< Genesis 6 >
1 Anthu atayamba kuchuluka pa dziko lapansi ndi kubereka ana aakazi,
Og det skete, der Menneskene havde begyndt at formeres paa Jorden, og Døtre fødtes dem,
2 ana aamuna a Mulungu anaona kuti ana aakazi a anthuwo anali okongola. Ndipo anakwatira aliyense amene anamusankha.
da saa Guds Sønner Menneskens Døtre, at de vare skønne, og toge sig Hustruer af alle, hvilke de valgte.
3 Tsono Yehova anati, “Sindilola kuti chipwirikiti chikuchitikachi chipitirire mpaka muyaya, pakuti iye ndi munthu; masiku a moyo wake adzakhala zaka 120.”
Da sagde Herren: Min Aand skal ikke herske i Mennesket evindelig, eftersom han er Kød; og hans Dage skulle være hundrede og tyve Aar.
4 Masiku amenewo komanso pambuyo pake, pa dziko lapansi panali Anefili, anthu amphamvu ndiponso otchuka. Anthuwa ndi amene ankabadwa ana a Mulungu aja atakwatira ana aakazi a anthu.
Paa den Tid vare Kæmper paa Jorden, ja ogsaa efter at Guds Sønner vare indgangne til Menneskens Døtre og havde avlet sig Børn; disse ere de vældige, hvilke fra fordums Tid have været navnkundige Mænd.
5 Pamene Yehova anaona kuti kuyipa kwa munthu pa dziko lapansi kunali kwakukulu ndi kuti nthawi zonse amalingalira ndi kukhumbira kuchita zoyipa zokhazokha,
Og Herren saa, at Menneskets Ondskab var stor paa Jorden, og at alt hans Hjertes Tankers Paafund var ikkun ondt hver Dag.
6 Yehova anamva chisoni kuti analenga munthu ndi kumuyika pa dziko lapansi, ndipo anawawidwa mtima.
Da angrede Herren, at han havde gjort Mennesket paa Jorden, og det bedrøvede ham i hans Hjerte.
7 Choncho Yehova anati, “Ndidzafafaniza munthu, nyama, zonse zokwawa, ndi mbalame za mu mlengalenga pa dziko lapansi, pakuti ndikumva chisoni kuti ndinazilenga zimenezi.”
Og Herren sagde: Jeg vil udslette Mennesket, som jeg har skabt, af Jorden, baade Mennesker og Kvæg og Kryb og Fugle under Himmelen; thi jeg angrer, at jeg gjorde dem.
8 Koma Yehova anamukomera mtima Nowa.
Men Noa fandt Naade for Herrens Øjne.
9 Mbiri ya Nowa inali yotere: Nowa anali munthu wolungama ndi wopanda tchimo pakati pa anthu a mʼbado wake. Ndipo anayenda ndi Mulungu.
Disse ere Noas Slægter. Noa, en retfærdig Mand, var ustraffelig i sin Tid, Noa vandrede med Gud.
10 Nowa anabereka ana aamuna atatu: Semu, Hamu ndi Yafeti.
Og Noa avlede tre Sønner: Sem, Kam og Jafet.
11 Chiwawa chinadzaza pa dziko lapansi kotero kuti dziko linakhala lowonongeka pamaso pa Mulungu.
Men Jorden var fordærvet for Guds Ansigt, og Jorden var fuld af Vold.
12 Mulungu atayangʼana, anaona kuti dziko layipadi chifukwa cha makhalidwe oyipa a anthu onse pa dziko lapansi.
Da saa Gud Jorden, og se, den var fordærvet; thi alt Kød havde fordærvet sin Vej paa Jorden.
13 Ndipo Mulungu anati kwa Nowa, “Ndatsimikiza mtima kuti ndiwononge anthu onse, pakuti dziko lapansi ladzaza ndi ntchito zawo zoyipa. Ndithudi ndiwawononga pamodzi ndi zonse za pa dziko.
Da sagde Gud til Noa: Alt Køds Ende er kommen for mit Ansigt; thi Jorden er fuld af Vold af dem; og se, jeg vil fordærve dem med Jorden.
14 Tsono udzipangire chombo cha matabwa a mtengo wanjale; mʼkati mwake upange zipinda ndipo upake phula mʼkati ndi kunja.
Gør dig en Ark af Gofertræ; gør Rum i Arken, og beg den inden og udentil med Beg.
15 Uchipange motere: Chombo chikhale mamita 140 mulitali, mamita 23 mulifupi ndi mamita 13 mu msinkhu wake.
Og denne er Maaden, efter hvilken du skal gøre den: Tre Hundrede Alen skal Arkens Længde være, halvtredsindstyve Alen dens Bredde og tredive Alen dens Højde.
16 Uchipangire denga ndi kuchimaliza ndi zenera la masentimita makumi asanu. Uyike khomo mʼmbali mwa chombocho ndi kupanga zipinda zosanjikana; chapansi, chapakati ndi chapamwamba.
Du skal gøre et Vindue paa Arken, og oventil skal du fuldkomme den til en Alen, og Arkens Dør skal du sætte paa dens Side; du skal gøre den med et nederste, et mellemste og et tredje Loft.
17 Ndidzagwetsa mvula ya chigumula pa dziko lapansi kuti ndiwononge zamoyo zonse za pansi pa thambo ndipo chilichonse cha pa dziko lapansi chidzafa.
Og jeg, se, jeg lader komme en Vandflod over Jorden til at fordærve alt Kød, som har Livs Aande i sig under Himmelen; alt det, som er paa Jorden, skal udaande.
18 Koma ndidzachita pangano langa ndi iwe. Iwe, ana ako aamuna, mkazi wako ndi akazi a ana ako nonse mudzalowa mʼchombocho.
Men med dig opretter jeg min Pagt; og du skal gaa i Arken, du og dine Sønner og din Hustru og dine Sønners Hustruer med dig.
19 Iwe udzalowa mʼchombocho ndi zolengedwa zamoyo zonse ziwiriziwiri, chachimuna ndi chachikazi, kuti zisungike ndi moyo pamodzi ndi iwe.
Og af alt det, som lever, af alt Kød, et Par af hver Slags skal du indføre i Arken, at lade leve med dig; Han og Hun skal det være.
20 Udzatenga ziwiriziwiri za mitundu yonse ya mbalame, mitundu yonse ya nyama, ndi mitundu yonse ya zokwawa kuti zikhale ndi moyo.
Af Fuglene efter deres Slags og af Kvæget efter deres Slags, af alle Haande Kryb paa Jorden efter deres Slags; et Par af hvert skal gaa ind til dig, at de maa leve.
21 Udzatengenso chakudya cha mtundu uliwonse ndi kuchisunga kuti inu ndi nyamazo muzidzadya.”
Og tag du dig af alle Haande Føde, som ædes, og samle til dig, at det maa blive dig og dem til Næring.
22 Nowa anachita zonse monga Mulungu anamulamulira.
Og Noa gjorde det, efter alt det, som Gud havde befalet ham, saaledes gjorde han.