< Genesis 43 >

1 Njala inakula kwambiri mʼdzikomo.
La famine sévissait dans le pays.
2 Tsono atatha kudya tirigu yense amene anakatenga ku Igupto, Yakobo anati kwa ana ake aja, “Pitani kuti mukatigulire chakudya china pangʼono.”
Lorsqu'ils eurent épuisé le blé qu'ils avaient apporté d'Égypte, leur père leur dit: « Retournez-y, achetez-nous encore un peu de nourriture. »
3 Koma Yuda anati kwa iye, “Munthu uja anatichenjeza monenetsa kuti, ‘Simudzandionanso ine pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanu.’
Juda lui parla, et dit: « L'homme nous a solennellement avertis, en disant: 'Vous ne verrez pas ma face, à moins que votre frère ne soit avec vous'.
4 Mukalola kuti mngʼono wathuyu apite nafe, ndiye ife tidzapita kukakugulirani chakudya.
Si tu envoies notre frère avec nous, nous descendrons et nous t'achèterons des vivres;
5 Koma mukapanda kumulola, ife sitipita, chifukwa munthuyo anatiwuza kuti, ‘Simudzandionanso pokhapokha mutabwera ndi mngʼono wanuyo.’”
mais si tu ne l'envoies pas, nous ne descendrons pas, car l'homme nous a dit: 'Tu ne verras pas ma face, à moins que ton frère ne soit avec toi'. »
6 Tsono Israeli anafunsa kuti, “Bwanji inu munandiputira mavuto oterewa pomuwuza munthuyo kuti muli ndi mʼbale wanu wina?”
Israël a dit: « Pourquoi m'as-tu traité si mal, en disant à l'homme que tu avais un autre frère? »
7 Iwo anayankha, “Munthuyo ankangofunsafunsa za ife ndi za banja lathu. Iye anatifunsa kuti, ‘Kodi abambo anu akanali ndi moyo? Kodi muli ndi mʼbale wanu wina?’ Ife tinkangoyankha mafunso ake. Ife tikanadziwa bwanji kuti adzanena kuti, ‘Mubwere naye kuno mʼbale wanu’?”
Ils répondirent: « L'homme nous a interrogés directement sur nous-mêmes et sur nos proches, en disant: « Ton père vit-il encore? As-tu un autre frère? Nous avons simplement répondu à ses questions. Pouvions-nous savoir qu'il allait dire: 'Fais descendre ton frère'? »
8 Ndipo Yuda anati kwa Israeli abambo ake, “Muloleni mnyamatayo apite ndi ine, ndipo tinyamuka nthawi yomweyo, kuti ife ndi inu pamodzi ndi ana athu tikhale ndi moyo.
Juda dit à Israël, son père: « Envoie le garçon avec moi, et nous nous lèverons et partirons, afin que nous vivions et ne mourions pas, nous, et toi, et aussi nos petits enfants.
9 Ine ndidzipereka kuti ndikhale chikole cha moyo wa mnyamatayu. Ine ndidzamuteteza. Ngati sindibwera naye ndi kumupereka kwa inu, ndidzakhala wolakwa pamaso panu moyo wanga wonse.
Je serai pour lui une garantie. C'est de ma main que vous le réclamerez. Si je ne vous l'amène pas, si je ne le mets pas devant vous, que j'en porte la responsabilité pour toujours;
10 Mmene zililimu, tikanapanda kuchedwa, bwenzi titapita ndi kubwerako kawiri.”
car si nous n'avions pas tardé, nous serions déjà revenus une seconde fois. »
11 Tsono abambo awo Israeli anawawuza kuti, “Ngati pafunika kutero, ndiye muchite izi: Ikanimo zipatso zabwino kwambiri za dziko lino mʼmatumba mwanu ndi kumutengera munthuyo ngati mphatso. Mumutengere mafuta wopaka pangʼono, uchi pangʼono, mafuta wonunkhiritsa chakudya, mule, mtedza ndi alimoni.
Leur père, Israël, leur dit: « S'il doit en être ainsi, faites ceci: Prenez dans vos sacs des fruits de choix du pays, et descendez un présent pour l'homme, un peu de baume, un peu de miel, des aromates et de la myrrhe, des noix et des amandes;
12 Mutenge ndalama zokwanira. Ndalama zina nʼzokamubwezera zija anakuyikirani mʼmatumba anu zija. Mwina anangolakwitsa.
et prenez dans votre main de l'argent en double, et rapportez l'argent qui est revenu dans la bouche de vos sacs. C'était peut-être un oubli.
13 Mutengeninso mngʼono wanuyu ndi kubwerera kwa munthuyo msanga.
Prends aussi ton frère, lève-toi, et retourne vers l'homme.
14 Ndipo Mulungu Wamphamvuzonse akuchitireni chifundo pamaso pa munthuyo kuti akamulole mʼbale wanu wina uja ndi Benjamini kuti abwerere ndi inu. Kukakhala kulira, ndine wolira basi.”
Que le Dieu tout-puissant te fasse grâce devant cet homme, afin qu'il te relâche ton autre frère et Benjamin. Si je suis privé de mes enfants, je suis privé. »
15 Choncho abale aja anatenga mphatso, ndalama zokwanira ndi Benjamininso. Iwo anafulumira kupita ku Igupto ndipo anakaonekera kwa Yosefe.
Les hommes prirent ce présent, et ils prirent en main l'argent double, ainsi que Benjamin; ils se levèrent, descendirent en Égypte, et se présentèrent devant Joseph.
16 Yosefe ataona Benjamini ali pamodzi ndi abale ake, anati kwa wantchito wa mʼnyumba mwake, “Atengereni anthu awa ku nyumba kwanga, ndipo uphe nyama ndi kukonza bwino chakudya popeza amenewa adya ndi ine masana ano.”
Lorsque Joseph vit Benjamin avec eux, il dit à l'intendant de sa maison: « Fais entrer les hommes dans la maison, égorge une bête et prépare-toi, car les hommes dîneront avec moi à midi. »
17 Wantchitoyo anachita monga momwe Yosefe ananenera, ndipo anawatengera abale aja ku nyumba kwa Yosefe.
L'homme fit ce que Joseph avait ordonné, et l'homme amena les hommes dans la maison de Joseph.
18 Tsono anthu aja anachita mantha ataona kuti akuwatengera ku nyumba kwa Yosefe. Mʼmaganizo awo ankanena kuti, “Atibweretsa kuno chifukwa cha ndalama zija zinabwezeredwa mʼmatumba athu poyamba paja. Ameneyu akufuna kuti atipanikize ndi kutigwira ukapolo natilanda abulu athu.”
Les hommes eurent peur, parce qu'ils avaient été amenés à la maison de Joseph; ils dirent: « C'est à cause de l'argent qui est revenu dans nos sacs la première fois que nous sommes amenés, afin qu'il cherche une occasion contre nous, qu'il nous attaque et qu'il nous saisisse comme esclaves, avec nos ânes. »
19 Choncho atafika pa khomo la nyumba ya Yosefe anamuyandikira wantchito wa Yosefe nayankhula naye kuti,
Ils s'approchèrent de l'intendant de la maison de Joseph, lui parlèrent à la porte de la maison,
20 “Pepani mbuye wathu, ife tinabweranso ulendo woyamba kudzagula chakudya
et dirent: « Oh, mon seigneur, nous sommes en effet descendus la première fois pour acheter de la nourriture.
21 koma titafika pa malo ena kuti tigone, tinatsekula matumba athu ndipo aliyense wa ife anapeza ndalama zake momwe zinalili zili pakamwa pa thumba lake. Ndiye tabwerera nazo.
Lorsque nous sommes arrivés au gîte, nous avons ouvert nos sacs, et voici que l'argent de chacun était dans l'ouverture de son sac, notre argent en plein poids. Nous l'avons rapporté dans notre main.
22 Tabweretsanso ndalama zina kuti tigule chakudya. Sitikudziwa kuti kaya ndani anayika ndalamazo mʼmatumba athu.”
Nous avons descendu d'autre argent dans notre main pour acheter de la nourriture. Nous ne savons pas qui a mis notre argent dans nos sacs. »
23 Koma iye anati, “Mitima yanu ikhale pansi ndipo musachite mantha. Mulungu wanu, Mulungu wa abambo anu, anakuyikirani chumacho mʼmatumba anu. Ine ndinalandira ndalama zanu.” Ndipo anakawatulutsira Simeoni.
Il dit: « La paix soit avec vous. N'ayez pas peur. Votre Dieu, et le Dieu de votre père, vous a donné un trésor dans vos sacs. J'ai reçu votre argent. » Il fit sortir Siméon vers eux.
24 Wantchito uja anawalowetsa anthuwo mʼnyumba ya Yosefe, nawapatsa madzi kuti asambe mapazi awo. Anadyetsanso abulu awo.
L'homme fit entrer les hommes dans la maison de Joseph, leur donna de l'eau et ils se lavèrent les pieds. Il donna du fourrage à leurs ânes.
25 Abale aja anakonzeratu mphatso zawo zija kuti adzapereke kwa Yosefe, popeza anamva kuti Yosefe adzadya komweko masana.
Ils préparèrent le cadeau pour la venue de Joseph à midi, car ils avaient entendu dire qu'ils devaient y manger du pain.
26 Yosefe atafika ku nyumbako, iwo anapereka mphatso zija namuweramira pansi.
Lorsque Joseph rentra chez lui, ils lui apportèrent dans la maison le présent qu'ils avaient en main, et se prosternèrent en terre devant lui.
27 Yosefe anawafunsa za moyo wawo kenaka anati, “Kodi abambo anu wokalamba amene munkandiwuza aja ali bwanji? Ali ndi moyobe?”
Il les interrogea sur leur bien-être et dit: « Votre père se porte-t-il bien, le vieillard dont vous avez parlé? Est-il encore en vie? »
28 Iwo anayankha kuti, “Mtumiki wanu abambo athu akanali ndi moyo ndipo ali bwino.” Ndipo anamugwadira namuweramira pansi.
Ils dirent: « Ton serviteur, notre père, se porte bien. Il est encore en vie. » Ils se prosternèrent humblement.
29 Pomwazamwaza maso Yosefe anaona Benjamini, mʼbale wake weniweni wa bere limodzi, ndipo anafunsa, “Kodi uyu ndiye mʼbale wanu wamngʼono kwambiri amene munkandiwuza uja?” Kenaka anati, “Ambuye akukomere mtima mwana wanga.”
Il leva les yeux et vit Benjamin, son frère, le fils de sa mère, et il dit: « Est-ce là ton plus jeune frère, dont tu m'as parlé? » Il répondit: « Que Dieu te fasse miséricorde, mon fils. »
30 Kenaka Yosefe anafulumira kutuluka chifukwa mtima wake unadzaza ndi chifundo cha mngʼono wake ndipo anafuna kulira. Tsono anakalowa mʼchipinda chakechake nakalira kumeneko.
Joseph se hâta, car son cœur se languissait de son frère, et il chercha un endroit pour pleurer. Il entra dans sa chambre, et y pleura.
31 Atatha kupukuta misozi mʼmaso mwake anatuluka, ndipo modzilimbitsa analamula kuti chakudya chibwere.
Il se lava le visage, et sortit. Il se maîtrisa, et dit: « Servez le repas. »
32 Anamupatsira Yosefe chakudya payekha, abale ake aja pawokha, ndiponso Aigupto amene ankadya pamodzi ndi iye nawonso pawokha. Izi zinali choncho chifukwa Aigupto ankanyansidwa kudya pamodzi ndi Ahebri.
Ils le servirent seuls, eux seuls, et les Égyptiens qui mangèrent avec lui seuls, car les Égyptiens ne mangent pas avec les Hébreux, car c'est une abomination pour les Égyptiens.
33 Abale aja anawakhazika patsogolo pa Yosefe. Iwo anawakhazika monga mwa mabadwidwe awo kuyambira woyamba kubadwa mpaka wotsirizira; ndipo ankangoyangʼanitsitsana modabwa.
Ils s'assirent devant lui, le premier-né selon son droit d'aînesse, et le plus jeune selon sa jeunesse, et les hommes s'étonnaient les uns des autres.
34 Tsono ankawagawira chakudya kuchokera pa tebulo la Yosefe. Koma chakudya cha Benjamini chinkaposa cha ena onsewa kasanu. Motero anadya ndi kumwa mpaka kukhuta, ndipo anasangalala pamodzi ndi Yosefe.
Il leur envoya des parts de devant lui, mais la part de Benjamin était cinq fois plus importante que celle de n'importe lequel des leurs. Ils burent et furent joyeux avec lui.

< Genesis 43 >