< Genesis 45 >

1 Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
Tedy się Józef nie mógł dalej wstrzymać przed wszystkimi, którzy stali przed nim, i zawołał: Wyprowadźcie wszystkie ode mnie. I nie został nikt przy nim, gdy się dał poznać Józef braci swej.
2 Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
I podniósł głos swój z płaczem; co słyszeli Egipczanie, słyszał też dom Faraonów.
3 Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
I rzekł Józef do braci swej: Jamci jest Józef; a żywże jeszcze ojciec mój? i nie mogli mu bracia jego odpowiedzieć, bo się zlękli oblicza jego.
4 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
Tedy rzekł Józef do braci swej: Przystąpcie, proszę, do mnie; i przystąpili. Zatem rzekł: Jam jest Józef, brat wasz, któregoście sprzedali do Egiptu.
5 Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
Jednak teraz nie frasujcie się, ani trwożcie sobą, żeście mię tu sprzedali; boć dla zachowania żywota waszego posłał mię Bóg przed wami.
6 Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
Bo już dwa lata głodu było na ziemi, a jeszcze pięć lat zostaje, których nie będą orać ani żąć.
7 Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
Posłał mię tedy Bóg przed wami, abym was zachował ostatek na ziemi, a żebym wam dodał żywności na oswobodzenie wielkie.
8 “Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
Teraz tedy nie wyście mię tu posłali, ale Bóg, który mię postanowił ojcem Faraonowym, i panem wszystkiego domu jego, a panującym nad wszystką ziemią Egipską.
9 Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
Spieszcież się, a idźcie do ojca mego, i mówcie do niego: Toć wskazuje syn twój Józef: Uczynił mię Bóg panem wszystkiego Egiptu, przyjedźże do mnie, a nie omieszkaj.
10 Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
I będziesz mieszkał w ziemi Gosen; a będziesz blisko mnie, ty i synowie twoi, i synowie synów twoich, i trzody twoje, i woły twoje, i wszystko, co masz.
11 Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
A będę cię tam żywił; bo jeszcze pięć lat głodu będzie, abyś od niedostatku nie zginął, ty, i dom twój, i wszystko, co masz.
12 “Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
A oto, oczy wasze widzą, i oczy brata mego, Benjamina, że usta moje mówią do was.
13 Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
Oznajmijcie też ojcu memu wszystkę zacność moje w Egipcie, i wszystko coście widzieli; spieszcie się tedy, a przyprowadźcie tu ojca mojego.
14 Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
Zatem padł na szyję Benjamina, brata swego, i płakał; Benjamin też płakał na szyi jego.
15 Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
I pocałowawszy wszystkę bracią swoję, płakał nad nimi; a potem rozmawiali z nim bracia jego.
16 Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
I rozgłoszono tę wieść w domu Faraonowym, mówiąc: Przyjechali bracia Józefowi; i podobało się to w oczach Faraonowych, i w oczach sług jego.
17 Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
Tedy rzekł Farao do Józefa: Powiedz braci swej: Uczyńcie tak: nakładłszy brzemion na bydła wasze, idźcie; a wróćcie się do ziemi Chananejskiej;
18 Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
A wziąwszy ojca waszego, i czeladź waszę, przyjedźcie do mnie; i dam wam dobre miejsce w ziemi Egipskiej, i będziecie używać tłustości ziemi.
19 “Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
I rozkaż im mówiąc: To uczyńcie: weźmijcie sobie z ziemi Egipskiej wozów, dla dziatek waszych i dla żon waszych, a wziąwszy ojca waszego przyjedźcie tu.
20 Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
A oko wasze niech nie żałuje sprzętu waszego, gdyż dobro wszystkiej ziemi Egipskiej wasze będzie.
21 Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
Uczynili tedy tak synowie Izraelowi; i dał im Józef wozy według rozkazania Faraonowego; dał im też żywności na drogę.
22 Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
Dał z onychże wszystkich każdemu odmienne szaty; ale Benjaminowi dał trzy sta srebrników, i pięcioro szat odmiennych.
23 Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
Ojcu też swemu posłał te rzeczy: dziesięć osłów, niosących z najlepszych rzeczy Egipskich, i dziesięć oślic, niosących zboże, i chleb, i żywność ojcu jego na drogę.
24 Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
Puścił tedy bracią swą, i odjechali, a mówił do nich: Nie wadźcie się na drodze.
25 Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
Którzy wyjechawszy z Egiptu przyjechali do ziemi Chananejskiej, do Jakóba ojca swego.
26 Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
I oznajmili mu, mówiąc: Jeszczeć żyw Józef, a onci jest panem nad wszystką ziemią Egipską; i zemdlało serce jego; bo im nie wierzył.
27 Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
Lecz oni powiedzieli mu wszystkie słowa Józefowe, które mówił do nich. A ujrzawszy wozy, które posłał Józef, aby go na nich przywieziono, tedy ożył duch Jakóba, ojca ich.
28 Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”
I rzekł Izrael: Dosyć mam na tem, gdy jeszcze Józef, syn mój, żyje; pójdę a oglądam go, pierwej niż umrę.

< Genesis 45 >