< Genesis 49 >
1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
And Jacob called unto his sons, and said: 'Gather yourselves together, that I may tell you that which shall befall you in the end of days.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Assemble yourselves, and hear, ye sons of Jacob; and hearken unto Israel your father.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Reuben, thou art my first-born, my might, and the first-fruits of my strength; the excellency of dignity, and the excellency of power.
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
Unstable as water, have not thou the excellency; because thou wentest up to thy father's bed; then defiledst thou it — he went up to my couch.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Simeon and Levi are brethren; weapons of violence their kinship.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
Let my soul not come into their council; unto their assembly let my glory not be united; for in their anger they slew men, and in their self-will they houghed oxen.
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
Cursed be their anger, for it was fierce, and their wrath, for it was cruel; I will divide them in Jacob, and scatter them in Israel.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Judah, thee shall thy brethren praise; thy hand shall be on the neck of thine enemies; thy father's sons shall bow down before thee.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Judah is a lion's whelp; from the prey, my son, thou art gone up. He stooped down, he couched as a lion, and as a lioness; who shall rouse him up?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
The sceptre shall not depart from Judah, nor the ruler's staff from between his feet, as long as men come to Shiloh; and unto him shall the obedience of the peoples be.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Binding his foal unto the vine, and his ass's colt unto the choice vine; he washeth his garments in wine, and his vesture in the blood of grapes;
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
His eyes shall be red with wine, and his teeth white with milk.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Zebulun shall dwell at the shore of the sea, and he shall be a shore for ships, and his flank shall be upon Zidon.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Issachar is a large-boned ass, couching down between the sheep-folds.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
For he saw a resting-place that it was good, and the land that it was pleasant; and he bowed his shoulder to bear, and became a servant under task-work
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan shall judge his people, as one of the tribes of Israel.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Dan shall be a serpent in the way, a horned snake in the path, that biteth the horse's heels, so that his rider falleth backward.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
I wait for Thy salvation, O Lord.
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Gad, a troop shall troop upon him; but he shall troop upon their heel.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
As for Asher, his bread shall be fat, and he shall yield royal dainties.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Naphtali is a hind let loose: he giveth goodly words.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Joseph is a fruitful vine, a fruitful vine by a fountain; its branches run over the wall.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
The archers have dealt bitterly with him, and shot at him, and hated him;
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
But his bow abode firm, and the arms of his hands were made supple, by the hands of the Mighty One of Jacob, from thence, from the Shepherd, the Stone of Israel,
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
Even by the God of thy father, who shall help thee, and by the Almighty, who shall bless thee, with blessings of heaven above, blessings of the deep that coucheth beneath, blessings of the breasts, and of the womb.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
The blessings of thy father are mighty beyond the blessings of my progenitors unto the utmost bound of the everlasting hills; they shall be on the head of Joseph, and on the crown of the head of the prince among his brethren.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Benjamin is a wolf that raveneth; in the morning he devoureth the prey, and at even he divideth the spoil.'
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
All these are the twelve tribes of Israel, and this is it that their father spoke unto them and blessed them; every one according to his blessing he blessed them.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
And he charged them, and said unto them: 'I am to be gathered unto my people; bury me with my fathers in the cave that is in the field of Ephron the Hittite,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
in the cave that is in the field of Machpelah, which is before Mamre, in the land of Canaan, which Abraham bought with the field from Ephron the Hittite for a possession of a burying-place.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
There they buried Abraham and Sarah his wife; there they buried Isaac and Rebekah his wife; and there I buried Leah.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
The field and the cave that is therein, which was purchased from the children of Heth.'
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And when Jacob made an end of charging his sons, he gathered up his feet into the bed, and expired, and was gathered unto his people.