< Genesis 45 >

1 Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
And Ioseph coude no longer refrayne before all them that stode aboute him but commaunded that they shuld goo all out from him and that there shuld be no man with him whyle he vttred him selfe vnto his brethern.
2 Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
And he wepte alowde so that the Egiptians and the house of Pharao herde it.
3 Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
And he sayde vnto his brethern: I am Ioseph: doth my father yet lyue? But his brethern coude not answere him for they were abasshed at his presence.
4 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
And Ioseph sayde vnto his brethern: come nere to me and they came nere. And he sayde: I am Ioseph youre brother whom ye sold in to Egipte.
5 Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
And now be not greued therwith nether let it seme a cruel thinge in youre eyes that ye solde me hither. For God dyd send me before you to saue lyfe.
6 Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
For this is the seconde yere of derth in the lande and fyue moo are behynde in which there shall nether be earynge nor hervest.
7 Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
Wherfore God sent me before you to make prouision that ye myghte continue in the erth and to save youre lyues by a greate delyuerance.
8 “Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
So now it was not ye that sent me hither but God: and he hath made me father vnto Pharao and lorde ouer all his house and rueler in all the land of Egipte.
9 Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
Hast you ad goo to my father and tell him this sayeth thy sonne Ioseph: God hath made me lorde ouer all Egipte. Come downe vnto me and tarye not
10 Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
And thou shalt dwell in the londe of Gosan and be by me: both thou and thi childern and thi childerns childern: and thy shepe and beestes and all that thou hast.
11 Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
There will I make provision for the: for there remayne yet v yeres of derth lest thou and thi houshold and all that thou hast perish.
12 “Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
Beholde youre eyes do se and the eyes also of my brother Ben Iamin that I speake to you by mouth.
13 Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
Therfore tell my father of all my honoure which I haue in Egipte and of all that ye haue sene ad make hast and brynge in father hither.
14 Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
And he fell on his brother Ben Iamis necke and wepte and Ben Iamin wepte on his necke.
15 Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
Moreouer he fylled all his brethern and wepte apon them. And after that his brethern talked with him.
16 Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
And when the tidynges was come vnto Pharaos housse that Iosephes brethern were come it pleased Pharao well and all his seruauntes.
17 Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
And Pharao spake vnto Ioseph: saye vnto thy brethern this do ye: lade youre beestes ad get you hence And when ye be come vnto the londe of Canaan
18 Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
take youre father and youre housholdes and come vnto me and I will geue you the beste of the lande of Egipte and ye shall eate the fatt of the londe.
19 “Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
And commaunded also. This do ye: take charettes with you out of the lande of Egipte for youre childern and for youre wyues: and brynge youre father and come.
20 Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
Also regarde not youre stuff for the goodes of all the londe of Egipte shalbe youres.
21 Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
And the childern of Israell dyd euen so And Ioseph gaue them charettes at the commaundment of Pharao and gaue them vitayle also to spende by the waye.
22 Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
And he gaue vnto eche of them chaunge of rayment: but vnto Ben Iamin he gaue. iij. hundred peces of syluer and. v. chaunge of rayment.
23 Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
And vnto his father he sent after the same maner: x. he asses laden with good out of Egipte and. x. she asses laden with corne bred and meate: to serue his father by the waye.
24 Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
So sent he his brethern awaye and they departed. And he sayde vnto them: se that ye fall nor out by the waye.
25 Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
And they departed from Egipte and came in to the land of Canaan vnto Iacob their father and told him saynge.
26 Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
Ioseph is yet a lyue and is gouerner ouer all the land of Egipte. And Iacobs hert wauered for he beleued tho not.
27 Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
And they tolde him all the wordes of Ioseph which he had sayde vnto them. But when he sawe the charettes which Ioseph had sent to carie him then his sprites reviued.
28 Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”
And Israel sayde. I haue ynough yf Ioseph my sonne be yet alyue: I will goo and se him yer that I dye.

< Genesis 45 >