< Genesis 50 >
1 Kenaka Yosefe anadzigwetsa pa nkhope ya abambo ake, nawapsompsona kwinaku akulira.
Zatem upadł Józef na twarz ojca swego, i płakał nad nim, a całował go.
2 Ndipo Yosefe analamula antchito ake a chipatala kuti akonze thupi la Israeli ndi mankhwala kuti lisawole. Kotero antchitowo anakonzadi thupilo.
I rozkazał Józef sługom swym lekarzom, aby wonnemi maściami namazali ojca jego; i namazali wonnemi maściami lekarze Izraela.
3 Antchito aja zinawatengera masiku 40 kuti akonze mtembo uja popeza ntchito ngati imeneyi inafunikira masiku monga amenewa. Ndipo Aigupto anamulira Yakobo kwa masiku makumi asanu ndi awiri.
A gdy się mazania jego wypełniło czterdzieści dni, ( bo się tak wypełniają dni tych, którzy wonnemi maściami mazani bywają ), tedy go płakali Egipczanie przez siedemdziesiąt dni.
4 Yosefe atatha kulira maliro a abambo ake, anayankhula kwa nduna za Farao nati, “Ngati mungandikomere mtima, chonde mundiyankhulire kwa Farao kumuwuza kuti,
A po wyjściu dni żałoby jego rzekł Józef do sług Faraonowych, mówiąc: Jeźlim teraz znalazł łaskę w oczach waszych, powiedzcie proszę Faraonowi, mówiąc:
5 ‘Abambo anga anandilumbiritsa ndipo anati, ‘Ndatsala pangʼono kumwalira, ukandiyike mʼmanda amene ndinakumba ndekha mʼdziko la Kanaani.’ Tsono mundilole ndikayike abambo anga, ndipo ndikabweranso.’”
Ojciec mój poprzysiągł mię mówiąc: Oto, ja umieram; w grobie moim, którym sobie wykopał w ziemi Chananejskiej, tam mię pogrzebiesz; a teraz niech jadę, proszę, i pogrzebię ojca mego, i zaś się wrócę.
6 Farao anati, “Pita ukayike abambo ako monga anakulumbiritsa kuti uchite.”
Tedy rzekł Farao: Jedź a pogrzeb ojca twego, jako cię poprzysiągł.
7 Kotero Yosefe anapita kukayika abambo ake. Nduna zonse za Farao, akuluakulu a bwalo lake ndi akuluakulu a ku Igupto, anapita naye pamodzi.
Jechał tedy Józef, aby pogrzebał ojca swego; jechali też z nim wszyscy słudzy Faraonowi, także starsi domu jego, i wszyscy starsi ziemi Egipskiej;
8 Anapitanso onse a pa banja la Yosefe ndi abale ake ndi onse amene anali a pa banja la abambo ake. Ana awo okha, nkhosa ndi ngʼombe zinatsala ku Goseni
I wszystek dom Józefów, i bracia jego, i dom ojca jego; tylko dziatki swoje, i owce swoje, i woły swoje zostawili w ziemi Gosen.
9 Asilikali okwera pa magaleta ndi asilikali a pa akavalo anapita nayenso pamodzi. Linali gulu lalikulu.
Szły też z nimi i wozy, i jezdni; a był poczet bardzo wielki.
10 Atafika pa Goreni ha-Atadi, pafupi ndi Yorodani, anachita mwambo waukulu wa maliro. Choncho Yosefe analira maliro a abambo ake masiku asanu ndi awiri.
I przyjechali aż na pole Atad, które jest przy brodzie Jordańskim, i płakali tam płaczem wielkim i bardzo ciężkim; i obchodził Józef po ojcu swym żałobę przez siedem dni.
11 Akanaani amene ankakhala ku Goreni ha-Atadi ataona mwambo wa maliro anati, “Aigupto ali ndi mwambo wa maliro a akulu.” Ndi chifukwa chake malo amenewo a pafupi ndi Yorodani amatchedwa Abeli-Mizraimu.
A ujrzawszy obywatele ziemi Chananejskiej żałobę onę na polu Atad, mówili: Żałoba to ciężka Egipczanów; przetoż nazwano imię miejsca onego Abel Micraim, które jest przy brodzie Jordańskim.
12 Choncho ana a Yakobo anachita monga momwe abambo awo anawalamula:
Uczynili tedy z nim synowie jego, jak im był rozkazał.
13 Ndiye kuti ana a Yakobo anamunyamula kupita naye ku Kanaani kuti akamuyike mʼphanga limene lili mʼmunda wa Makipela pafupi ndi Mamre. Abrahamu anagula mundawo kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
I zawieźli go synowie jego do ziemi Chananejskiej, i pogrzebli go w jaskini na polu Machpela, którą Abraham był kupił z rolą na osiadłość grobu, od Efrona Hetejczyka, przeciwko Mamre.
14 Atatha kuyika abambo ake, Yosefe anabwerera ku Igupto, pamodzi ndi abale ake ndi onse amene anapita nawo kukayika abambo ake.
Zatem się wrócił Józef do Egiptu z bracią swą, i ze wszystkimi, którzy jeździli z nim na pogrzeb ojca jego, odprawiwszy pogrzeb ojca swego.
15 Abale ake a Yosefe ataona kuti abambo awo amwalira, anati, “Nanga tidzatani ngati Yosefe anatisungira mangawa nafuna kutibwezera pa zoyipa zonse zimene tinamuchitira?”
A widząc bracia Józefowi, że umarł ojciec ich, mówili: Podobno będzie nas miał w nienawiści Józef, i sowicie odda nam wszystko złe, któreśmy mu uczynili.
16 Motero anatumiza mawu kwa Yosefe kuti, “Abambo anu anasiya malangizo asanafe nati:
Wskazali tedy do Józefa, mówiąc: Ojciec twój rozkazał, pierwej niż umarł, mówiąc:
17 ‘Zimene mudzayenera kunena kwa Yosefe ndi izi: Ndikukupempha kuti uwakhululukire abale ako cholakwa chawo ndi machimo awo, popeza anakuchitira zoyipa.’ Ndiye tsopano chonde tikhululukireni zolakwa zimene ife akapolo a Mulungu wa abambo anu tinachita.” Yosefe atangomva mawu amenewa anayamba kulira.
Tak powiedzcie Józefowi: Proszę, odpuść teraz przestępstwo braci twej, i grzech ich, żeć złość wyrządzili; proszę odpuść teraz występek sługom Boga ojca twego. I płakał Józef, gdy to mówili do niego.
18 Kenaka abale ake anabwera nadzigwetsa pansi pamaso pake, nati, “Ife ndife akapolo anu.”
I przystąpili bracia jego, a upadłszy przed nim, mówili: Otośmy sługami twoimi.
19 Koma Yosefe anawawuza kuti, “Musachite mantha. Kodi ine ndalowa mʼmalo mwa Mulungu?
I rzekł do nich Józef: Nie bójcie się: bo azażem ja wam za Boga?
20 Inu munafuna kundichitira zoyipa, koma Mulungu anasandutsa zoyipazo kuti zikhale zabwino kuti zikwaniritsidwe zimene zikuchitika panozi, zopulumutsa miyoyo yambiri.
Wyście złe myślili przeciwko mnie, ale Bóg obrócił to w dobre, chcąc uczynić to, co się dziś dzieje, aby zachował tak wielki lud.
21 Kotero, musachite mantha. Ine ndidzasamalira inu pamodzi ndi ana anu omwe.” Tsono iye anawalimbitsa mtima powayankhula moleza mtima.
A przetoż nie bójcie się, ja żywić będę was i dziatki wasze; a tak cieszył je, i mówił z nimi łagodnie.
22 Yosefe anakhala mu Igupto pamodzi ndi banja lonse la abambo ake. Anakhala ndi moyo zaka 110
I mieszkał Józef w Egipcie, sam i dom ojca jego, a żył Józef sto i dziesięć lat.
23 ndipo anaona mʼbado wachitatu wa ana a Efereimu. Yosefe anatenganso ana a Makiri, mwana wa Manase kukhala ngati ana a mʼbanja lake.
I oglądał Józef syny Efraimowe aż do trzeciego pokolenia. Synowie też Machyra, syna Manasesowego, porodzili się na kolanach Józefowych.
24 Kenaka Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndatsala pangʼono kufa. Koma mosakayika Mulungu adzakuyangʼanirani nadzakutengani kukutulutsani mʼdziko lino kupita ku dziko limene Iye analonjeza kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo.”
I rzekł Józef do braci swej: Ja umrę, ale Bóg zapewnie nawiedzi was, i wyprowadzi was z ziemi tej do ziemi, o którą przysiągł Abrahamowi, Izaakowi i Jakóbowi.
25 Ndipo Yosefe analumbiritsa ana a Israeli lumbiro nati, “Lonjezani kuti Mulungu akadzakusungani mudzanyamula mafupa anga kuwachotsa ku malo kuno.”
I poprzysiągł Józef syny Izraelowe, mówiąc: Gdy was nawiedzi Pan Bóg, wynieście też kości moje stąd.
26 Choncho Yosefe anafa ali ndi zaka 110. Motero iwo atakonza thupi lake ndi mankhwala kuti lisawole, analiyika mʼbokosi ku Igupto.
I umarł Józef, mając sto i dziesięć lat; którego namazawszy wonnemi maściami, włożono do trumny w Egipcie.