< Genesis 5 >

1 Ndondomeko ya mibado ya Adamu ndi iyi: Pamene Mulungu analenga munthu, anamulenga mʼchifaniziro cha Mulungu.
This is the book of the generations of Adam. On the day that God created man, in the likeness of God made he him:
2 Iye analenga mwamuna ndi mkazi. Anawadalitsa ndipo anawatcha “Munthu.”
Male and female created he them; and blessed them, and called their name Adam, on the day when they were created.
3 Pamene Adamu anali ndi zaka 130, anabereka mwana wamwamuna wofanana naye ndipo anamutcha Seti.
And Adam lived a hundred and thirty years, and begat a son in his likeness, after his image; and called his name Sheth.
4 Atabadwa Seti, Adamu anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And the days of Adam after he had begotten Sheth were eight hundred years; and he begat sons and daughters.
5 Zaka zonse za Adamu zinali 930 ndipo anamwalira.
And all the days that Adam lived were nine hundred and thirty years; and he died.
6 Pamene Seti anali ndi zaka 105, anabereka Enosi.
And Sheth lived a hundred and five years, and begat Enosh.
7 Atabadwa Enosi, Seti anakhala ndi moyo zaka zina 807 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Sheth lived after he had begotten Enosh eight hundred and seven years; and he begat sons and daughters.
8 Zaka zonse za Seti zinali 912 ndipo anamwalira.
And all the days of Sheth were nine hundred and twelve years; and he died.
9 Pamene Enosi anali ndi zaka 90, anabereka Kenani.
And Enosh lived ninety years, and begat Kenan.
10 Atabadwa Kenani, Enosi anakhala ndi moyo zaka zina 815 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Enosh lived after he had begotten Kenan eight hundred and fifteen years; and he begat sons and daughters.
11 Zaka zonse za Enosi pamodzi zinali 905 ndipo anamwalira.
And all the days of Enosh were nine hundred and five years; and he died.
12 Pamene Kenani anali ndi zaka 70, anabereka Mahalaleli.
And Kenan lived seventy years, and begat Mahalalel.
13 Atabadwa Mahalaleli, Kenani anakhala ndi moyo zaka zina 840 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Kenan lived after he had begotten Mahalalel eight hundred and forty years; and he begat sons and daughters
14 Zaka zonse za Kenani zinali 910, ndipo anamwalira.
And all the days of Kenan were nine hundred and ten years; and he died.
15 Pamene Mahalaleli anali ndi zaka 65, anabereka Yaredi.
And Mahalalel lived sixty and five years, and begat Jared.
16 Atabadwa Yaredi, Mahalaleli anakhala ndi moyo zaka zina 830 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Mahalalel lived after he had begotten Jared eight hundred and thirty years; and he begat sons and daughters.
17 Zaka zonse za Mahalaleli zinali 895 ndipo anamwalira.
And all the days of Mahalalel were eight hundred ninety and five years; and he died.
18 Pamene Yaredi anali ndi zaka 162, anabereka Enoki.
And Jared lived a hundred sixty and two years, and begat Enoch.
19 Atabadwa Enoki, Yaredi anakhala ndi moyo zaka zina 800 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Jared lived after he had begotten Enoch eight hundred years; and he begat sons and daughters.
20 Zaka zonse za Yaredi zinali 962 ndipo anamwalira.
And all the days of Jared were nine hundred sixty and two years; and he died.
21 Pamene Enoki anali ndi zaka 65, anabereka Metusela.
And Enoch lived sixty and five years, and begat Methushelah.
22 Atabadwa Metusela, Enoki anayenda ndi Mulungu zaka 300 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Enoch walked with God after he had begotten Methushelah three hundred years; and begat sons and daughters.
23 Zaka zonse za Enoki zinali 365.
And all the days of Enoch were three hundred sixty and five years.
24 Enoki anayenda ndi Mulungu; ndipo iye sanaonekenso chifukwa Mulungu anamutenga.
And Enoch walked with God, and he was no more; for God had taken him.
25 Pamene Metusela anali ndi zaka 187, anabereka Lameki.
And Methushelah lived a hundred eighty and seven years and begat Lemech.
26 Ndipo atabadwa Lameki, Metusela anakhala ndi moyo zaka zina 782 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Methushelah lived after he had begotten Lemech seven hundred eighty and two years; and he begat sons and daughters.
27 Zaka zonse za Metusela zinali 969, ndipo anamwalira.
And all the days of Methushelah were nine hundred sixty and nine years; and he died.
28 Pamene Lameki anali ndi zaka 182, anabereka mwana wamwamuna.
And Lemech lived a hundred eighty and two years, and begat a son.
29 Ndipo anamutcha Nowa ndipo anati, “Iyeyu adzatipumulitsa ku ntchito zathu zolemetsazi, zolima nthaka imene Yehova anayitemberera.”
And he called his name Noach, [[Noah, ]] saying, This one shall comfort us concerning our work and the toil of our hands, because of the ground which the Lord hath cursed.
30 Atabadwa Nowa, Lameki anakhala zaka zina 595 ndipo anabereka ana ena aamuna ndi aakazi.
And Lemech lived after he had begotten Noah five hundred ninety and five years; and begat sons and daughters.
31 Zaka zonse za Lameki zinali 777, ndipo kenaka anamwalira.
And all the days of Lemech were seven hundred seventy and seven years; and he died.
32 Pamene Nowa anali ndi zaka 500, anabereka Semu, Hamu ndi Yafeti.
And Noah was five hundred years old, and Noah begat Shem, Ham, and Japheth.

< Genesis 5 >