< Genesis 49 >

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
Then Jacob called his sons, and he said to them: “Gather together, so that I may announce what will happen to you in the last days.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Gather together and listen, O sons of Jacob. Listen to Israel, your father.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Reuben, my firstborn, you are my strength and the beginning of my sorrow: first in gifts, greater in authority.
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
You are being poured out like water, may you not increase. For you climbed onto your father’s bed, and you defiled his resting place.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
The brothers Simeon and Levi: vessels of iniquity waging war.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
Let not my soul go by their counsel, nor my glory be within their meeting. For in their fury they killed a man, and in their self-will they undermined a wall.
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
Cursed be their fury, because it was obstinate, and their indignation, because it was harsh. I will divide them in Jacob, and I will scatter them in Israel.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Judah, your brothers will praise you. Your hand will be at the necks of your enemies; the sons of your father will reverence you.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Judah is a lion’s young. You have gone up to the prey, my son. While resting, you have lain like a lion. And just like a lioness, who would rouse him?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
The scepter from Judah and the leader from his thigh will not be taken away, until he who will be sent arrives, and he will be the expectation of Gentiles.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Tying his young colt to the vineyard, and his donkey, O my son, to the vine, he will wash his robe in wine, and his cloak in the blood of the grape.
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
His eyes are more beautiful than wine, and his teeth whiter than milk.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Zebulun will live at the seashore and by the outpost of ships, reaching as far as Sidon.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Issachar will be a strong donkey, reclining between the borders.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
He saw that rest would be good, and that the land was excellent. And so he bent his shoulder to carry, and he became a servant under tribute.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan will judge his people just like any other tribe in Israel.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Let Dan be a snake in the way, a viper in the path, biting the hooves of horses, so that his rider may fall backward.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
I will wait for your salvation, O Lord.
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Gad, being girded, will fight before him. And he himself will be girded backward.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
Asher: his bread will be fat, and he will provide delicacies to the kings.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Naphtali is a stag sent forth, offering words of eloquent beauty.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Joseph is a growing son, a growing son and stately to behold; the daughters run back and forth on the wall.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
But those who held darts, provoked him, and they contend with him, and they envied him.
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
His bow sits in strength, and the bands of his arms and hands have been let loose by the hands of the mighty one of Jacob. From there he went forth as a pastor, the stone of Israel.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
The God of your father will be your helper, and the Almighty will bless you with the blessings of heaven above, with the blessings of the abyss that lies beneath, with the blessings of the breasts and of the womb.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
The blessings of your father are strengthened by the blessings of his fathers, until the desire of the hills of eternity shall arrive. May they be at the head of Joseph, and at the summit of the Nazarite, among his brothers.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Benjamin is a ravenous wolf, in the morning he will eat the prey, and in the evening he will divide the spoil.”
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
All these are the twelve tribes of Israel. These things their father spoke to them, and he blessed each one with their proper blessings.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
And he instructed them, saying: “I am being gathered to my people. Bury me with my fathers in the double cave, which is in the field of Ephron the Hittite,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
opposite Mamre, in the land of Canaan, which Abraham bought, along with its field, from Ephron the Hittite, as a possession for burial.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
There they buried him, with his wife Sarah.” And there Isaac was buried with his wife Rebekah. There also Leah lies preserved.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
And having finished these commands by which he instructed his sons, he drew his feet onto the bed, and he passed away. And he was gathered to his people.

< Genesis 49 >