< Genesis 49 >

1 Pambuyo pake Yakobo anayitanitsa ana ake aamuna nati: Sonkhanani pamodzi kuti ndikuwuzeni zimene zidzakuchitikireni mʼmasiku a mʼtsogolo.
Og Jakob kaldte ad sine Sønner og sagde: Samler eder, og jeg vil forkynde eder, hvad eder skal vederfares i de sidste Dage.
2 “Bwerani ndipo imvani mawu anga, inu ana a Yakobo; mverani abambo anu Israeli.
Kommer til Hobe og hører, Jakobs Sønner! og hører paa Israel, eders Fader.
3 “Rubeni, ndiwe woyamba kubadwa; mphamvu yanga ndiponso chizindikiro choyamba cha mphamvu zanga, wopambana pa ulemerero ndi mphamvu.
Ruben, du er min førstefødte, min Magt og min første Kraft, ypperlig i Værdighed og ypperlig i Styrke!
4 Wokokoma ngati madzi a chigumula, koma sudzakhalanso wopambana, iwe unagona pa bedi la abambo ako, ndithu unayipitsa bedi la mdzakazi wake.
Du bruser op som Vandet; du skal ikke være ypperlig; thi du besteg din Faders Leje, da besmittede du det; han har besteget min Seng.
5 “Simeoni ndi Levi ndi pachibale pawo, anachitira nkhanza anthu amene anachita nawo pangano.
Simeon og Levi ere Brødre; Volds Vaaben ere deres Sværd.
6 Iwe moyo wanga, usakhale nawo pa misonkhano yawo ya mseri, kapena kugwirizana nawo mʼmabwalo awo, pakuti anapha anthu mu mkwiyo wawo ndipo anapundula ngʼombe zamphongo monga kunawakomera.
Min Sjæl skal ikke komme i deres hemmelige Raad, min Ære skal ikke forenes med deres Forsamling; thi i deres Vrede have de slaget Mænd ihjel, og i deres Egenraadighed have de lemlæstet Oksen.
7 Matemberero awagwere chifukwa cha mkwiyo wawo woopsa chonchi ndi ukali wawo wankhanza choterewu! Ine ndidzawabalalitsa mʼdziko la Yakobo ndi kuwamwaza iwo mʼdziko la Israeli.
Forbandet være deres Vrede, thi den var streng, og deres Hastighed, thi den var haard; jeg vil fordele dem i Jakob og adsprede dem i Israel.
8 “Yuda, ndiwe amene abale ako adzatamanda; dzanja lako lidzagwira pa khosi pa adani ako; abale ako adzakugwadira iwe.
Juda, dig skulle dine Brødre love, din Haand skal være paa dine Fjenders Nakke; for dig skulle din Faders Sønner bøje sig.
9 Yuda ali ngati mwana wa mkango; umabwerera ku malo ako ndi zofunkha, mwana wanga. Monga mkango, amadziwongola ndi kugona pansi, ndipo ngati mkango waukazi, ndani angalimbe mtima kumudzutsa?
Juda er en ung Løve; du opsteg fra Rov, min Søn! han har bøjet sig, han laa som en Løve og som en Løvinde; hvem tør jage ham op?
10 Ndodo yaufumu sidzachoka mwa Yuda, udzawupanirira ulamuliro motero kuti palibe amene adzawuchotse, mpaka mwini wake weniweni atabwera ndipo mitundu yonse ya anthu idzamumvera.
Der skal ikke vige Kongespir fra Juda og ikke Herskerstav fra hans Fødder, førend Silo skal komme, og Folkene skulle hænge ved ham.
11 Ndiye amene amamangirira bulu wake wamkazi kumtengo wa mpesa, ndi mwana wa bulu ku nthambi ya mpesa wabwino. Ndi iye amene amachapa zovala zake mu vinyo; ndi mkanjo wake mu vinyo wofiira ngati magazi.
Han binder sit unge Asen til Vintræet og sin Asenindes Føl til Vinranken; han tor sit Klædebon i Vin, og sin Kjortel i Vindrueblod.
12 Maso ake adzakhala akuda chifukwa cha vinyo, mano ake woyera chifukwa cha mkaka.
Han er rødere i Øjnene end Vin, og hvidere paa Tænderne end Mælk.
13 “Zebuloni adzakhala mʼmphepete mwa nyanja; adzakhala pa dooko la sitima zapamadzi; malire ake adzafika ku Sidoni.
Sebulon skal bo ved Havets Strand, og han skal være ved Skibenes Strand, og hans Side ligger op til Sidon.
14 “Isakara ali ngati bulu wamphamvu wogona pansi pakati pa makola.
Isaskar skal være et knokkelstærkt Asen, som ligger imellem Kvægfoldene.
15 Ataona ubwino wake wa pamalo pake popumira ndi kukongola kwa dziko lake, iye anaweramutsa msana kuti anyamule katundu wake ndipo anasanduka wogwira ntchito ya ukapolo.
Thi han saa, at Hvilen var god, og at Landet var dejligt, og han har bøjet sine Skuldre til at bære og er bleven en skatskyldig Tjener.
16 “Dani adzaweruza mwachilungamo anthu ake monga limodzi mwa mafuko a anthu a mu Israeli.
Dan skal dømme sit Folk, som en af Israels Stammer.
17 Dani adzakhala ngati njoka ya mʼmphepete mwa msewu, songo yokhala mʼnjira imene imaluma chidendene cha kavalo kuti wokwerapoyo agwe chagada.
Dan skal være en Slange paa Vejen, en Hornslange paa Stien, som bider Hestens Hov, saa dens Rytter falder bag af.
18 “Ndikuyembekeza chipulumutso chanu Yehova.
Herre, jeg bier efter din Frelse!
19 “Gadi adzachitidwa chiwembu ndi gulu la amaliwongo, koma iye adzawathamangitsa.
Gad — en Skare skal trænge ind paa ham, men han skal trænge den tilbage.
20 “Dziko la Aseri lidzabereka chakudya chokoma, ndipo iye adzapereka chakudya kwa mafumu.
Fra Aser kommer det fede, som er hans Brød; og han skal give kongelige Lækkerheder.
21 “Nafutali ali ngati mbawala yayikazi yokhala ndi ana okongola kwambiri.
Nafthali er en frit løbende Hind, han, som giver dejlig Tale.
22 “Yosefe ali ngati mtengo wobereka zipatso, mtengo wobereka zipatso pafupi ndi kasupe, nthambi zake zimayanga pa chipupa cha mwala.
Josef er en Kvist paa det frugtbare Træ, en Kvist paa det frugtbare Træ ved Kilden; Grenene gaa op over Muren.
23 Alenje a uta anamuchita chiwembu mwankhanza; anamuthamangitsa ndi mauta awo.
Og Bueskytterne forbitrede ham og skøde og hadede ham.
24 Koma uta wake sunagwedezeke, ndi manja ake amphamvu aja analimbika, chifukwa cha mphamvu za Mulungu Wamphamvu wa Yakobo, chifukwa ali Mʼbusa ndi Thanthwe la Israeli.
Og hans Bue blev dog stærk, og hans Hænders Arme smidige; det kom fra Jakobs mægtiges Hænder, hist fra, fra Hyrden, fra Israels Klippe.
25 Chifukwa cha Mulungu wa makolo ako amene amakuthandiza; chifukwa cha Mulungu Wamphamvu, amene amakudalitsa ndi mvula yochokera kumwamba, ndi madzi otumphuka pansi pa nthaka, ndipo amakudalitsa pokupatsa ana ambiri ndi ngʼombe zambiri.
Fra din Faders Gud — og han hjælpe dig! — og fra den Almægtige — og han velsigne dig! — komme Velsignelser fra Himmelen ovenfra og Velsignelser fra Dybet nedenfra, Brysters og Moderlivs Velsignelser.
26 Madalitso a kholo lako ndi amphamvu kuposa madalitso a mapiri akale oposa zabwino za ku zitunda zamgonagona. Zonse izi zikhale pamutu pa Yosefe, pa mphumi pa wopatulika uja amene anapatulidwa pakati pa abale ake.
Din Faders Velsignelser ere mægtigere end mine Forfædres Velsignelser, indtil de evige Højes Grænser; de skulle komme paa Josefs Hoved og paa hans Isse, som er en Fyrste iblandt sine Brødre.
27 “Benjamini ali ngati mʼmbulu wolusa; umene mmawa umapha ndi kudya zofunkha, ndipo madzulo umagawa zofunkhazo,”
Benjamin skal røve som en Ulv; om Morgenen skal han æde Rov, og om Aftenen skal han uddele Bytte.
28 Onse awa ndi mafuko khumi ndi awiri a Israeli, ndipo zimenezi ndi zomwe abambo awo ananena pamene anawadalitsa, kuwapatsa aliyense madalitso ake womuyenera iye.
Alle disse ere de tolv Israels Stammer; og dette er det, som deres Fader talede til dem, da han velsignede dem, hver efter sin Velsignelse velsignede han dem.
29 Kenaka Yakobo analamula ana ake nati: “Ine ndatsala pangʼono kufa. Tsono mukandiyike pamodzi ndi makolo anga mʼphanga la mʼmunda wa Efroni Mhiti.
Og han befalede dem og sagde til dem: Naar jeg er samlet til mit Folk, da begraver mig hos mine Fædre i den Hule, som er paa Efron den Hethiters Ager,
30 Ili ndi phanga la mʼmunda wa Makipela, pafupi ndi Mamre mʼdziko la Kanaani. Abrahamu anagula phangalo pamodzi ndi munda womwe kwa Efroni Mhiti kuti pakhale manda.
i den Hule, som er paa den Ager Makpela, som er tvært over for Mamre i Kanaans Land, hvilken Ager Abraham købte af Efron den Hethiter til Begravelses Ejendom.
31 Kumeneko kunayikidwa Abrahamu ndi mkazi wake Sara, Isake ndi mkazi wake Rebeka ndipo ndinayikakonso Leya.
Der have de begravet Abraham og Sara, hans Hustru; der have de begravet Isak og Rebekka, hans Hustru; og der har jeg begravet Lea.
32 Munda ndi manda amene ali mʼmenemo zinagulidwa kwa Ahiti.”
Den Agers Ejendom og den Hule, som er derpaa, er købt af Heths Børn.
33 Yakobo atamaliza kupereka malangizo kwa ana ake, anabwezera miyendo yake pa bedi, namwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
Der Jakob var kommen til Ende med at byde sine Børn dette, da tog han sine Fødder til sig op paa Sengen og opgav sin Aand og blev samlet til sit Folk.

< Genesis 49 >