< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
This is the book of generacioun of Adam, in the dai wher ynne God made man of nouyt. God made man to the ymage and licnesse of God;
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
God formede hem male and female, and blesside hem, and clepide the name of hem Adam, in the day in which thei weren formed.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
Forsothe Adam lyuede an hundrid yeer and thretti, and gendride a sone to his ymage and liknesse, and clepide his name Seth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And the daies of Adam after that he gendride Seth weren maad eiyte hundrid yeer, and he gendride sones and douytris.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
And al the tyme in which Adam lyuede was maad nyne hundrid yeer and thretti, and he was deed.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
Also Seth lyuede an hundrid and fyue yeer, and gendride Enos.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Seth lyuede aftir that he gendride Enos eiyte hundrid and seuen yeer, and gendride sones and douytris.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
And alle the daies of Seth weren maad nyne hundrid and twelue yeer, and he was deed.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
Forsothe Enos lyuede nynti yeer, and gendride Caynan;
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
aftir whos birthe Enos lyuede eiyte hundrid and fiftene yeer, and gendride sones and douytris.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
And alle the daies of Enos weren maad nyne hundrid and fyue yeer, and he was deed.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
Also Caynan lyuyde seuenti yeer, and gendride Malalehel.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Caynan lyuede after that he gendride Malalehel eiyte hundrid and fourti yeer, and gendride sones and douytris.
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
And alle the dayes of Caynan weren maad nyn hundrid and ten yeer, and he was deed.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
Forsothe Malalehel lyuede sixti yeer and fyue, and gendride Jared.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Malalehel lyuede aftir that he gendride Jared eiyte hundrid and thretti yeer, and gendride sones and douytris.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
And alle the daies of Malalehel weren maad eiyte hundrid nynti and fyue yeer, and he was deed.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
And Jared lyuede an hundrid and two and sixti yeer, and gendride Enoth.
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Jared lyuede aftir that he gendride Enoth eiyte hundrid yeer, and gendride sones and douytris.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
And alle the dayes of Jared weren maad nyn hundrid and twei and sexti yeer, and he was deed.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
Forsothe Enoth lyuede fyue and sixti yeer, and gendride Matusalem.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Enoth yede with God; and Enoth lyuede after that he gendride Matusalem thre hundrid yeer, and gendride sones and douytris.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
And alle the daies of Enoth weren maad thre hundride and fyue and sexti yeer.
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
And Enoth yeed with God, and apperide not afterward, for God took hym awei.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
Also Matusalem lyuede an hundrid and `fourscoor yeer and seuene, and gendride Lameth.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Matusalem lyuede after that he gendride Lameth seuene hundrid and `fourscoor yeer and twei, and gendride sones and douytris.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
And alle the daies of Matusale weren maad nyn hundrid and nyn and sixti yeer, and he was deed.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
Forsothe Lameth lyuede an hundrid and `fourscoor yeer and two, and gendride a sone;
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
and clepide his name Noe, and seide, This man schal comforte vs of the werkis and traueilis of oure hondis, in the loond which the Lord curside.
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Lameth lyuede after that he gendride Noe fyue hundrid `nynti and fyue yeer, and gendride sones and douytris.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
And alle the daies of Lameth weren maad seuene hundrid `thre scoor and seuentene yeer, and he was deed.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
Forsothe Noe whanne he was of fyue hundrid yeer gendride Sem, Cham, and Jafeth.

< Genesis 5 >