< Genesis 49 >
1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
І покликав Яків усіх синів своїх та й промовив: Зберіться, а я сповіщу́ вам, що́ вас спіткає напри́кінці днів.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Зійдіться та слухайте ви, сини Якова, і прислу́хайтеся до Ізраїля, вашого батька!
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Руви́ме, — ти мій перворідний, моя міць і поча́ток ти сили моєї, верх вели́чности й верх ти могутности!
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
Ти пі́нився був, як вода, — та не втримаєшся, бо ти увійшов був на ложе свойого отця, і збезчестив його, на постелю мою ти піднявся!
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Симео́н і Леві́й — то брати́, їхня зброя — знаря́ддя насильства.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
Хай до їхньої змови не входить душа моя, і нехай не прилу́читься слава моя до їх зборів, бо вони в своїм гніві люди́ну забили, а в своїй самоволі вола копи́т позбавили...
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
Прокля́тий гнів їхній, бо сильний, та їхня лютість, тяжка́ бо вона! Поділю́ їх я в Якові, і їх розпоро́шу в Ізраїлі!
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
О Юдо, — похва́лять тебе твої браття! Рука твоя — на шиї твоїх ворогів, сини батька твого тобі вкло́няться.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Юда — лев молодий! Ти, мій сину, вертаєшся з здо́бичі: прихиливсь він, поклався як лев й як левиця, — зведе хто його?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
Не віді́йметься бе́рло від Юди, ані в його сте́гон законодавець, аж прийде Примири́тель, що Йому буде по́слух наро́дів.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Він прив'язує до винограду свого молодого осла, а до вибраної виноградини — сина ослиці своєї. Він одежу свою буде прати в вині, а шату свою — в виноградній крові́!
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
Від вина він зробивсь мутноокий, а від молока — білозубий.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Завуло́н буде мешкать над берегом мо́рським, над берегом тим, де стають кораблі, а границя його — до Сидону.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Іссаха́р — то костистий осел, що лежить між кошарами.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
І побачив він спо́кій, що добрий, та землю, що стала приємна, і він нахилив свої плечі, щоб не́сти, і став працювать на податок.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Дан буде судить свій наро́д, як один із Ізра́їльських родів.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Дан буде вуже́м при дорозі, змією отру́йливою при шляху́, що п'я́ти коневі кусає, і його верхіве́ць позад себе впаде.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
Спасіння від Тебе чекаю, о Господи!
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Ґад — на нього юрба нападатиме, та він нападе на їх п'я́ти.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
Аси́р — його хліб буде ситий, і він буде давати присма́ки царські.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Нефтали́м — вільна ланя, він прекрасні слова́ видає.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Йо́сип — вітка родюча, вітка родючая над джерело́м, її віття по муру спина́ється.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
І огірчи́ли його та з луку стріляли, і знена́виділи були стрі́льці його.
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
Та зостався міцним його лук, і стали пружні́ рамена́ його рук, — від рук Сильного Якового, звідти Па́стир, Тверди́ня синів Ізраїлевих.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
Проси ти від Бога, свойого Отця, — і Він допоможе тобі, і проси Всемогутнього — і Він благосло́вить тебе благослове́нням небе́с, що на висоті, благослове́нням безодні, що долі лежить, благослове́ннями перс та утро́би.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
Благослове́ння батька твого стали сильніші від благослове́ння батьків моїх, — аж до пожада́них висот віковічних. Нехай вони бу́дуть на голову Йо́сипову, на ма́ківку вибраного з-поміж братів своїх!
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Веніями́н — хижий вовк: вранці їсть він лови́тву, а на вечір розділює здо́бич“.
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
Оце всі дванадцять племен Ізраїлевих, і те, що́ говорив їм батько їх. І він поблагословив їх, — кожного за благослове́нням його поблагословив їх.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
І він наказав їм, і промовив до них: „Я прилучаюся до своєї рідні... Поховайте мене при батьках моїх у печері, що на полі Ефрона хіттеянина,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
у тій печері, що на полі Махпели, що навпроти Мамре́ в ханаанській землі, яке поле купив був Авраам від Ефрона хіттеянина на володіння для гробу.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
Там поховано Авраама й жінку його Сарру, там поховали Ісака та його жінку Ревеку, і там поховав я Лію.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
Поле й печера, що на нім, то добуток від синів Хета“.
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
І закінчив Яків заповіта синам своїм, і втягнув свої ноги до ліжка, та й спочи́в. І він прилучився до своєї рідні.