko lapansi masiku makumi anayi usana ndi usiku.
大雨在地上下了四十天四十夜。
13 Linali tsiku lomwelo pamene Nowa ndi ana ake aamuna, Semu, Hamu ndi Yafeti, pamodzi ndi mkazi wake ndi akazi a ana ake atatu aja analowa mu chombo.
正在這一天,諾厄和他的兒子閃、含、耶斐特,他的妻子和他的三個兒媳,一同進了方舟。
14 Iwowa analowa mʼchombomo pamodzi ndi nyama iliyonse ya kutchire monga mwa mtundu wake, ziweto zonse monga mwa mitundu yawo, nyama yokwawa iliyonse monga mwa mtundu wake ndi mbalame iliyonse monga mwa mtundu wake.
他們八口和所有的野獸、各種牲畜、各種在地上爬行的爬蟲、各種飛禽,
15 Nowa analowa mu chombo muja pamodzi ndi zamoyo zonse.
一切有生氣有血肉的,都一對一對地同諾厄進了方舟。
16 Iye analowa nazo zazimuna ndi zazikazi monga mmene Mulungu anamulamulira. Kenaka Yehova anatseka pa khomo.
凡有血肉的,都是一公一母地進了方舟,如天主對諾厄所吩咐的。隨後上主關了門。
17 Chigumula chinagwa pa dziko la pansi kwa masiku makumi anayi. Madzi anayamba kuchuluka ndipo ananyamula chombo chija ndi kuchiyandamitsa pamwamba pa dziko.
洪水在地上氾濫了四十天;水不斷增漲,浮起了方舟,方舟遂由地面上升起。
18 Madzi anafika mwamphamvu ndipo anachulukirachulukira pa dziko lapansi moti chombo chinayandama pamwamba pa madziwo.
洪水洶湧,在地上猛漲,方舟漂浮在水面上。
19 Madzi a chigumula anabwerabe molimbika motero kuti mapiri ataliatali onse a pa dziko anamizidwa.
洪水在地上一再猛漲,天下所有的高山也都沒了頂;
20 Madzi anakwera namiza mapiri kwa mamita pafupifupi asanu ndi awiri.
洪水高出淹沒的群山十有五肘。
21 Chamoyo chilichonse choyenda pa dziko lapansi chinafa: mbalame, ziweto, nyama zakuthengo, miyandamiyanda ya zonse zolengedwa za pa dziko lapansi pamodzi ndi anthu.
凡地上行動而有血肉的生物:飛禽、牲畜、野獸,在地上爬行的爬蟲,以及所有的人全滅亡了;
22 Chilichonse chamoyo, chokhala pa mtunda chinafa.
凡在旱地上以鼻呼吸的生靈都死了。
23 Chamoyo chilichonse pa dziko lapansi chinawonongedwa, kuyambira munthu, nyama, zokwawa ndi mbalame. Nowa yekha ndiye anatsala pamodzi ndi onse amene anali naye.
這樣,天主消滅了在地面上的一切生物,由人以至於牲畜、爬蟲以及天空中的飛鳥,這一切都由地上消滅了,只剩下諾厄和同他在方舟內的人物。
24 Madziwo anadzaza dziko lonse lapansi kwa masiku 150.
洪水在地上氾濫了一百五十天。

< Genesis 7 >

The Great Flood
The Great Flood