< Genesis 45 >
1 Tsono Yosefe sanathenso kuwugwira mtima kuti asalire pamaso pa antchito ake ndipo anafuwula kuti, “Aliyense achoke pamaso panga!” Motero panalibe wina aliyense pamene Yosefe anadziwulula kwa abale ake.
and not be able Joseph to/for to refrain to/for all [the] to stand upon him and to call: call out to come out: come all man from upon me and not to stand: stand man: anyone with him in/on/with to know Joseph to(wards) brother: male-sibling his
2 Ndipo analira mokweza mwakuti Aigupto anamva. Onse a ku nyumba kwa Farao anamvanso za zimenezi.
and to give: cry out [obj] voice his in/on/with weeping and to hear: hear Egyptian and to hear: hear house: household Pharaoh
3 Yosefe anati kwa abale ake, “Ine ndine Yosefe! Kodi abambo anga akanali ndi moyo?” Koma abale ake sanathe kumuyankha chifukwa anali ndi mantha kwambiri pamaso pake.
and to say Joseph to(wards) brother: male-sibling his I Joseph still father my alive and not be able brother: male-sibling his to/for to answer [obj] him for to dismay from face his
4 Ndipo Yosefe anati kwa abale ake, “Senderani pafupi nane.” Atasendera iye anati, “Ine ndine mʼbale wanu Yosefe amene munamugulitsa ku Igupto!
and to say Joseph to(wards) brother: male-sibling his to approach: approach please to(wards) me and to approach: approach and to say I Joseph brother: male-sibling your which to sell [obj] me Egypt [to]
5 Ndipo tsopano, musawawidwe mtima kapena kudzipsera mtima chifukwa choti munandigulitsa ine kuno, popeza Mulungu ananditsogoza ine kuti adzapulumutse miyoyo yanu.
and now not to hurt and not to be incensed in/on/with eye: appearance your for to sell [obj] me here/thus for to/for recovery to send: depart me God to/for face: before your
6 Kwa zaka ziwiri tsopano, kwakhala kuli njala mʼdziko muno, ndipo kwa zaka zisanu zikubwerazi, anthu sadzalima kapena kukolola.
for this year [the] famine in/on/with entrails: among [the] land: country/planet and still five year which nothing plowing and harvest
7 Koma Mulungu ananditsogoza kuti adzakusungeni ndi moyo ndi kuti mudzakhale ndi zidzukulu pa dziko lapansi.
and to send: depart me God to/for face: before your to/for to set: put to/for you remnant in/on/with land: country/planet and to/for to live to/for you to/for survivor great: large
8 “Motero, si inu amene munanditumiza kuno koma Mulungu. Iye anandisandutsa kukhala nduna yayikulu ya Farao, ndipo zonse za mʼnyumba mwake zili mʼmanja mwangamu. Komanso amene akulamulira dziko lonse la Igupto ndi ine.
and now not you(m. p.) to send: depart [obj] me here/thus for [the] God and to set: make me to/for father to/for Pharaoh and to/for lord to/for all house: household his and to rule in/on/with all land: country/planet Egypt
9 Tsono fulumirani mubwerere kwa abambo anga ndi kuwawuza kuti, ‘Mwana wanu Yosefe akuti, Mulungu anandisandutsa kukhala mbuye wa dziko lonse la Igupto. Ndiye bwerani kuno musachedwe.
to hasten and to ascend: rise to(wards) father my and to say to(wards) him thus to say son: child your Joseph to set: make me God to/for lord to/for all Egypt to go down [emph?] to(wards) me not to stand: stand
10 Ndipo inu, ana anu, zidzukulu zanu, pamodzi ndi nkhosa ndi ngʼombe zanu ndi antchito anu amene muli nawo muzidzakhala mʼdziko la Goseni pafupi ndi ine.
and to dwell in/on/with land: country/planet Goshen and to be near to(wards) me you(m. s.) and son: child your and son: child son: child your and flock your and cattle your and all which to/for you
11 Ine ndizidzakupatsani zakudya kumeneko chifukwa zaka zisanu za njala zikubwera ndithu. Kupanda kutero, inu ndi mabanja anu pamodzi ndi anthu anu onse mudzasowa chakudya.’
and to sustain [obj] you there for still five year famine lest to possess: poor you(m. s.) and house: household your and all which to/for you
12 “Tsono inu nonse pamodzi ndi mʼbale wangayu Benjamini, mukuona kuti ndi inedi amene ndikuyankhula nanu.
and behold eye your to see: see and eye brother: male-sibling my Benjamin for lip my [the] to speak: speak to(wards) you
13 Mukawawuze abambo anga kuti ndili pa ulemerero ku dziko la Igupto kuno ndi zonse zimene mwaziona. Tsopano fulumirani kuti mukabwere nawo kuno abambo anga.”
and to tell to/for father my [obj] all glory my in/on/with Egypt and [obj] all which to see: see and to hasten and to go down [obj] father my here/thus
14 Kenaka Yosefe anakhumbatira Benjamini, mngʼono wake uja nayamba kulira. Nayenso Benjamini anayamba kulira atamukumbatira.
and to fall: fall upon neck Benjamin brother: male-sibling his and to weep and Benjamin to weep upon neck his
15 Atatero, Yosefe anapsompsona abale ake onse aja, akulira. Pambuyo pake abale ake aja anacheza ndi Yosefe.
and to kiss to/for all brother: male-sibling his and to weep upon them and after so to speak: speak brother: male-sibling his with him
16 Akunyumba kwa Farao atamva kuti abale ake a Yosefe abwera, Farao pamodzi ndi nduna zake zonse anakondwera.
and [the] voice: message to hear: hear house: household Pharaoh to/for to say to come (in): come brother: male-sibling Joseph and be good in/on/with eye: appearance Pharaoh and in/on/with eye: appearance servant/slave his
17 Farao anati kwa Yosefe, “Uwawuze abale ako kuti, ‘Senzetsani nyama zanu katundu ndi kubwerera ku dziko la Kanaani.
and to say Pharaoh to(wards) Joseph to say to(wards) brother: male-sibling your this to make: do to load [obj] cattle your and to go: went to come (in): come land: country/planet [to] Canaan
18 Mukabwere nawo abambo anu ndi mabanja anu kuno, ndipo ine ndidzakupatsani dera lachonde kwambiri mʼdziko la Igupto. Mudzadya zokoma za mʼdzikoli.’”
and to take: take [obj] father your and [obj] house: household your and to come (in): come to(wards) me and to give: give to/for you [obj] goodness land: country/planet Egypt and to eat [obj] fat [the] land: country/planet
19 “Uwawuzenso kuti, ‘Tengani ngolo zingapo za kuno ku Igupto kuti mukakwezepo ana anu, akazi anu pamodzi ndi abambo ako ndi kubwera nawo kuno.
and you(m. s.) to command this to make: do to take: take to/for you from land: country/planet Egypt cart to/for child your and to/for woman: wife your and to lift: bear [obj] father your and to come (in): come
20 Musadandaule zosiya katundu komweko chifukwa dziko lachonde la kuno ku Igupto lidzakhala lanu.’”
and eye your not to pity upon article/utensil your for goodness all land: country/planet Egypt to/for you he/she/it
21 Choncho ana a Israeli anachita zimenezo. Yosefe anawapatsa ngolo monga Farao analamulira, ndipo anawapatsanso chakudya cha paulendo wawo.
and to make: do so son: child Israel and to give: give to/for them Joseph cart upon lip: word Pharaoh and to give: give to/for them provision to/for way: journey
22 Anaperekanso kwa aliyense zovala zatsopano, koma kwa Benjamini anapereka siliva wolemera pafupifupi makilogalamu anayi ndi zovala zisanu.
to/for all their to give: give to/for man: anyone change mantle and to/for Benjamin to give: give three hundred silver: money and five change mantle
23 Ndipo abambo ake anawatumizira izi: abulu khumi osenza zinthu zabwino kwambiri za ku Igupto, ndi abulu aakazi khumi osenza tirigu, buledi ndi zakudya zina za pa ulendo wake.
and to/for father his to send: depart like/as this ten donkey to lift: bear from goodness Egypt and ten she-ass to lift: bear grain and food: bread and food to/for father his to/for way: journey
24 Kenaka anawalola abale ake aja kuti azipita, ndipo akunyamuka, iye anawawuza kuti, “Osakangana mʼnjira!”
and to send: depart [obj] brother: male-sibling his and to go: went and to say to(wards) them not to tremble in/on/with way: journey
25 Ndipo anachoka ku Igupto nafika kwa abambo awo Yakobo mʼdziko la Kanaani.
and to ascend: rise from Egypt and to come (in): come land: country/planet Canaan to(wards) Jacob father their
26 Iwo anawuza abambo awo kuti, “Yosefe akanali ndi moyo! Ndiponsotu, ndiye akulamulira dziko la Igupto.” Yakobo anangoti kakasi osankhulupirira.
and to tell to/for him to/for to say still Joseph alive and for he/she/it to rule in/on/with all land: country/planet Egypt and be numb heart his for not be faithful to/for them
27 Komabe atamufotokozera zonse zimene Yosefe anawawuza ndipo ataona ngolo zimene Yosefe anatumiza kuti adzakweremo popita ku Igupto, mtima wa Yakobo, abambo awo unatsitsimuka.
and to speak: speak to(wards) him [obj] all word Joseph which to speak: speak to(wards) them and to see: see [obj] [the] cart which to send: depart Joseph to/for to lift: bear [obj] him and to live spirit Jacob father their
28 Ndipo Israeli anati, “Ndatsimikizadi! Mwana wanga Yosefe akanali ndi moyodi. Ndipita ndikamuone ndisanafe.”
and to say Israel many still Joseph son: child my alive to go: went and to see: see him in/on/with before to die