< Genesis 49 >

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
Forsothe Jacob clepide hise sones, and seide to hem, Be ye gaderid that Y telle what thingis schulen come to you in the laste daies;
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
be ye gaderid, `and here, ye sones of Jacob, here ye Israel youre fadir.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Ruben, my firste gendrid sone, thou art my strengthe and the bigynnyng of my sorewe; thou ouytist to be the former in yiftis, the more in lordschip;
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
thou art sched out as watir; wexe thou not, for thou stiedist on the bed of thi fader, and defoulidist his bed.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Symeon and Leuy, britheren, fiytynge vessils of wickidnesse;
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
my soule come not in to the councel of hem, and my glorie be not in the congregacioun of hem; for in her woodnesse thei killiden a man, and in her wille thei myneden the wal;
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
curside be the woodnesse of hem, for it is obstynat, and the indignacioun of hem for it is hard; Y schal departe hem in Jacob, and I schal scatere hem in Israel.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Judas, thi britheren schulen preise thee, thin hondis schulen be in the nollis of thin enemyes; the sones of thi fadir schulen worschipe thee.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
`A whelp of lioun `is Judas; my sone thou stiedist to prey; thou restidist, and hast leyn as a lioun, and as a lionesse who schal reise hym?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
The septre schal not be takun awey fro Juda, and a duyk of his hipe, til he come that schal be sent, and he schal be abiding of hethene men;
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
and he schal tye his colt at the vyner, and his femal asse at the vyne; A! my sone, he schal waische his stoole in wyn, and his mentil in the blood of grape;
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
hise iyen ben fairere than wyn, and hise teeth ben whittere than mylk.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Zabulon schal dwelle in the brenk of the see, and in the stondyng of schipis; and schal stretche til to Sydon.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Isachar, a strong asse,
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
liggynge bitwixe termes, seiy reste, that it was good and seiy the lond that it was best, and he vndirsettide his schuldre to bere, and he was maad seruynge to tributis.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan schal deme his puple, as also another lynage in Israel.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Dan be maad a serpent in the weie, and cerastes in the path, and bite the feet of an hors, that the `stiere therof falle bacward; Lord,
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
Y schal abide thin helthe.
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Gad schal be gird, and schal fiyte bifor hym, and he schal be gird bihynde.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
Aser his breed schal be plenteuouse, and he schal yyue delicis to kyngis.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Neptalym schal be an hert sent out, and yyuynge spechis of fairenesse.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Joseph, a sone encreessynge, `a sone encresinge, and fair in biholdyng; douytris runnen aboute on the wal,
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
but hise brithren wraththeden hym, and chidden, and thei hadden dartis, and hadden enuye to hym.
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
His bowe sat in the stronge, and the boondis of his armes, and hondis weren vnboundun bi the hond of the myyti of Jacob; of hym a scheepherd yede out, the stoon of Israel.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
God of thi fadir schal be thin helpere, and Almyyti God schal blesse thee with blessyngis of heuene fro aboue, and with blessyngis of the see liggynge binethe, with blessyngis of tetis, and of wombe;
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
the blessyngis of thi fadir ben coumfortid, the blessyngis of his fadris, til the desire of euerlastynge hillis cam; blessyngis ben maad in the heed of Joseph, and in the nol of Nazarei among his britheren.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Beniamyn, a rauyschynge wolf, schal ete prey eerly, and in the euentid he schal departe spuylis.
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
Alle these weren in twelue kynredis of Israel; her fadir spak these thingys to hem, and blesside hem alle by propre blessyngis,
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
and comaundide hem, and seide, Y am gaderid to my puple, birie ye me with my fadris in the double denne, which is in the lond of Efron Ethei, ayens Manbre,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
in the lond of Canaan, which denne Abraham bouyte with the feeld of Efron Ethei, in to possessioun of sepulcre.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
There thei birieden hym, and Sare his wijf, also Ysaac was biried there with Rebecca his wijf; there also Lia liggith biried.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And whanne the comaundementis weren endid, bi whiche he tauyte the sones, he gaderide hise feet on the bed, and diede, and he was put to his puple.

< Genesis 49 >