< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
Ceci est l’histoire des générations de l’humanité. Lorsque Dieu créa l’être humain, il le fit à sa propre ressemblance.
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
Il les créa mâle et femelle, les bénit et les appela l’homme, le jour de leur création.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
Adam, ayant vécu cent trente ans, produisit un être à son image et selon sa forme, et lui donna pour nom Seth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après avoir engendré Seth, Adam vécut huit cents ans, engendrant des fils et des filles.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
Tout le temps qu’Adam vécut fut donc de neuf cent trente ans; et il mourut.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
Seth, ayant vécu cent cinq ans, engendra Énos.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après avoir engendré Énos, Seth vécut huit cent sept ans, engendrant des fils et des filles.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
Tous les jours de Seth furent de neuf cent douze ans, après quoi il mourut.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
Énos vécut quatre-vingt-dix ans, et engendra Kênân.
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Enos vécut, après avoir engendré Kênân, huit cent quinze ans; et il eut des fils et des filles.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
Tous les jours d’Énos furent de neuf cent cinq ans, après quoi il mourut.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
Kênân, ayant vécu soixante-dix ans, engendra Mahalalêl.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Kènan vécut, après la naissance, de Mahalalêl, huit cent quarante ans, et eut des fils et des filles.
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
Toute la vie de Kênân fut de neuf cent dix ans, après quoi il mourut.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
Mahalalêl, ayant vécu soixante-cinq ans, engendra Yéred.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Mahalalél, après avoir engendré Yéred, vécut huit cent trente ans, et engendra des fils et des filles.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
Tous les jours de Mahalalèl furent de huit cent quatre-vingt-quinze ans, puis il mourut.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
Véred, ayant vécu cent soixante-deux ans, engendra Hénoc.
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Yéred vécut, après la naissance d’Hénoc, huit cents ans; il eut des fils et des filles.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
La vie entière de Yéred fut de neuf cent soixante-deux ans, après quoi il mourut.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
Hénoc vécut soixante-cinq ans, et engendra Mathusalem.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Hénoc se conduisit selon Dieu, après avoir engendré Mathusalem, durant trois cents ans, et engendra des fils et des filles.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
Tous les jours d’Hénoc furent de trois cent soixante-cinq ans;
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
Hénoc se conduisait selon Dieu, lorsqu’il disparut, Dieu l’ayant retiré du monde.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
Mathusalem, ayant vécu cent quatre-vingt-sept ans, engendra Lamec.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Mathusalem vécut, après avoir engendré Lamec, sept cent quatre-vingt-deux ans; il eut encore des fils et des filles.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
Tous les jours de Mathusalem furent de neuf cent soixante-neuf ans, après quoi il mourut.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
Lamec, ayant vécu cent quatre-vingt-deux ans, engendra un fils.
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
Il énonça son nom Noé, en disant: "Puisse-t-il nous soulager de notre tâche et du labeur de nos mains, causé par cette terre qu’a maudite l’Éternel!"
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Lamec vécut, après avoir engendré Noé, cinq cent quatre-vingt-quinze ans; il engendra des fils et des filles.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
Toute la vie de Lamec fut de sept cent soixante-dix-sept ans; et il mourut.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
Noé, étant âgé de cinq cents ans, engendra Sem, puis Cham et Japhet.

< Genesis 5 >