< Genesis 44 >
1 Pambuyo pake Yosefe analamulira wantchito wa mʼnyumba mwake kuti, “Adzazire chakudya anthuwa mʼmatumba mwawo monga mmene anganyamulire, ndipo uwayikire ndalama zawo pakamwa pa matumba awowo.
І наказав він тому, що над домом його, говорячи: „Понаповнюй мішки цих людей їжею, скільки зможуть вони нести. І поклади срібло кожного до отвору мішка його.
2 Tsono uyike chikho changa cha siliva chija, pakamwa pa thumba la wamngʼono kwambiriyu pamodzi ndi ndalama zake za chakudya” Ndipo iye anachita monga Yosefe ananenera.
А чашу мою, чашу срібну, поклади до отвору мішка наймолодшого, та срібло за хліб його“. І зробив той за словом Йо́сиповим, яке він сказав був.
3 Mmawa kutacha anthu aja analoledwa kuti apite ndi abulu awo.
Розвиднилось рано вра́нці, і люди ці були́ відпущені, вони та їхні осли.
4 Atangotuluka mu mzinda muja, koma asanapite patali, Yosefe anati kwa wantchito wake, “Nyamuka atsatire anthu aja msanga. Ndipo ukawapeza, uwafunse kuti, ‘Bwanji mwabwezera zoyipa ndi zabwino?
Вони вийшли з міста, ще не віддалилися, а Йо́сип сказав до того, що над домом його: „Устань, побіжи за тими людьми, і дожени їх, та й скажи їм: „На́що ви заплатили злом за добро?
5 Mwaberanji chikho chimene mbuye wanga amamweramo ndi kugwiritsa ntchito akafuna kuwombeza? Chimene mwachitachi ndi chinthu choyipa.’”
Хіба це не та чаша, що з неї п'є пан мій, і він, ворожачи, ворожить нею? І зле ви зробили, що вчинили таке “.
6 Wantchito uja atawapeza ananena mawu anawuzidwa aja.
І той їх догнав, і сказав їм ті слова.
7 Koma iwo anati kwa iye, “Kodi mbuye wanga mukuneneranji zimenezi? Sizingatheke ndi pangʼono pomwe kuti antchito anufe nʼkuchita zoterozo ayi!
А вони відказали йому: „Нащо пан мій говорить отакі то слова? Далеке рабам твоїм, щоб зробити таку річ.
8 Paja ife pobwera kuchokera ku Kanaani tinatenga ndalama kubwezera zimene tinazipeza mʼmatumba mwathu. Ndiye pali chifukwa chanji kuti tikabe siliva kapena golide mʼnyumba mwa mbuye wanu?
Таж срібло́, що знайшли ми в отворах наших мішків, ми вернули тобі з Краю ханаанського. А як би ми вкрали з дому пана твого срібло чи золото?
9 Ngati wantchito wanu wina pano atapezeka nacho chikhocho, ameneyo aphedwe ndipo ena tonsefe tidzakhala akapolo anu, mbuye wathu.”
У кого із рабів твоїх вона, чаша, буде знайдена, то помре він, а також ми станемо рабами моєму панові“.
10 Iye anati, “Chabwino, tsono zikhale monga mwaneneramu. Komatu aliyense amene angapezeke nacho chikhocho adzakhala kapolo wanga, ndipo ena nonsenu muzipita mwaufulu.”
А той відказав: „Тож тепер, як ви сказали, так нехай буде воно! У кого вона знайдена буде, той стане мені за раба, а ви будете чисті“.
11 Tsono onse anafulumira kutsitsa pansi aliyense thumba lake ndi kulitsekula.
І поспішно поспускали вони кожен свого мішка на землю. І порозв'язували кожен мішка свого.
12 Kenaka anayamba kufufuza, kuyambira pa wamkulu mpaka pa wamngʼono. Ndipo chikhocho chinapezeka mʼthumba mwa Benjamini.
І став він шукати. Розпочав від найстаршого, а скінчив наймолодшим. І знайдена чаша в мішку Веніяминовім!
13 Apo onse anangʼamba zovala zawo ndi chisoni. Ndipo anasenzetsa abulu katundu wawo nabwerera ku mzinda konkuja.
І пороздирали вони свою одіж! І кожен нав'ючив осла свого, і вернулись до міста.
14 Pamene Yuda ndi abale ake ankafika ku nyumba kwa Yosefe nʼkuti Yosefe akanali komweko. Ndipo anadzigwetsa pansi pamaso pake.
І ввійшли Юда й брати його до дому Йосипа, — а він ще був там. І попа́дали вони перед лицем його на землю.
15 Yosefe anafunsa kuti, “Nʼchiyani mwachitachi? Kodi simudziwa kuti munthu ngati ine ndikhoza kuona zinthu mwakuwombeza?”
І сказав до них Йо́сип: „Що́ це за вчинок, що ви зробили? Хіба ви не знали, що справді відгадає такий муж, як я?“
16 Yuda anayankha, “Kodi tinganenenji kwa mbuye wanga? Tinena chiyani? Tingadzilungamitse bwanji? Mulungu waulula kulakwa kwa antchito anu. Ndipo tsopano ndife akapolo a mbuye wanga, ife tonse pamodzi ndi amene wapezeka ndi chikhocho.”
А Юда промовив: „Що́ ми скажемо панові моєму? Що́ будемо говорити? Чим виправдаємось? Бог знайшов провину твоїх рабів! Ось ми раби панові моєму, і ми, і той, що в руці його була знайдена чаша“.
17 Koma Yosefe anati, “Sindingachite choncho ayi! Yekhayo amene wapezeka ndi chikhocho ndi amene akhale kapolo wanga. Ena nonsenu, bwererani kwa abambo anu mu mtendere.”
А Йо́сип відказав: „Дале́ке мені, щоб зробити оце. Чоловік, що в руці його була знайдена чаша, — він буде мені за раба! А ви йдіть із миром до вашого батька“.
18 Ndipo Yuda anamuyandikira iye nati, “Chonde mbuye wanga mulole kapolo wanune ndinene mawu pangʼono kwa mbuye wanga. Musandipsere mtima, kapolo wanune, popeza inu muli ngati Farao yemwe.
І приступив до нього Юда та й промовив: „О мій пане, нехай скаже раб твій слово до ушей пана свого, і нехай не палає гнів твій на раба твого, бо ти такий, як фараон.
19 Mbuye wanga munafunsa akapolo anufe kuti, ‘Kodi muli ndi abambo anu kapena mʼbale wanu?’
Пан мій запитав був рабів своїх, говорячи: „Чи є в вас батько або брат?“
20 Ndipo ife tinayankha, ‘Inde mbuye wathu, ife tili ndi abambo athu wokalamba, ndipo pali mwana wamwamuna wamngʼono amene anabadwa abambo athu atakalamba kale. Mʼbale wake anafa ndipo ndi yekhayo mʼmimba mwa amayi ake amene watsala ndipo abambo ake amamukonda.’
І сказали ми до пана мого: „Є в нас батько старий та мале дитя його старости, а брат його вмер. І позостався він сам у своєї матері, а батько його любить.
21 “Ndipo inu munatiwuza kuti, ‘Mubwere naye kwa ine kuti ndidzamuone ndekha.’
А ти був сказав своїм рабам: „Зведіть до мене його, і нехай я кину свої́м оком на нього“.
22 Ife tinati, ‘Mbuye wathu, mnyamatayo sangasiye abambo ake, akawasiya ndiye kuti abambo akewo adzafa.’
І сказали ми до пана мого: „Не може той хлопець покинути батька свого. А покине він батька свого, то помре той “.
23 Koma inu munatichenjeza kuti, ‘Pokhapokha mutabwera naye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri, simudzandionanso.’
А ти сказав своїм рабам: „Коли не зійде з вами наймолодший ваш брат, не побачите більше лиця мого“.
24 Ndiye pamene tinafika kwa kapolo wanu, abambo athu tinawawuza zonse zimene munanena.
І сталося, коли ми зійшли були до раба твого, до нашого батька, то ми розповіли йому слова мого пана.
25 “Abambo athu anatiwuza kuti, ‘Pitaninso mukagule kachakudya pangʼono.’
А батько наш сказав: „Верніться, купіть нам трохи їжі“.
26 Koma tinati, ‘Sitingathe kupitanso. Sitingapite pokhapokha mngʼono wathuyu apite nafe chifukwa munthu uja anati sitingaonane naye ngati mngʼono wathuyu sakhala nafe.’
А ми відказали: „Не можемо зійти. Коли найменший наш брат буде з нами, то зійдемо ми, бо не можемо бачити лиця того мужа, якщо брат наш наймолодший не буде з нами“.
27 “Koma kapolo wanu, abambo athu anatiwuza kuti, ‘Inu mukudziwa kuti mkazi wanga anandiberekera ana aamuna awiri.
І сказав до нас раб твій, наш батько: „Ви знаєте, що двох була́ породила мені жінка моя.
28 Mmodzi wa iwo anandisiya. Ine ndimati anadyedwa ndi chirombo popeza sindinamuonenso mpaka lero.
Та пішов від мене один, і я сказав: справді, дійсно розшарпаний він. І я не бачив його аж дотепе́р.
29 Tsopano mukanditengeranso uyu, nakaphedwa mu njira ndiye kuti mudzandikankhira ku manda ndi chisoni.’ (Sheol )
А заберете ви також цього від мене, і спіткає його нещастя, то зведете ви сивину мою цим злом до шеолу“. (Sheol )
30 “Tsono ngati tizibwerera kwa mtumiki wanu, abambo athu popanda mnyamatayu, amene moyo wa abambo ake uli pa iyeyu,
А тепер, коли я прийду́ до раба твого, мого батька, а юнака не буде з нами, — а душа його зв'язана з душею тією, —
31 ndipo akakaona kuti mnyamatayu palibe, basi akafa. Ife tidzakhala ngati takankhira abambo athu ku manda ndi chisoni. (Sheol )
То станеться, коли він побачить, що юнака нема, то помре. І зведуть твої раби сивину раба твого, нашого батька, у смутку до шеолу. (Sheol )
32 Ndiponsotu ine ndinadzipereka kwa abambo anga kukhala chikole chotsimikiza kuti mnyamatayu ndidzamuteteza, ndipo ndinati, ‘Ngati sindibwerera naye mnyamatayu kwa inu, ndiye kuti ndidzakhala wochimwira inu abambo anga moyo wanga wonse.’
Бо раб твій поручився за юнака батькові своєму, кажучи: Коли я не приведу́ його до тебе, то згрішу перед батьком свої́м на всі дні!
33 “Tsono, chonde mulole kuti ine kapolo wanu nditsalire kuno kukhala kapolo wa mbuye wathu mʼmalo mwa mnyamatayu. Koma iye apite pamodzi ndi abale akewa.
А тепер нехай же сяде твій раб замість того юнака за раба панові моєму. А юнак нехай іде з своїми братами!
34 Ndingabwerere bwanji kwa abambo anga ngati sindingapite ndi mnyamatayu? Ayi! Sindifuna kukaona tsoka limene lingakagwere abambo anga.”
Бо як я прийду́ до батька свого, а юнака зо мною нема? Щоб не побачити мені того нещастя, що спіткає мого батька“.