< Genesis 5 >
1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
Dies ist das Buch von Adams Geschlechtern. An dem Tage, da Gott Adam schuf, machte er ihn im Gleichnis Gottes.
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
Mann und Weib [W. Männlich und weiblich] schuf er sie, und er segnete sie und gab ihnen den Namen Mensch, [H. Adam] an dem Tage, da sie geschaffen wurden. -
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
Und Adam lebte 130 Jahre und zeugte einen Sohn in seinem Gleichnis, nach seinem Bilde, und gab ihm den Namen Seth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und die Tage Adams, nachdem er Seth gezeugt hatte, waren 800 Jahre, und er zeugte Söhne und Töchter.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
Und alle Tage Adams, die er lebte, waren 930 Jahre, und er starb. -
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
Und Seth lebte 105 Jahre und zeugte Enos.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Seth lebte, nachdem er Enos gezeugt hatte, 807 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
Und alle Tage Seths waren 912 Jahre, und er starb. -
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
Und Enos lebte 90 Jahre und zeugte Kenan.
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Enos lebte, nachdem er Kenan gezeugt hatte, 815 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
Und alle Tage Enos waren 905 Jahre, und er starb. -
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
Und Kenan lebte 70 Jahre und zeugte Mahalalel.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Kenan lebte, nachdem er Mahalalel gezeugt hatte, 840 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
Und alle Tage Kenans waren 910 Jahre, und er starb. -
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
Und Mahalalel lebte 65 Jahre und zeugte Jered.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Mahalalel lebte, nachdem er Jered gezeugt hatte, 830 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
Und alle Tage Mahalalels waren 895 Jahre, und er starb. -
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
Und Jered lebte 162 Jahre und zeugte Henoch. [H. Chanok: eingeweit, belehrt]
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Jered lebte, nachdem er Henoch gezeugt hatte, 800 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
Und alle Tage Jereds waren 962 Jahre, und er starb. -
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
Und Henoch lebte 65 Jahre und zeugte Methusalah.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Henoch wandelte mit Gott, nachdem er Methusalah gezeugt hatte, 300 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
Und alle Tage Henochs waren 365 Jahre.
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
Und Henoch wandelte mit Gott; und er war nicht mehr, denn Gott nahm ihn hinweg. -
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
Und Methusalah lebte 187 Jahre und zeugte Lamech.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Methusalah lebte, nachdem er Lamech gezeugt hatte, 782 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
Und alle Tage Methusalahs waren 969 Jahre, und er starb. -
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
Und Lamech lebte 182 Jahre und zeugte einen Sohn.
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
Und er gab ihm den Namen Noah, [H. Noach: Trost, Ruhe] indem er sprach: Dieser wird uns trösten über unsere Arbeit und über die Mühe unserer Hände wegen des Erdbodens, den Jehova verflucht hat.
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Und Lamech lebte, nachdem er Noah gezeugt hatte, 595 Jahre und zeugte Söhne und Töchter.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
Und alle Tage Lamechs waren 777 Jahre, und er starb. -
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
Und Noah war 500 Jahre alt; und Noah zeugte Sem, [H. Schem: Name, Ruf] Ham [H. Cham: Bedeutung ungewiß] und Japhet. [Erweiterung, Ausbreitung; vergl. Kap. 9,27]