< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
Voici le livre de l’histoire d’Adam. Lorsque Dieu créa Adam, il le fit à la ressemblance de Dieu.
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
Il les créa mâle et femelle, et il les bénit, et il leur donna le nom d’Homme, lorsqu’ils furent créés.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
Adam vécut cent trente ans, et il engendra un fils à sa ressemblance, selon son image, et il lui donna le nom de Seth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Les jours d’Adam, après qu’il eut engendré Seth, furent de huit cents ans, et il engendra des fils et des filles.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
Tout le temps qu’Adam vécut fut de neuf cent trente ans, et il mourut.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
Seth vécut cent cinq ans, et il engendra Enos.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Enos, Seth vécut huit cent sept ans, et il engendra des fils et des filles.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
Tout le temps que Seth vécut fut de neuf cent douze ans, et il mourut.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
Enos vécut quatre-vingt-dix ans, et il engendra Caïnan.
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Caïnan, Enos vécut huit cent quinze ans, et il engendra des fils et des filles.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
Tout le temps qu’Enos vécut fut de neuf cent cinq ans, et il mourut.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
Caïnan vécut soixante-dix ans, et il engendra Malaléel.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Malaléel, Caïnan vécut huit cent quarante ans, et il engendra des fils et des filles.
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
Tout le temps que Caïnan vécut fut de neuf cent dix ans, et il mourut.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
Malaléel vécut soixante-cinq ans, et il engendra Jared.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Jared, Malaléel vécut huit cent trente ans, et il engendra des fils et des filles.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
Tout le temps que Malaléel vécut fut de huit cent quatre-vingt-quinze ans, et il mourut.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
Jared vécut cent soixante-deux ans, et il engendra Hénoch.
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Hénoch, Jared vécut huit cents ans, et il engendra des fils et des filles.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
Tout le temps que Jared vécut fut de neuf cent soixante-deux ans, et il mourut.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
Hénoch vécut soixante-cinq ans, et il engendra Mathusalem.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Mathusalem, Hénoch marcha avec Dieu trois cents ans, et il engendra des fils et des filles.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
Tout le temps qu’Hénoch vécut fut de trois cent soixante-cinq ans.
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
Hénoch marcha avec Dieu, et on ne le vit plus, car Dieu l’avait pris.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
Mathusalem vécut cent quatre-vingt-sept ans, et il engendra Lamech.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Lamech, Mathusalem vécut sept cent quatre-vingt-deux ans, et il engendra des fils et des filles.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
Tout le temps que Mathusalem vécut fut de neuf cent soixante-neuf ans, et il mourut.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
Lamech vécut cent quatre-vingt-deux ans, et il engendra un fils.
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
Il lui donna le nom de Noé, en disant: « Celui-ci nous soulagera de nos fatigues et du travail pénible de nos mains, provenant de ce sol qu’a maudit Yahweh. »
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
Après qu’il eut engendré Noé, Lamech vécut cinq cent quatre-vingt-quinze ans, et il engendra des fils et des filles.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
Tout le temps que Lamech vécut fut de sept cent soixante-dix-sept ans, et il mourut.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
Noé, âgé de cinq cents ans, engendra Sem, Cham et Japheth.

< Genesis 5 >