< Genesis 48 >

1 Patapita kanthawi Yosefe anawuzidwa kuti, “Abambo ako akudwala.” Choncho anatenga ana ake awiri aja Manase ndi Efereimu ndi kupita nawo kwa Yakobo.
And it came to pass after these things, that some one said to Joseph, Behold, thy father is sick; and he took his two sons with him, Menasseh and Ephraim.
2 Yakobo atawuzidwa kuti, “Mwana wanu Yosefe wabwera,” Israeli anadzilimbitsa nadzuka kukhala tsonga pa bedi pake.
And some one told Jacob, and said, Behold, thy son Joseph is coming unto thee; and Israel strengthened himself, and sat upon the bed.
3 Yakobo anati kwa Yosefe, “Mulungu Wamphamvuzonse anandionekera ku Luzi mʼdziko la Kanaani, ndipo anandidalitsa,
And Jacob said unto Joseph, God, the Almighty, appeared unto me at Luz in the land of Canaan, and blessed me,
4 nati kwa ine, ‘Ndidzakupatsa ana ambiri ndipo zidzukulu zako zidzasanduka mitundu yambiri ya anthu. Ndidzapereka dziko ili kwa zidzukulu zako zobwera pambuyo pako kuti likhale lawo mpaka muyaya.’
And he said unto me, Behold, I will make thee fruitful, and multiply thee, and I will make of thee a multitude of people; and I will give this land to thy seed after thee for an everlasting possession.
5 “Tsopano ana ako aamuna awiri amene anabadwa ine ndisanabwere kuno adzakhala ana anga. Efereimu ndi Manase adzakhala anga monga mmene alili Rubeni ndi Simeoni.
And now thy two sons, who were born unto thee in the land of Egypt, before I came unto thee into Egypt, shall be mine; Ephraim and Menasseh shall be unto me as Reuben and Simeon.
6 Koma amene ati adzabadwe pambuyo pa iwowa adzakhala ako ndipo cholowa chawo chidzadziwika ndi mayina a abale awo.
And thy issue, which thou begettest after them, shall be thine, after the name of their brothers shall they be called in their inheritance.
7 Pamene ndimabwerera kuchoka ku Parani, mwachisoni Rakele, amayi ako anamwalira mʼdziko la Kanaani, tikanali mʼnjira, mtunda wokafika ku Efurata ukanalipo. Ndipo ndinawayika kumeneko mʼmphepete mwa msewu wa ku Efurata” (amene ndi Betelehemu).
And as for me, when I came from Padan, Rachel died by me in the land of Canaan on the way, when yet there was some distance to come unto Ephrath: and I buried her there on the way of Ephrath, the same is Beth-lechem.
8 Israeli ataona ana a Yosefe anafunsa kuti, “Anyamatawa ndi a yani?”
And Israel perceived the sons of Joseph, and said, Who are these?
9 Yosefe anati kwa abambo ake, “Awa ndi ana anga amene Mulungu wandipatsa kuno.” Ndipo Israeli anati, “Bwera nawo kuno kuti ndiwadalitse.”
And Joseph said unto his father, They are my sons, whom God hath given me in this place. And he said, Bring them, I pray thee, unto me, and I will bless them.
10 Koma maso a Israeli anali ofowoka chifukwa cha kukalamba moti sankaona nʼkomwe. Tsono Yosefe anabwera nawo ana ake aja pafupi ndi abambo ake ndipo abambo ake anawapsompsona nawakumbatira.
Now the eyes of Israel were dim through age, he could not see; and he brought them near unto him, and he kissed them, and embraced them.
11 Israeli anati kwa Yosefe, “Ine sindinali kuyembekeza kuti nʼkudzaonanso nkhope yako, ndipo tsopano Mulungu wandilola kuti ndionenso ngakhale ana ako.”
And Israel said unto Joseph, To see thy face I had not hoped; and lo, God hath shown me also thy seed.
12 Tsono Yosefe anawachotsa ana aja pa mawondo a Israeli ndipo anamuweramira nkhope pansi.
And Joseph brought them out from between his knees, and he bowed himself with his face to the earth.
13 Yosefe anawagwira ana onse awiri padzanja, Efereimu ku dzanja lake lamanja kulunjika dzanja lamanzere la Israeli ndipo Manase ku dzanja lamanzere kulunjikitsa dzanja lamanja la Israeli, ndipo anawayandikiza kwa Yakobo.
And Joseph took them both, Ephraim in his right hand toward Israel's left, and Menasseh in his left hand toward Israel's right, and brought them near unto him.
14 Koma Israeli anapinganitsa mikono motero kuti anayika dzanja lake lamanja pamutu pa Efereimu ngakhale kuti iyeyo anali wamngʼono ndi dzanja lake lakumanzere analisanjika pamutu pa Manase ngakhale kuti iyeyu ndiye anali mwana woyamba.
And Israel stretched out his right hand, and laid it upon Ephraim's head, who was the younger, and his left hand upon Menasseh's head; he laid his hands wittingly; although Menasseh was the first-born.
15 Kenaka anadalitsa Yosefe nati, “Mulungu amene makolo anga Abrahamu ndi Isake anamutumikira, Mulungu amene wakhala ali mʼbusa wanga moyo wanga wonse kufikira lero,
And he blessed Joseph, and said, The God, before whom my fathers Abraham and Isaac did walk, the God who fed me from my first being unto this day,
16 mngelo amene wandipulumutsa ine ku zovuta zonse, ameneyo adalitse anyamata awa. Kudzera mwa iwowa dzina langa ndi mayina a makolo anga, Abrahamu ndi Isake, adzamveka. Iwowa adzakhala ndi ana ambiri nadzasanduka mtundu waukulu pa dziko lapansi.”
The angel who redeemed me from all evil, bless the lads; and let my name be called on them, and the name of my fathers Abraham and Isaac; and let them grow into a multitude in the midst of the earth.
17 Yosefe ataona kuti abambo ake ayika dzanja lamanja pa Efereimu, sanakondwere. Choncho anagwira dzanja la abambo ake kuti alichotse pamutu pa Efereimu ndi kuliyika pamutu pa Manase,
And when Joseph saw that his father would lay his right hand upon the head of Ephraim, it displeased him: and he took hold of his father's hand, to remove it from the head of Ephraim unto the head of Menasseh.
18 nati kwa abambo ake, “Ayi, abambo anga, uyu ndiye woyamba kubadwa, ikani dzanja lanu lamanja pamutu pake.”
And Joseph said unto his father, Not so, my father; for this is the first-born, put thy right hand upon his head.
19 Koma abambo ake anakana nati, “Ndikudziwa, mwana wanga, ndikudziwa. Adzukulu a iyeyunso adzakhala mtundu waukulu. Komabe mʼbale wake wamngʼonoyu adzakhala wamkulu kuposa iye, ndipo zidzukulu zake zidzakhala mitundu yayikulu ya anthu.”
And his father refused, and said, I know, my son, I know, he also shall become a people, and he also shall be great; but truly his younger brother shall be greater than he, and his seed shall become a multitude of nations.
20 Tsono iye anawadalitsa tsiku limenelo nati, “Aisraeli adzagwiritsa ntchito dzina lanu podalitsa nadzati: Mulungu akudalitseni monga Efereimu ndi Manase.” Choncho anayika Efereimu patsogolo pa Manase.
And he blessed them that day, saying, With thee shall Israel bless, saying, God make thee as Ephraim and Menasseh: and so he set Ephraim before Menasseh.
21 Kenaka Israeli anati kwa Yosefe, “Ine ndatsala pangʼono kufa, koma Mulungu adzakhala ndipo adzakutenganinso kubwerera nanu ku dziko la makolo anu.
And Israel said unto Joseph, Behold, I die; but God will be with you, and bring you again unto the land of your fathers
22 Ndiponso iwe wekha ndikupatsa moposera abale ako, malo woonjezera, Sekemu, malo amene ndinalanda kwa Aamori ndi lupanga ndi uta wanga.”
Moreover I have given unto thee one portion above thy brothers, which I took out of the hand of the Emorite with my sword and with my bow.

< Genesis 48 >