< Genesis 47 >
1 Yosefe anapita kukamuwuza Farao kuti, “Abambo anga, abale anga pamodzi ndi nkhosa, ngʼombe zawo, ndi antchito awo abwera kuchokera ku dziko la Kanaani ndipo tsopano ali ku Goseni.”
And Ioseph wet and tolde Pharao and sayde: my father and my brethern their shepe and their beastes and all that they haue are come out of the lade of Canaan and are in the lande of Gosan.
2 Iye anapita kwa Farao kuja ndi abale ake asanu, kukawaonetsa.
And Ioseph toke a parte of his brethern: euen fyue of them and presented them vnto Pharao.
3 Farao anafunsa abale akewo kuti, “Mumagwira ntchito yanji?” Iwo anamuyankha kuti, “Ife, bwana ndife oweta ziweto, monga ankachitira makolo athu.
And Pharao sayde vnto his brethern: what is youre occupation? And they sayde vnto Pharao: feaders of shepe are thi seruauntes both we ad also oure fathers.
4 Ife tabwera kudzakhala kuno kwa kanthawi chifukwa njala yafika poopsa ku Kanaani motero kuti kulibe msipu wodyetsera ziweto. Ndiye bwana tiloleni kuti tikhale ku Goseni.”
They sayde moreouer vnto Pharao: for to sogcorne in the lande are we come for thy seruauntes haue no pasture for their shepe so sore is the fameshment in the lande of Canaan. Now therfore let thy seruauntes dwell in the lande of Gosan.
5 Farao anati kwa Yosefe, “Abambo ako ndi abale ako abwera kwa iwe.
And Pharao sayde vnto Ioseph: thy father and thy brethren are come vnto the.
6 Dziko lonse la Igupto lili mʼdzanja lako. Uwakhazike abambo ako ndi abale ako mʼmalo achonde kwambiri. Akhale ku Goseni. Ndipo ngati ukudziwapo ena mwa iwo amene ali akatswiri pa kuweta ziweto, uwapatse udindo woyangʼanira ziweto zanga.”
The londe of Egipte is open before the: In the best place of the lande make both thy father and thy brothren dwell: And even in the lond of Gosan let them dwell. Moreouer yf thou knowe any men of actiuyte amonge them make them ruelars ouer my catell.
7 Kenaka Yosefe anapita ndi abambo ake kwa Farao kukawaonetsa, ndipo Yakobo anadalitsa Faraoyo.
And Ioseph brought in Iacob his father and sett him before Pharao And Iacob blessed Pharao.
8 Atatero, Farao anafunsa Yakobo kuti, “Muli ndi zaka zingati?”
And Pharao axed Iacob how old art thou?
9 Yakobo anayankha kuti, “Zaka za maulendo anga zakwana 130. Zaka za moyo wanga ndi zowerengeka, komanso zakhala zaka za masautso. Zaka za moyo wanga sizingafanane ndi zaka za moyo wa makolo anga.”
And Iacob sayde vnto Pharao: the dayes of my pilgremage are an hundred and. xxx. yeres. Few and euell haue the dayes of my lyfe bene and haue not attayned vnto the yeres of the lyfe of my fathers in the dayes of their pilgremages.
10 Atatha kumudalitsa Farao uja, Yakobo anatsanzika nʼkunyamuka.
And Iacob blessed Pharao and went out from him.
11 Choncho Yosefe anakhazika abambo ake aja ndi abale ake mʼdziko la Igupto. Iye anawapatsa dera la Ramesesi limene linali dziko lachonde kwambiri monga analamulira Farao.
And Ioseph prepared dwellinges for his father and his brethern and gaue them possessions in the londe of Egipte in the best of the londe: eue in the lande of Raemses as Pharao commaunded.
12 Yosefe anaperekanso chakudya kwa abambo ake, kwa abale ake ndi kwa onse a mʼnyumba ya abambo ake monga mwa chiwerengero cha ana awo.
And Ioseph made prouysion for his father his brethern and all his fathers housholde as yonge childern are fedd with bread.
13 Njala inakula kwambiri motero kuti chakudya chinasowa mʼdziko lonse. Anthu a ku Igupto ndi ku Kanaani analefuka nayo njalayo.
There was no bread in all the londe for the derth was exceadige sore: so yt ye lode of Egipte and ye lode of Canaan were fameshyd by ye reason of ye derth.
14 Yosefe anasonkhanitsa ndalama zonse zimene anthu a mu Igupto ndi Kanaani ankapereka pogula tirigu, ndipo anabwera nazo ku nyumba kwa Farao.
And Ioseph brought together all ye money yt was founde in yt lade of Egipte and of Canaan for ye corne which they boughte: and he layde vp the money in Pharaos housse.
15 Anthu a ku Igupto ndi Kanaani ndalama zitawathera, Aigupto onse anabwera kwa Yosefe nati, “Tipatseni chakudya. Nanga tiferenji pamaso panu? Ndalama zathu zatha.”
When money fayled in the lade of Egipte and of Canaan all the Egiptians came vnto Ioseph and sayde: geue us sustenaunce: wherfore suffrest thou vs to dye before the for oure money is spent.
16 Ndipo Yosefe anawayankha kuti, “Bwerani ndi ziweto zanu ndipo tidzasinthana ndi chakudya poti mukuti ndalama zanu zatha.”
Then sayde Ioseph: brynge youre catell and I well geue yow for youre catell yf ye be without money.
17 Choncho anthu anabwera ndi ziweto zawo monga akavalo, nkhosa, mbuzi, ngʼombe ndi abulu ndipo Yosefe anawapatsa zakudya.
And they brought their catell vnto Ioseph. And he gaue them bread for horses and shepe and oxen and asses: so he fed them with bread for all their catell that yere.
18 Chitatha chaka chimenecho, anthu anapitanso kwa Yosefe chaka chinacho nati, “Ife sitingakubisireni mbuye wathu kuti ndalama zathu zatithera ndipo ziweto zathu zili ndi inu, palibenso choti nʼkukupatsani mbuye wathu kupatula matupi athu ndi dziko lathu.
When that yere was ended they came vnto him the nexte yere and sayde vnto him: we will not hydest from my lorde how that we haue nether money nor catell for my lorde: there is no moare left for my lorde but euen oure bodies and oure londes.
19 Tiferenji ife ndi dziko lathu inu mukuona? Mutipatse chakudya ndipo tidzigulitsa ife ndi minda yathu yomwe. Ife tidzakhala akapolo a Farao. Tipatseni mbewuzo kuti tikhale ndi moyo tisafe ndipo dziko lisachite bwinja.”
Wherfore latest thou us dye before thyne eyes and the londe to goo to noughte? bye us and oure landes for bread: and let both vs and oure londes be bonde to Pharao. Geue vs seed that we may lyue and not dye and that the londe goo not to wast.
20 Choncho Yosefe anamugulira Farao dziko lonse la Igupto. Aliyense mu Igupto anagulitsa munda wake chifukwa njala inakula kwambiri. Dziko lonse linasanduka la Farao,
And Ioseph boughte all the lande of Egipte for Pharao. For the Egiptians solde euery man his londe because the derth was sore apo them: and so the londe be came Pharaos.
21 ndipo Yosefe anawasandutsa anthu onse kukhala akapolo a Farao, kuchokera ku malire a mbali ina ya Igupto kukafika ku malire a mbali ina ya dzikolo.
And he appoynted the people vnto the cities from one syde of Egipte vnto the other:
22 Komabe, sanagule minda ya ansembe chifukwa Farao ankawapatsa thandizo lokwanira. Nʼchifukwa chake sanagulitse minda yawo.
only the londe of the Prestes bought he not. For there was an ordinauce made by Pharao for ye preastes that they shulde eate that which was appoynted vnto them: which Pharao had geuen them wherfore they solde not their londes.
23 Yosefe anati kwa anthuwo, “Tsono poti ndakugulani inu ndi minda yanu, kugulira Farao. Nayi mbewu kuti mudzale mʼminda yanu.
Then Ioseph sayde vnto the folke: beholde I haue boughte you this daye ad youre landes for Pharao. Take there seed and goo sowe the londe.
24 Koma podzakolola, mudzapereka gawo limodzi la magawo asanu aliwonse kwa Farao. Magawo anayi enawo adzakhala anu. Zina mudzasunge mbewu ndi zina mudzadye inuyo, mabanja anu ndi ana anu.”
And of the encrease ye shall geue the fyfte parte vnto Pharao and. iiij. partes shalbe youre awne for seed to sowe the feld: and for you and them of youre housholdes and for youre childern to eate.
25 Iwo anati, “Mwatipulumutsa potichitira zabwinozi, mbuye wathu, tsono tidzakhala akapolo a Farao.”
And they answered: Thou haste saued oure lyves Let vs fynde grace in the syghte of my lorde and let us be Pharaos servautes.
26 Choncho Yosefe anakhazikitsa lamulo limene lilipobe mpaka lero mʼdziko lonse la Igupto kuti limodzi la magawo asanu a zokolola ndi la Farao. Ndi minda ya ansembe yokha imene sinatengedwe kukhala ya Farao.
And Ioseph made it a lawe ouer the lade of Egipte vnto this daye: that men must geue Pharao the fyfte parte excepte the londe of the preastes only which was not bond vnto Pharao.
27 Tsono Aisraeli anakhazikika mʼdziko la Igupto ku chigawo cha Goseni. Kumeneko anapeza chuma ndipo anaberekana nachuluka kwambiri.
And Israel dwelt in Egipte: euen in the countre of Gosan. And they had their possessions therein and they grewe and multiplyed exceadingly.
28 Yakobo anakhala ku Igupto zaka 17 ndipo zaka za moyo wake zinali 147.
Moreouer Iacob lyued in the lande of Egipte. xvij. yeres so that the hole age of Iacob was an hundred and. xlvij. yere.
29 Nthawi itayandikira yoti Israeli amwalire, anayitanitsa mwana wake Yosefe nati kwa iye, “Ngati ukundikondadi monga abambo ako, ika dzanja lako pansi pa ntchafu yanga ndipo ulonjeze kuti udzaonetsa kukoma mtima ndi kukhulupirika kwako kwa ine kuti sudzayika mtembo wanga kuno ku Igupto.
When the tyme drewe nye that Israel must dye: he sent for his sonne Ioseph and sayde vnto him: Yf I haue founde grace in thy syghte put thy hande vnder my thye and deale mercifully ad truely with me that thou burie me not in Egipte:
30 Ine ndikagona pamodzi ndi makolo anga. Choncho ndikadzamwalira udzanditulutse mu Igupto muno ndipo ukayike mtembo wanga kumene anayikidwa makolo anga.” Yosefe anati, “Ndidzachita monga mwanenera.”
but let me lye by my fathers and carie me out of Egipte and burie me in their buryall. And he answered: I will do as thou hast sayde.
31 Yakobo anati, “Lumbira kwa ine.” Yosefe analumbira kwa iye, ndipo Israeli anapembedza Mulungu atatsamira ndodo yake.
And he sayde: swere vnto me: ad he sware vnto him. And than Israel bowed him vnto the beddes head.