< Genesis 47 >

1 Yosefe anapita kukamuwuza Farao kuti, “Abambo anga, abale anga pamodzi ndi nkhosa, ngʼombe zawo, ndi antchito awo abwera kuchokera ku dziko la Kanaani ndipo tsopano ali ku Goseni.”
Potem je prišel Jožef in povedal faraonu ter rekel: »Moj oče, moji bratje, njihovi tropi, njihove črede in vse, kar imajo, so prišli iz kánaanske dežele. Glej, v gošenski deželi so.«
2 Iye anapita kwa Farao kuja ndi abale ake asanu, kukawaonetsa.
Vzel je nekatere izmed svojih bratov, pet mož in jih predstavil faraonu.
3 Farao anafunsa abale akewo kuti, “Mumagwira ntchito yanji?” Iwo anamuyankha kuti, “Ife, bwana ndife oweta ziweto, monga ankachitira makolo athu.
Faraon je njegovim bratom rekel: »Kakšen je vaš poklic?« Faraonu so odgovorili: »Tvoji služabniki so pastirji, tako mi, kakor tudi naši očetje.«
4 Ife tabwera kudzakhala kuno kwa kanthawi chifukwa njala yafika poopsa ku Kanaani motero kuti kulibe msipu wodyetsera ziweto. Ndiye bwana tiloleni kuti tikhale ku Goseni.”
Poleg tega so faraonu rekli: »Zato smo prišli, da začasno prebivamo v deželi, kajti tvoji služabniki nimajo pašnika za svoje trope, kajti huda lakota je v kánaanski deželi. Sedaj te torej prosimo, naj tvoji služabniki prebivajo v gošenski deželi.«
5 Farao anati kwa Yosefe, “Abambo ako ndi abale ako abwera kwa iwe.
Faraon je Jožefu spregovoril, rekoč: »Tvoj oče in tvoji bratje so prišli k tebi.
6 Dziko lonse la Igupto lili mʼdzanja lako. Uwakhazike abambo ako ndi abale ako mʼmalo achonde kwambiri. Akhale ku Goseni. Ndipo ngati ukudziwapo ena mwa iwo amene ali akatswiri pa kuweta ziweto, uwapatse udindo woyangʼanira ziweto zanga.”
Egiptovska dežela je pred teboj. V najboljši deželi pripravi svojemu očetu in bratom, da prebivajo. V gošenski deželi naj prebivajo in če poznaš med njimi katerekoli marljive ljudi, potem jih naredi gospodarje nad mojo živino.«
7 Kenaka Yosefe anapita ndi abambo ake kwa Farao kukawaonetsa, ndipo Yakobo anadalitsa Faraoyo.
Jožef je privedel svojega očeta Jakoba in ga postavil pred faraona in Jakob je blagoslovil faraona.
8 Atatero, Farao anafunsa Yakobo kuti, “Muli ndi zaka zingati?”
Faraon je Jakobu rekel: »Koliko si star?«
9 Yakobo anayankha kuti, “Zaka za maulendo anga zakwana 130. Zaka za moyo wanga ndi zowerengeka, komanso zakhala zaka za masautso. Zaka za moyo wanga sizingafanane ndi zaka za moyo wa makolo anga.”
Jakob je faraonu rekel: »Dni let mojega popotovanja je sto trideset let. Malo in zli so bili dnevi let mojega življenja in nisem dosegel dni let življenja svojih očetov v dneh njihovega popotovanja.«
10 Atatha kumudalitsa Farao uja, Yakobo anatsanzika nʼkunyamuka.
Jakob je blagoslovil faraona in odšel izpred faraona.
11 Choncho Yosefe anakhazika abambo ake aja ndi abale ake mʼdziko la Igupto. Iye anawapatsa dera la Ramesesi limene linali dziko lachonde kwambiri monga analamulira Farao.
Jožef je namestil svojega očeta in svoje brate ter jim dal posest v egiptovski deželi, v najboljšem delu dežele, v Ramesésovi deželi, kakor je faraon zapovedal.
12 Yosefe anaperekanso chakudya kwa abambo ake, kwa abale ake ndi kwa onse a mʼnyumba ya abambo ake monga mwa chiwerengero cha ana awo.
Jožef je vzdrževal svojega očeta, svoje brate in vso družino svojega očeta s kruhom, glede na njihove družine.
13 Njala inakula kwambiri motero kuti chakudya chinasowa mʼdziko lonse. Anthu a ku Igupto ndi ku Kanaani analefuka nayo njalayo.
In ni bilo kruha v vsej deželi, kajti lakota je bila zelo huda, tako da je egiptovska dežela in vsa kánaanska dežela zaradi lakote slabela.
14 Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse zimene anthu a mu Igupto ndi Kanaani ankapereka pogula tirigu, ndipo anabwera nazo ku nyumba kwa Farao.
Jožef je zbral ves denar, ki se je našel v egiptovski deželi in v kánaanski deželi, za žito, ki so ga kupovali. In Jožef je denar prinesel v faraonovo hišo.
15 Anthu a ku Igupto ndi Kanaani ndalama zitawathera, Aigupto onse anabwera kwa Yosefe nati, “Tipatseni chakudya. Nanga tiferenji pamaso panu? Ndalama zathu zatha.”
Ko pa je v egiptovski deželi in v kánaanski deželi zmanjkalo denarja, so vsi Egipčani prišli k Jožefu in rekli: »Daj nam kruha, kajti zakaj bi umrli v tvoji prisotnosti? Kajti denarja je zmanjkalo.«
16 Ndipo Yosefe anawayankha kuti, “Bwerani ndi ziweto zanu ndipo tidzasinthana ndi chakudya poti mukuti ndalama zanu zatha.”
Jožef je rekel: »Dajte svojo živino in jaz vam bom dal za vašo živino, če je denarja zmanjkalo.«
17 Choncho anthu anabwera ndi ziweto zawo monga akavalo, nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi abulu ndipo Yosefe anawapatsa zakudya.
Svojo živino so privedli k Jožefu in Jožef jim je dal kruha v zameno za konje in za trope in za živino od čred in za osle in to leto jih je nahranil s kruhom za vso njihovo živino.
18 Chitatha chaka chimenecho, anthu anapitanso kwa Yosefe chaka chinacho nati, “Ife sitingakubisireni mbuye wathu kuti ndalama zathu zatithera ndipo ziweto zathu zili ndi inu, palibenso choti nʼkukupatsani mbuye wathu kupatula matupi athu ndi dziko lathu.
Ko je bilo to leto končano, so prišli k njemu drugo leto in mu rekli: » Tega ne bomo skrivali pred mojim gospodom, da je naš denar porabljen. Moj gospod ima tudi naše črede in živino. Sploh ni veliko ostalo v očeh mojega gospoda, razen naših teles in naših zemljišč.
19 Tiferenji ife ndi dziko lathu inu mukuona? Mutipatse chakudya ndipo tidzigulitsa ife ndi minda yathu yomwe. Ife tidzakhala akapolo a Farao. Tipatseni mbewuzo kuti tikhale ndi moyo tisafe ndipo dziko lisachite bwinja.”
Zakaj bi umrli pred tvojimi očmi, tako mi kakor naša dežela? Kupi nas in našo deželo za kruh, pa bomo mi in naša dežela služabniki faraonu. Daj nam seme, da bomo lahko živeli in ne umrli, da dežela ne bo zapuščena.«
20 Choncho Yosefe anamugulira Farao dziko lonse la Igupto. Aliyense mu Igupto anagulitsa munda wake chifukwa njala inakula kwambiri. Dziko lonse linasanduka la Farao,
Jožef je vso egiptovsko deželo kupil za faraona, kajti Egipčani so prodali vsak človek svoje polje, ker je nad njimi prevladala lakota in tako je dežela postala faraonova.
21 ndipo Yosefe anawasandutsa anthu onse kukhala akapolo a Farao, kuchokera ku malire a mbali ina ya Igupto kukafika ku malire a mbali ina ya dzikolo.
Kar se tiče ljudstva, jih je premestil v mesta, od enega konca egiptovskih meja, celo do drugega njegovega konca.
22 Komabe, sanagule minda ya ansembe chifukwa Farao ankawapatsa thandizo lokwanira. Nʼchifukwa chake sanagulitse minda yawo.
Samo zemljišč duhovnikov ni pokupil, kajti duhovniki so imeli od faraona njim določen delež in jedli svoj delež, ki jim ga je faraon dajal, zato svojih zemljišč niso prodali.
23 Yosefe anati kwa anthuwo, “Tsono poti ndakugulani inu ndi minda yanu, kugulira Farao. Nayi mbewu kuti mudzale mʼminda yanu.
Potem je Jožef rekel ljudstvu: »Glejte, danes sem kupil vas in vašo deželo za faraona. Glejte, tukaj je seme za vas in vi boste posejali deželo.
24 Koma podzakolola, mudzapereka gawo limodzi la magawo asanu aliwonse kwa Farao. Magawo anayi enawo adzakhala anu. Zina mudzasunge mbewu ndi zina mudzadye inuyo, mabanja anu ndi ana anu.”
Z donosom se bo zgodilo, da boste peti del dali faraonu, štirje deli pa bodo vaši lastni, za seme polja in za vašo hrano in za tiste iz vaših družin in za hrano za vaše malčke.«
25 Iwo anati, “Mwatipulumutsa potichitira zabwinozi, mbuye wathu, tsono tidzakhala akapolo a Farao.”
Rekli so: »Rešil si naša življenja. Naj najdemo milost v očeh mojega gospoda, mi pa bomo faraonovi služabniki.«
26 Choncho Yosefe anakhazikitsa lamulo limene lilipobe mpaka lero mʼdziko lonse la Igupto kuti limodzi la magawo asanu a zokolola ndi la Farao. Ndi minda ya ansembe yokha imene sinatengedwe kukhala ya Farao.
Jožef je to naredil v egiptovski deželi [za] zakon do današnjega dne, da bo imel faraon peti del, razen dežele duhovnikov, ki ni postala faraonova.
27 Tsono Aisraeli anakhazikika mʼdziko la Igupto ku chigawo cha Goseni. Kumeneko anapeza chuma ndipo anaberekana nachuluka kwambiri.
Izrael je prebival v egiptovski deželi, v pokrajini Gošen in v njej so imeli posesti in rastli ter se silno pomnožili.
28 Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147.
Jakob je v egiptovski deželi živel sedemnajst let. Tako je bila celotna Jakobova starost sto sedeminštirideset let.
29 Nthawi itayandikira yoti Israeli amwalire, anayitanitsa mwana wake Yosefe nati kwa iye, “Ngati ukundikondadi monga abambo ako, ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga ndipo ulonjeze kuti udzaonetsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwako kwa ine kuti sudzayika mtembo wanga kuno ku Igupto.
Približal se je čas, ko je Izrael moral umreti in poklical je svojega sina Jožefa ter mu rekel: »Če sem sedaj našel milost v tvojem pogledu, položi, prosim te, svojo roko pod moje stegno ter z menoj postopaj dobrotljivo in iskreno. Ne pokoplji me, prosim te, v Egiptu,
30 Ine ndikagona pamodzi ndi makolo anga. Choncho ndikadzamwalira udzanditulutse mu Igupto muno ndipo ukayike mtembo wanga kumene anayikidwa makolo anga.” Yosefe anati, “Ndidzachita monga mwanenera.”
temveč hočem ležati s svojimi očeti in ti me boš odnesel iz Egipta in me pokopal na njihovem grobišču.« Rekel je: »Storil bom kakor si rekel.«
31 Yakobo anati, “Lumbira kwa ine.” Yosefe analumbira kwa iye, ndipo Israeli anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
Rekel je: »Prisezi mi.« In prisegel mu je. In Izrael se je priklonil na vzglavju postelje.

< Genesis 47 >