< Genesis 48 >

1 Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
and to be after [the] word: thing [the] these and to say to/for Joseph behold father your be weak: ill and to take: take [obj] two son: child his with him [obj] Manasseh and [obj] Ephraim
2 Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
and to tell to/for Jacob and to say behold son: child your Joseph to come (in): come to(wards) you and to strengthen: strengthen Israel and to dwell upon [the] bed
3 Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
and to say Jacob to(wards) Joseph God Almighty to see: see to(wards) me in/on/with Luz in/on/with land: country/planet Canaan and to bless [obj] me
4 nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
and to say to(wards) me look! I be fruitful you and to multiply you and to give: make you to/for assembly people and to give: give [obj] [the] land: country/planet [the] this to/for seed: children your after you possession forever: enduring
5 “Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
and now two son: child your [the] to beget to/for you in/on/with land: country/planet Egypt till to come (in): come I to(wards) you Egypt [to] to/for me they(masc.) Ephraim and Manasseh like/as Reuben and Simeon to be to/for me
6 Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
and relatives your which to beget after them to/for you to be upon name brother: male-sibling their to call: call by in/on/with inheritance their
7 Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
and I in/on/with to come (in): come I from Paddan to die upon me Rachel in/on/with land: country/planet Canaan in/on/with way: journey in/on/with still distance land: country/planet to/for to come (in): come Ephrath and to bury her there in/on/with way: journey Ephrath he/she/it Bethlehem Bethlehem
8 Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
and to see: see Israel [obj] son: child Joseph and to say who? these
9 Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
and to say Joseph to(wards) father his son: child my they(masc.) which to give: give to/for me God in/on/with this and to say to take: bring them please to(wards) me and to bless them
10 Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
and eye Israel to honor: dull from old age not be able to/for to see: see and to approach: bring [obj] them to(wards) him and to kiss to/for them and to embrace to/for them
11 Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
and to say Israel to(wards) Joseph to see: see face your not to pray and behold to see: see [obj] me God also [obj] seed: children your
12 Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
and to come out: send Joseph [obj] them from from with knee his and to bow to/for face his land: soil [to]
13 Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
and to take: take Joseph [obj] two their [obj] Ephraim in/on/with right his from left Israel and [obj] Manasseh in/on/with left his from right Israel and to approach: bring to(wards) him
14 Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
and to send: reach Israel [obj] right his and to set: put upon head Ephraim and he/she/it [the] little and [obj] left his upon head Manasseh to cross hands [obj] hand his for Manasseh [the] firstborn
15 Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
and to bless [obj] Joseph and to say [the] God which to go: walk father my to/for face: before his Abraham and Isaac [the] God [the] to pasture [obj] me from still my till [the] day: today [the] this
16 mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
[the] messenger: angel [the] to redeem: redeem [obj] me from all bad: evil to bless [obj] [the] youth and to call: call by in/on/with them name my and name father my Abraham and Isaac and to multiply to/for abundance in/on/with entrails: among [the] land: country/planet
17 Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
and to see: see Joseph for to set: put father his hand right his upon head Ephraim and be evil in/on/with eye: appearance his and to grasp hand father his to/for to turn aside: remove [obj] her from upon head Ephraim upon head Manasseh
18 nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
and to say Joseph to(wards) father his not so father my for this [the] firstborn to set: put right your upon head his
19 Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
and to refuse father his and to say to know son: child my to know also he/she/it to be to/for people and also he/she/it to magnify and but brother: male-sibling his [the] small: young to magnify from him and seed: children his to be fullness [the] nation
20 Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
and to bless them in/on/with day [the] he/she/it to/for to say in/on/with you to bless Israel to/for to say to set: make you God like/as Ephraim and like/as Manasseh and to set: put [obj] Ephraim to/for face: before Manasseh
21 Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
and to say Israel to(wards) Joseph behold I to die and to be God with you and to return: again [obj] you to(wards) land: country/planet father your
22 Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”
and I to give: give to/for you shoulder one upon brother: male-sibling your which to take: take from hand: power [the] Amorite in/on/with sword my and in/on/with bow my

< Genesis 48 >