< Genesis 49 >

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
Wezwał tedy Jakób synów swoich i rzekł: Zbierzcie się, a oznajmię wam, co ma przyjść na was w ostatnie dni.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Zbierzcie się, i słuchajcie synowie Jakóbowi, a słuchajcie Izraela, ojca waszego.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Ruben pierworodny mój, tyś moc moja, i początek siły mojej, zacny dostojeństwem, i zacny męstwem.
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
Spłyniesz jako woda: nie będziesz zacnym, boś wstąpił na łoże ojca twego, i splugawiłeś łoże moje, i zginęło dostojeństwo twoje.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Symeon i Lewi, bracia, naczynia nieprawości miecze ich.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
W radę ich niechaj nie wchodzi dusza moja, a z zgromadzeniem ich niech się nie jednoczy sława moja; bo w zapalczywości swej zabili męża, a w swej woli wywrócili mur.
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
Przeklęta zapalczywość ich, iż uporna, i gniew ich, iż zatwardziały. Rozdzielę je w Jakóbie, a rozproszę je w Izraelu.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Juda, tyś jest, ciebie chwalić będą bracia twoi; ręka twoja będzie na szyi nieprzyjaciół twoich; kłaniać się tobie będą synowie ojca twego.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Szczenię lwie Juda, od łupu, synu mój, wróciłeś się; skłonił się i położył się jako lew, i jako lwica, a któż go obudzi?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
Nie będzie odjęte sceptrum od Judy, ani Zakonodawca od nóg jego, aż przyjdzie Szylo, i jemu będzie oddane posłuszeństwo narodów.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Uwiąże u winnej macicy oślę swe, a u wybornej macicy winnej oślątko oślicy swej; omyje w winie szatę swoję, a we krwi jagód winnych odzienie swoje
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
Czerwieńsze oczy jego nad wino, a bielsze zęby jego nad mleko.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Zabulon na brzegu morskim mieszkać będzie, i przy porcie okrętów, a granice jego aż do Sydonu.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Isaszar jako osieł kościsty, leżący między dwoma brzemiony.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
Upatrzył pokój, że jest dobry, i ziemię, że piękna, nachylił ramię swe ku noszeniu, dla tegoż będzie hołd dawał.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan sądzić będzie lud swój, jako jedno z pokoleń Izraelskich.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Dan będzie wężem na drodze, żmiją na ścieżce, kąsając pięty końskie, że spadnie nazad jeździec jego.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
Zbawienia twego oczekiwam, Panie!
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Gad od wojska zwyciężony będzie; ale i on potem zwycięży.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
Z Asera tłusty chleb jego, a on wyda rozkoszy królewskie.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Neftali jako łani wypuszczona, mówiąc piękne słowa.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Latorośl płodna Józef, latorośl wyrastająca nad źródłem, a latorośli jego rozchodzą się po murze.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
Acz gorzkością napełnili go, i strzelali nań, a nienawidzili go strzelcy.
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
Jednak został potężny łuk jego, a zmocniły się ramiona rąk jego, w rękach mocnego Boga Jakóbowego, stąd się stał pasterzem i opoką Izraelową.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
Od Boga ojca twego, który cię wspomógł, i od Wszechmogącego, któryć błogosławił błogosławieństwy niebieskiemi z wysoka, i błogosławieństwy przepaści leżącej głęboko, i błogosławieństwy piersi i żywota.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
Błogosławieństwa ojca twego mocniejsze będą nad błogosławieństwa przodków moich, aż do granic pagórków wiecznych; będą nad głową Józefową, i nad wierzchem głowy odłączonego między bracią swą.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Benjamin jako wilk porywający, rano jeść będzie łup, a wieczór będzie dzielił korzyść.
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
Teć wszystkie są dwanaście pokolenia Izraelskie, i to, co im powiedział ojciec ich, i błogosławił im; każdemu według błogosławieństwa jego błogosławił im.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
A rozkazał im, i rzekł do nich: Ja będę przyłączon do ludu mego; pogrzebcież mię z ojcy moimi w jaskini, która jest na polu Efrona Hetejczyka;
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
W jaskini, która jest na polu Machpela, która jest na przeciwko Mamre w ziemi Chananejskiej, którą kupił Abraham z rolą od Efrona Hetejczyka, w osiadłość grobu.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
Tam pogrzebiono Abrahama, i Sarę, żonę jego; tam pogrzebiono Izaaka, i Rebekę żonę jego; tamem też pogrzebał Liję.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
A kupiono tę rolą i jaskinią, która na niej, od synów Hetowych.
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
Tedy przestawszy Jakób mówić do synów swoich, złożył nogi swe na łoże i umarł, i przyłączon jest do ludu swego.

< Genesis 49 >