< Genesis 48 >

1 Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
Après ces choses, quelqu'un dit à Joseph: « Voici ton père qui est malade. » Il prit avec lui ses deux fils, Manassé et Éphraïm.
2 Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
Quelqu'un en informa Jacob, et dit: « Voici ton fils Joseph qui vient vers toi. » Israël se fortifia, et s'assit sur le lit.
3 Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
Jacob dit à Joseph: « Le Dieu tout-puissant m'est apparu à Luz, au pays de Canaan, et il m'a béni.
4 nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
Il m'a dit: « Voici, je te rendrai fécond, je te multiplierai, je ferai de toi une multitude de peuples, et je donnerai ce pays à ta postérité après toi, comme possession éternelle.
5 “Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
Or, tes deux fils, qui te sont nés au pays d'Égypte avant que je ne vienne vers toi en Égypte, sont à moi; Éphraïm et Manassé, comme Ruben et Siméon, seront à moi.
6 Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
Ta descendance, que tu auras engendrée après eux, sera à toi. Ils seront appelés du nom de leurs frères dans leur héritage.
7 Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
Quant à moi, quand je suis venu de Paddan, Rachel est morte près de moi au pays de Canaan, en chemin, alors qu'il y avait encore de la distance à parcourir jusqu'à Éphrata, et je l'ai enterrée là, sur le chemin d'Éphrata (appelée aussi Bethléem). »
8 Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
Israël vit les fils de Joseph, et dit: « Qui sont ceux-ci? »
9 Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
Joseph dit à son père: « Ce sont mes fils, que Dieu m'a donnés ici. » Il dit: « Amène-les-moi, je te prie, et je les bénirai. »
10 Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
Or les yeux d'Israël s'étaient obscurcis à cause de l'âge, de sorte qu'il ne voyait pas bien. Joseph les fit approcher de lui; il les embrassa et les serra dans ses bras.
11 Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
Israël dit à Joseph: « Je ne pensais pas voir ton visage, et voici que Dieu m'a permis de voir aussi ta descendance. »
12 Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
Joseph les fit sortir d'entre ses genoux, et il se prosterna, le visage tourné vers la terre.
13 Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
Joseph les prit tous deux, Éphraïm dans sa main droite vers la main gauche d`Israël, et Manassé dans sa main gauche vers la main droite d`Israël, et il les fit approcher de lui.
14 Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
Israël étendit sa main droite et la posa sur la tête d'Ephraïm, qui était le plus jeune, et sa main gauche sur la tête de Manassé, guidant sciemment ses mains, car Manassé était le premier-né.
15 Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
Il bénit Joseph, et dit, « Le Dieu devant lequel mes pères Abraham et Isaac ont marché, le Dieu qui m'a nourri toute ma vie jusqu'à aujourd'hui,
16 mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
l'ange qui m'a racheté de tout mal, bénis les gars, et que mon nom soit nommé sur eux, et le nom de mes pères, Abraham et Isaac. Qu'ils deviennent une multitude sur la terre. »
17 Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
Lorsque Joseph vit que son père posait sa main droite sur la tête d'Ephraïm, cela lui déplut. Il leva la main de son père, pour la faire passer de la tête d'Ephraïm à celle de Manassé.
18 nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
Joseph dit à son père: « Pas ainsi, mon père, car c'est le premier-né. Pose ta main droite sur sa tête. »
19 Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
Son père refusa, et dit: « Je le sais, mon fils, je le sais. Lui aussi deviendra un peuple, et lui aussi sera grand. Mais son jeune frère sera plus grand que lui, et sa descendance deviendra une multitude de nations. »
20 Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
Il les bénit ce jour-là, en disant: « Israël bénira en vous, en disant: 'Que Dieu vous fasse comme Ephraïm et comme Manassé'" Il plaça Ephraïm devant Manassé.
21 Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
Israël dit à Joseph: « Voici, je meurs, mais Dieu sera avec toi, et il te ramènera dans le pays de tes pères.
22 Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”
De plus, je t'ai donné une part au-dessus de tes frères, que j'ai arrachée de la main de l'Amoréen avec mon épée et avec mon arc. »

< Genesis 48 >